< Yeremiya 34 >

1 Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi gulu lake lonse lankhondo, pamodzi ndi maufumu onse a pa dziko lapansi amene ankawalamulira ndiponso anthu a mitundu yonse ankathira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda yonse yozungulira Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Babylon lengpa Nebuchadnezzar chu alengvaipohna gamho’a kon in asepai jouse toh ahung kon in, Jerusalem leh akimvel’a khopi ho douna gal asattai. Hichepet chun Pakaiyin Jeremiah henga hitin aseiye.
2 “Yehova, Mulungu wa Israeli akuti: Pita kwa Zedekiya mfumu ya Yuda ndipo ukamuwuze kuti Yehova akuti mzinda uno ndidzawupereka mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni ndipo adzawutentha ndi moto.
Zedekiah lengpa henga gachenlang hitin gaseiyin; “Pakai Israel Pathen chun aseiye, keiman hiche khopi hi Babylon lengpa khut a kapehdoh ahitai, chule aman meiya agovam ding ahi.
3 Iweyo sudzapulumuka mʼmanja mwake koma udzagwidwa ndithu ndipo adzakupereka mʼmanja mwake. Udzayiona mfumu ya ku Babuloni maso ndi maso ako ndipo udzayankhula nayo pakamwa ndi pakamwa. Ndipo udzapita ku Babuloni.
Chule nangjong ama-a kon’a najamdoh louhel ding, nakimandoh ding chuleh Babylon lengpa toh nakimaito teiding ahi. Chuteng Babylon gam’a sohchanga nakikaimang ding ahi.
4 “Koma iwe Zedekiya mfumu ya Yuda, imva lonjezo ili la Yehova. Izi ndi zimene Yehova akunena za iwe: Sudzaphedwa pa nkhondo;
Amavang, vo Judah lengpa Zedekiah, Pakai thutep hi ngaiyin, Nangma galmun’a nathilou ding ahi, tin Pakaiyin aseiye.
5 udzafera pa mtendere. Monga anthu ankafukiza lubani poyika maliro a makolo ako akale, amene anali mafumu iwe usanalowe ufumu, choncho nawenso podzayika maliro ako adzafukiza lubani ndipo polira azidzati, ‘Kalanga, mbuye wanga!’ Ine mwini ndalonjeza zimenezi, akutero Yehova.”
Nangma lungmong tah a nathiding ahinai. Napu napate leng masaho kibolna banga mihon gimnamtwi ahin hal uva, nathilong a-op diu; Amaho chu nachung a lainatah’a kapdiu, ohe, ilengpau athitai, atidiu ahi, tin Pakaiyin aseiye, ati.
6 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza zonsezi Zedekiya mfumu ya Yuda, mu Yerusalemu.
Hichun Jeremiah themgao pan, Pakai thusei chu Zedekiah lengpa henga agaseitai.
7 Nthawi imeneyi nʼkuti gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni likuthira nkhondo Yerusalemu ndi mizinda ina yotsala ya Yuda, Lakisi ndi Azeka. Imeneyi yokha ndiye inali mizinda yotetezedwa yotsala ya ku Yuda.
Hichepet chun, Babylon lengpa sepaihon Jerusalem leh Judah gamsunga kulpi kikaikhuma kisuse nailou khopi Lachish leh Azekah teni jong chu ahindel khum un gal in asattauvin ahi.
8 Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya. Nthawi imeneyi nʼkuti mfumu Zedekiya atachita pangano ndi anthu onse a mu Yerusalemu kuti alengeze zakuti akapolo awo adzawamasule.
Chuin Zedekiah lengpan agamsung mipite toh kitepna khat asemdoh in; soh’a kivul ho jalen nading thu aphon doh jou chun, Pakaiyin Jeremiah henga hitin ahinseiyin ahi.
9 Aliyense amene anali ndi akapolo a Chihebri, aamuna kapena aakazi awamasule; palibe amene ayenera kusunga mu ukapolo Myuda mnzake.
Aman amitakip henga thupeh aneiyin, Hebrew mi soh’a kivul jouse, numei hihen pasal hijongle, abon’a alha-ong diuvin thupeh aneiyin ahi. Koiman anammi Hebrew mi chu soh a aneithei louhel ding ahi, tin aseitai.
10 Choncho akuluakulu pamodzi ndi anthu onse amene anachita pangano ili anagwirizana kuti amasule akapolo awo aamuna ndi aakazi ndi kuti asawasungenso mu ukapolo. Iwo anachitadi zimenezi ndipo anawamasuladi.
Chuin leng chapaten jong chule mipiten jong, abonchauvin lengpa thupeh chu ajuicheh uvin, asohteu chu abonchauvin achamlhat sah tauve.
11 Koma pambuyo pake anasintha maganizo awo ndi kuwatenganso amuna ndi akazi amene anawamasula aja ndipo anawasandutsanso akapolo.
Ahin khonung in, amahon alung’u akhelkit uvin, alha-ongsau soh numeiho le pasal hochu, abon uvin anung mat kit uvin, soh in aneikittauve.
12 Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti:
Hijeh chun Pakaiyin Jeremiah henga hitin aseitai.
