< Yeremiya 34 >
1 Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Parole qui fut adressée à Jérémie par le Seigneur, lorsque Nabuchodonosor, roi de Babylone, et toute son armée, et tous les royaumes de la terre qui étaient sous le pouvoir de sa main, et tous les peuples combattaient contre Jérusalem et contre toutes ses villes, disant:
2 “Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
Voici ce que dit le Seigneur, Dieu d’Israël: Va, et parle à Sédécias, roi de Juda; et tu lui diras: Voici ce que dit le Seigneur: Voilà que moi, je livrerai cette cité aux mains du roi de Babylone, et il y mettra le feu.
3 Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
Et toi tu n’échapperas pas à sa main, mais tu seras pris très certainement, et tu seras livré à sa main: et tes yeux verront les yeux du roi de Babylone, et sa bouche parlera à ta bouche, et tu entreras à Babylone.
4 “Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
Cependant écoute la parole du Seigneur, Sédécias, roi de Juda; voici ce que te dit le Seigneur: Tu ne mourras point par le glaive.
5 udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
Mais tu mourras en paix; et comme on a brûlé les corps de tes pères, des rois précédents qui ont été avant toi, ainsi on te brûlera; et malheur, ô prince! criera-t-on sur toi; parce que c’est moi qui ai prononcé cette parole, dit le Seigneur.
6 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
Et Jérémie, le prophète, dit toutes ces paroles à Sédécias, roi de Juda, dans Jérusalem.
7 Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
Et l’armée du roi de Babylone combattait contre Jérusalem, et contre toutes les cités de Juda qui étaient restées, contre Lachis et contre Azécha; car c’étaient les villes fortifiées, qui étaient restées des cités de Juda.
8 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
Parole qui fut adressée à Jérémie par le Seigneur, après que le roi Sédécias eut fait un pacte avec tout le peuple dans Jérusalem, en publiant
9 Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
Que chacun renvoyât libre son serviteur et chacun sa servante, Hébreu et Hébreue, et qu’ils n’exerçassent nullement leur domination sur eux, c’est-à-dire sur un Juif et leur frère.
10 Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
Ils entendirent donc tous les princes et tout le peuple, qui avaient fait pacte que chacun renverrait libre son serviteur et chacun sa servante, et qu’ils n’exerceraient plus de domination sur eux; ils écoutèrent donc et les renvoyèrent.
11 Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
Mais ils changèrent ensuite, et ils reprirent leurs serviteurs et leurs servantes qu’ils avaient renvoyés libres, et les soumirent à la condition de serviteurs et de servantes.
12 Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
Et la parole du Seigneur fut adressée à Jérémie, disant:
13 “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
Voici ce que dit le Seigneur, Dieu d’Israël: Moi, j’ai fait alliance avec vos pères au jour où je les ai retirés de la terre d’Egypte, de la maison de servitude, disant:
14 ‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
Lorsque sept ans seront accomplis, que chacun renvoie son frère Hébreu, qui lui a été vendu; il te servira six ans, puis tu le renverras d’auprès de toi libre; et vos pères ne m’ont point écouté et ils n’ont pas incliné leur oreille.
15 Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
Et vous, vous êtes tournés vers moi aujourd’hui; vous avez fait ce qui était juste à mes yeux, en publiant la liberté chacun pour son ami; et vous avez fait ce pacte en ma présence, dans la maison dans laquelle mon nom a été invoqué sur elle.
16 Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
Et vous êtes revenus sur ce que vous aviez fait, et vous avez profané mon nom; et vous avez repris chacun votre esclave et chacun votre servante, que vous aviez renvoyés afin qu’ils fussent libres, et en leur propre pouvoir, et vous les avez réduits à vous être serviteurs et servantes.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
À cause de cela voici ce que dit le Seigneur: Vous, vous ne m’avez pas écouté pour annoncer la liberté chacun à votre frère et chacun à votre ami; voici que moi, dit le Seigneur, je vous annonce la liberté d’être abandonnés au glaive, à la peste et à la famine; je vous livrerai à la vexation dans tous les royaumes de la terre.
18 Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
Et je traiterai les hommes qui violent mon alliance, et qui n’ont pas observé les paroles du pacte auxquelles ils ont consenti en ma présence, comme le veau qu’ils ont coupé en deux, et entre les parties duquel ils ont passé;
19 Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
Ces hommes sont les princes de Juda, les princes de Jérusalem, les eunuques et les prêtres, et tout le peuple de cette terre, qui ont passé entre les parties du veau;
20 Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
Je les livrerai donc aux mains de leurs ennemis, aux mains de ceux qui cherchent leur âme; et leurs corps morts seront en pâture aux volatiles du ciel et aux bêtes de la terre.
21 “Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
Et Sédécias, roi de Juda, et ses princes, je les livrerai aux mains de leurs ennemis, et aux mains de ceux qui cherchent leurs âmes, et aux mains des armées du roi de Babylone, lesquelles se sont retirées de vous.
22 Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”
Voilà que moi j’ordonne, dit le Seigneur, je les ramènerai dans cette cité, et ils combattront contre elle, et ils la prendront, et ils y mettront le feu; et les cités de Juda, j’en ferai une solitude pour qu’il n’y ait point d’habitant.