< Yeremiya 34 >
1 Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Rijeè koja doðe Jeremiji od Gospoda, kad Navuhodonosor car Vavilonski i sva vojska njegova, i sva carstva zemaljska koja bijahu pod njegovom vlašæu, i svi narodi vojevahu na Jerusalim i na sve gradove njegove, i reèe:
2 “Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
Ovako veli Gospod Bog Izrailjev: idi i kaži Sedekiji caru Judinu i reci mu: ovako veli Gospod: evo, ja æu predati taj grad u ruke caru Vavilonskom, i on æe ga spaliti ognjem.
3 Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
A ti neæeš uteæi iz njegove ruke, nego æeš biti uhvaæen i predan u njegove ruke, i oèi æe se tvoje vidjeti s oèima cara Vavilonskoga i njegova æe usta govoriti s tvojim ustima, i otiæi æeš u Vavilon.
4 “Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
Ali èuj rijeè Gospodnju, Sedekija care Judin; ovako veli Gospod za te: neæeš poginuti od maèa.
5 udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
Nego æeš umrijeti na miru, i kao što pališe ocima tvojima, preðašnjim carevima, koji su bili prije tebe, tako æe paliti i tebi, i naricaæe za tobom: jaoh gospodaru! jer ja rekoh ovo, govori Gospod.
6 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
I kaza Jeremija prorok Sedekiji caru Judinu sve ove rijeèi u Jerusalimu.
7 Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
A vojska cara Vavilonskoga udaraše na Jerusalim i na sve ostale gradove Judine, na Lahis i Aziku, jer ti bjehu ostali tvrdi gradovi izmeðu gradova Judinijeh.
8 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
Rijeè koja doðe Jeremiji od Gospoda kad car Sedekija uèini zavjet sa svijem narodom koji bješe u Jerusalimu da im proglasi slobodu,
9 Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
Da svaki otpusti slobodna roba svojega i robinju svoju, Jevrejina i Jevrejku, da ni u koga ne bude rob Judejac brat njegov.
10 Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
I poslušaše svi knezovi i sav narod, koji prista na zavjet, da svaki otpusti slobodna roba svojega i robinju svoju, da im ne budu više robovi, poslušaše i otpustiše.
11 Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
A poslije opet staše uzimati robove i robinje, koje bijahu otpustili na volju, i nagoniše ih da im budu robovi i robinje.
12 Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
I doðe rijeè Gospodnja Jeremiji od Gospoda govoreæi:
13 “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
Ovako veli Gospod Bog Izrailjev: ja uèinih zavjet s ocima vašim kad vas izvedoh iz zemlje Misirske, iz doma ropskoga, govoreæi:
14 ‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
Kad se svršuje sedma godina, otpuštajte svaki brata svojega Jevrejina koji ti se bude prodao i služio ti šest godina, otpusti ga slobodna od sebe. Ali ne poslušaše me oci vaši niti prignuše uha svojega.
15 Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
I vi se bjeste sada obratili i uèinili što je pravo preda mnom proglasivši slobodu svaki bližnjemu svojemu, uèinivši zavjet preda mnom u domu koji se zove mojim imenom.
16 Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
Ali udariste natrag i pogrdiste ime moje uzevši opet svaki roba svojega i robinju svoju, koje bijaste otpustili slobodne na njihovu volju, i natjeraste ih da vam budu robovi i robinje.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Zato ovako veli Gospod: vi ne poslušaste mene da proglasite slobodu svaki bratu svojemu i bližnjemu svojemu; evo, ja proglašujem slobodu suprot vama, govori Gospod, maèu, pomoru i gladi, i predaæu vas da se potucate po svijem carstvima zemaljskim.
18 Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
I predaæu ljude koji prestupiše moj zavjet, koji ne izvršiše rijeèi zavjeta koji uèiniše preda mnom, rasjekavši tele na dvoje i prošavši izmeðu polovina,
19 Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
Knezove Judine i knezove Jerusalimske, dvorane i sveštenike i sav narod ove zemlje, koji proðoše izmeðu polovina onoga teleta,
20 Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
Predaæu ih u ruke neprijateljima njihovijem i u ruke onima koji traže dušu njihovu, i mrtva æe tijela njihova biti hrana pticama nebeskim i zvijerima zemaljskim.
21 “Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
I Sedekiju cara Judina i knezove njegove predaæu u ruke neprijateljima njihovijem i u ruke onima koji traže dušu njihovu, u ruke vojsci cara Vavilonskoga, koja se vratila od vas.
22 Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”
Evo, ja æu im zapovjediti, veli Gospod, i dovešæu ih opet na ovaj grad, i biæe ga i uzeæe ga i spaliæe ga ognjem; i gradove Judine obratiæu u pustoš da niko neæe stanovati u njima.