13 “Yehova Mulungu wa Israeli akuti: Ine ndinachita pangano ndi makolo anu pamene ndinawatulutsa ku Igupto, mʼdziko la ukapolo. Ine ndinati,
Pakai Israel Pathen chun hitin aseiye, Keiman napu napateu chu asohchannau Egypt gam’a kon’a kahuh doh chun, amaho toh kitepna khat kana semdoh in ahi.
14 ‘Chaka chachisanu ndi chiwiri chilichonse aliyense wa inu ayenera kumasula mʼbale wake wa Chihebri amene anadzigulitsa yekha kwa inuyo. Iyeyo amasulidwe akagwira ntchito zaka zisanu ndi chimodzi, mumulole apite mwaufulu.’ Komatu makolo anu sanandimvere kapena kusamala konse.
Keiman napu napateu jah’a, kumgup nasoh uva pangsa Hebrew mi poupou, kumgup sehleh nalha-ong uva nachamlhat sah teitei diu ahi, kati. Ahivangin amahon kathusei ho ngai nahsah in aneipouve.
15 Posachedwa pomwepa inu munalapa ndi kuchita zinthu zabwino pamaso panga: Aliyense wa inu anamasula mʼbale wake. Ndipo munachita pangano pamaso panga mʼNyumba imene imadziwika ndi dzina langa kuti mudzachitadi zimenezi.
Tunin nanghon kathupeh bangin lung naheiyun, Israel in nakom’a soh a umho lhadoh dingin nakinopto sohtauve. Nanghon keima houin sung laitah’a, ikihounau bangin kitepna khat nasemtauve.
16 Koma tsopano mwasintha maganizo anu ndipo mwayipitsa dzina langa. Mwatenganso ukapolo aamuna ndi aakazi amene munawamasula aja kuti apite kumene akufuna. Mwawakakamiza kuti akhalebe akapolo anu.
Ahinlah, nanghon lung nakhel kit un, nakitepnau nasukeh uvin, nalhadohsau soh numeiho leh soh pasal ho jouse, nanung mat kit uvin, nasoh uvin napansah kit uvin, kamin chu nasunoh tauvin ahi.
17 “Nʼchifukwa chake Yehova akuti: Inu simunandimvere Ine; simunalengeze kuti abale anu amasulidwe. Chabwino! Ine ndidzakupatsani ufulu; ufulu wake ukhala wophedwa ndi nkhondo, mliri ndi njala. Ndidzakusandutsani chinthu chochititsa mantha pakati pa maufumu onse a dziko lapansi.
Hijeh chun Pakaiyin hitin aseiye, “Nanghon kathupehsa nanam chanpi ho soh’a kon’a nachamlhat sah diu ahi, kati chu najuitapouve. Keiman nangho gal a mangthah ding, kelthoh a genthei ding chule natlesat thigam dinga kalha-ong diu nahitauve. Chutahle vannoiya namtin vaipin natijat pi uva nakidah diu ahi.
18 Inu simunasunge pangano limene munachita ndi Ine. Simunasamale lonjezo limene munachita pamaso panga. Choncho ndidzakusandutsani ngati mwana wangʼombe uja amene ankamudula pawiri napita pakati pa zigawozo.
Nanghon ikitepnau nasukehtauve. Nanghon nakihahsel uva bongnou nahapsat uva, akah’a nakijot bang uva chu, keiman nangho kahapsat ding nahiuve.
19 Amene ankadutsa pakati pa zigawozo anali atsogoleri a Yuda ndi Yerusalemu, akuluakulu a bwalo, ansembe ndi anthu onse a mʼdzikomo.
Keiman nangho kasattel diu, vaipo ho, thempuho chule mipite jouse, bongnou kisattel banga kasattel diu ahi. ajeh chu nanghon nakitepnau nasukehtauve.
20 Onsewa ndidzawapereka kwa adani awo amene akufuna kuwapha. Mitembo yawo idzakhala chakudya cha mbalame zamlengalenga ndi zirombo za dziko lapansi.
Keiman nanghon namelmateu khut a kapehdoh u nahitai. Amahon namat uva nathadiu, chule natahsa uchu gamsaho leh vachaten anehdiu ahi.
21 “Ndidzapereka Zedekiya mfumu ya Yuda ndi nduna zake kwa adani awo amene akufuna kuwapha, kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni limene nthawi ino layamba kubwerera mʼmbuyo.
Keiman Judah lengpa Zedekiah leh avaipote abonchauva, nanghoa kon’a kinungtolsa Babylon lengpa khut a kapehdoh ding ahi.
22 Taonani, Ine ndidzawalamula, akutero Yehova, ndipo ndidzawabweretsanso ku mzinda uno. Adzathira nkhondo mzindawu, kuwulanda ndi kuwutentha. Ndipo Ine ndidzasandutsa chipululu mizinda ya Yuda kotero kuti palibe amene adzakhalemo.”
Keiman Babylon sepaite kalekou kit ding; Amahon hiche khopihi ahin delkhum diu, meiya ahalvam diu ahi. Hitia chu Judah gamsung khopi jouse kasuhmang ding, chule beihel a ahomkeova kakoi ding ahi, ati.

< Yeremiya 34 >