< Yeremiya 34 >

1 Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Detta är det ord, som af Herranom skedde till Jeremia, då NebucadNezar, Konungen i Babel, samt med allom sinom här, och med all rike på jordene, som under hans välde voro, och med all folk, örligade mot Jerusalem, och alla dess städer, och sade:
2 “Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
Detta säger Herren Israels Gud: Gack bort, och tala med Zedekia, Juda Konung, och säg till honom: Så säger Herren: Si, jag skall gifva denna staden uti Konungens händer i Babel, och han skall bränna honom upp i eld.
3 Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
Och du skall icke undkomma hans hand, utan varda gripen, och i hans hand gifven, så att du skall se honom med ögonen, och muntliga tala med honom, och till Babel komma.
4 “Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
Så hör dock, du Zedekia, Juda Konung, Herrans ord; detta säger Herren om dig: Du skall icke dö genom svärd;
5 udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
Utan du skall dö i frid; och lika som man hafver bränt öfver dina fäder, de förra Konungar, som för dig varit hafva, så skall man ock bränna öfver dig, och begråta dig: Ack! herre; ty jag hafver det sagt, säger Herren.
6 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
Och Propheten Jeremia talade all dessa, orden till Zedekia, Juda Konung, i Jerusalem;
7 Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
Då Konungens här i Babel allaredo stridde emot Jerusalem, och emot alla qvarlefda Juda städer, nämliga emot Lachis och Aseka; ty desse, såsom de fastaste städer, voro ännu qvarblefne af Juda städer.
8 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
Detta är det ord, som af Herranom skedde till Jeremia, sedan Konung Zedekia ett förbund gjort hade med allo folkena i Jerusalem, till att utropa ett friår;
9 Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
Så att hvar och en skulle gifva sin träl och hvar och en sina trälinno fri, de der Ebreer och Ebreiske voro, att den ene Juden icke skulle vara dens andras träl.
10 Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
Då lydde honom alle Förstarna, och allt folket, som det förbund undergångit hade, att hvar och en skulle gifva sin träl och trälinno fri, och icke mer hålla dem för lifegna, och gåfvo dem lösa.
11 Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
Men något derefter vände de om igen, och togo de trälar och trälinnor åter till sig, som de frigifvit hade, och tvingade dem, att de trälar och trälinnor vara måste.
12 Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
Då skedde Herrans ord till Jeremia af Herranom, och sade:
13 “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
Detta säger Herren, Israels Gud: Jag hafver gjort ett förbund med edra fäder, då jag förde dem utur Egypti land, utu träldomens hus, och sade:
14 ‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
Då sju år förlidne äro, så skall hvar och en låta sin broder, den en Ebreer är, och sig honom sålt, och i sex år tjent hafver, fri och lös; men edra fäder hörde mig intet, och böjde intet sin öron dertill.
15 Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
Så hafven I nu i dag omvändt eder, och gjort det mig väl behagade, att I låten utropa ett friår, hvar och en sinom nästa, och hafven deruppå gjort ett förbund inför mig uti de huse, som efter mitt Namn nämndt är;
16 Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
Men I hafven åter sedan trädt derifrå, och ohelgat mitt Namn, och hvar och en igentagit sin träl och trälinno, de I haden frigifvit, att de skulle vara sine egne, och tvingen dem nu att de edre trälar och trälinnor vara måste.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Derföre säger Herren alltså: I hörden icke mig, att I måtten utropat ett friår, hvar och en sinom broder, och sinom nästa. Si, så ropar jag, säger Herren, eder ett friår ut, till svärd, till pestilentie, till hunger; och skall icke låta eder bliva uti något rike på jordene.
18 Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
Och de som öfverträda mitt förbund, och icke hålla dess förbunds ord, som de för mig gjort hafva, dem skall jag så göra, lika som dem kalfvenom, den de i tu stycke höggo, och emellan båda stycken gingo;
19 Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
Nämliga Juda Förstar, Jerusalems Förstar, de kamererare, Presterna, och allt folket i landena, som emellan stycken af kalfven gångne äro;
20 Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
Och skall gifva dem uti deras fiendars hand, och deras som efter deras lif stå, att deras kroppar skola foglomen under himmelen och djuromen på jordene till spis varda.
21 “Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
Och Zedekia, Juda Konung, och hans Förstar, skall jag gifva uti deras fiendars händer, och i deras som efter deras lif stå, och i Konungens härs händer af Babel, hvilken nu ifrån eder afdragen är.
22 Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”
Ty si, jag vill befalla dem, säger Herren, och skall åter låta dem komma inför denna staden, och de skola strida emot honom, och vinna honom, och uppbränna honom i eld; och jag skall föröda Juda städer, så att der ingen mer bo skall.

< Yeremiya 34 >