< Yeremiya 33 >
1 Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
Un Tā Kunga vārds notika uz Jeremiju otru reizi, kad viņš vēl bija ieslēgts cietuma pagalmā, sacīdams:
2 “Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
Tā saka Tas Kungs, kas to dara, Tas Kungs, kas to izdara, lai tas notiek - Kungs ir viņa vārds -
3 ‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
Piesauc Mani, tad Es tev atbildēšu un tev darīšu zināmas lielas un brīnišķas lietas, ko tu nezini.
4 Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
Jo tā saka Tas Kungs, Israēla Dievs, par šīs pilsētas namiem un par Jūda ķēniņa namiem, kas tiek nolauzīti vaļņu un zobena priekšā,
5 Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
Par tiem, kas nāk karot pret Kaldejiem, lai tos (namus) pilda ar miroņu miesām, ko Es nokauju Savā bardzībā un Savā dusmībā, un tādēļ ka Es Savu vaigu no šīs pilsētas esmu apslēpis, visa viņu ļaunuma dēļ:
6 “‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
Redzi, Es to sasiešu un dziedināšu, un tos darīšu veselus, un tiem parādīšu pilnīgu un pastāvīgu laimi.
7 Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
Un Es vedīšu atpakaļ Jūda cietumniekus un Israēla cietumniekus, un tos uztaisīšu tā kā papriekš.
8 Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
Un Es tos šķīstīšu no visa viņu nozieguma, ar ko tie pret Mani grēkojuši, un Es tiem piedošu visus viņu pārkāpumus, ar ko tie pret Mani grēkojuši un ar ko tie no Manis atkāpušies.
9 Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
Un tad(Jeruzāleme) Man būs par prieka vārdu, par slavu un par godu pie visām tautām virs zemes, kas dzirdēs visu to labumu, ko Es tiem daru, un tās bīsies un drebēs par visu to labumu un par visu to mieru, ko Es viņai dodu.
10 “Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
Tā saka Tas Kungs: šinī vietā, par ko jūs sakāt, tā ir postaža bez cilvēka un lopa, pa Jūda pilsētām un pa Jeruzālemes ielām, kas ir postītas, ka tur nav ne cilvēka, ne iedzīvotāja, ne lopa,
11 mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
Tur atkal dzirdēs prieka balsi un līksmības balsi, brūtgāna balsi un brūtes balsi, balsi no tiem, kas saka: teiciet To Kungu Cebaot, jo Tas Kungs ir labs, jo Viņa žēlastība paliek mūžīgi, - un kas nes pateicības upuri Tā Kunga namā. Jo Es vedīšu atpakaļ tās zemes cietumniekus kā papriekš, saka Tas Kungs.
12 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
Tā saka Tas Kungs Cebaot: šinī vietā, kas ir postaža bez cilvēka un lopa, un visās apkārtējās pilsētās būs atkal ganu dzīvokļi, kas ganīs ganāmus pulkus.
13 Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
Pa kalnu pilsētām un lejas pilsētām un pa dienvidu(Negebas) pilsētām un Benjamina zemē un ap Jeruzālemi un pa Jūda pilsētām ganāmi pulki atkal ies apakš skaitītāju rokām, saka Tas Kungs.
14 “‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
Redzi, nāks dienas, saka Tas Kungs, ka Es piepildīšu to labo vārdu, ko Es esmu runājis uz Israēla namu un Jūda namu.
15 “‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
Tanīs dienās un tanī laikā Es Dāvidam likšu izplaukt taisnības Zaram, un tas darīs tiesu un taisnību virs zemes.
16 Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
Tanīs dienās Jūda taps atpestīts, un Jeruzāleme dzīvos bez bailēm, un šis ir tas (vārds), ar ko Viņu sauks: Tas Kungs mūsu taisnība.
17 Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
Jo tā saka Tas Kungs: Dāvidam netrūks vīra, kas sēdēs Israēla nama goda krēslā.
18 ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
Arī priesteru, levitu netrūks Manā priekšā, kas upurē dedzināmos upurus un iededzina ēdamus upurus un sataisa kaujamus upurus mūžīgi.
19 Yehova anawuza Yeremiya kuti:
Un Tā Kunga vārds notika uz Jeremiju un sacīja:
20 Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
Tā saka Tas Kungs: ja jūs varat iznīcināt Manu derību ar dienu un Manu derību ar nakti, ka dienas un nakts vairs nav savā laikā,
21 Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
Tad arī iznīks Mana derība ar Manu kalpu Dāvidu, ka tam dēla nebūs, kas valda uz viņa goda krēsla, un (Mana derība) ar levitiem, priesteriem, Maniem kalpotājiem.
22 Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
Tā kā debess pulku nevar skaitīt un jūras smiltis nevar mērot, tāpat Es vairošu Sava kalpa Dāvida dzimumu un levitus, kas Man kalpo.
23 Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
Un Tā Kunga vārds notika uz Jeremiju sacīdams:
24 “Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
Vai tu neredzi, ko šie ļaudis runā un saka? Tās divas ciltis, ko Tas Kungs bija izredzējis, Viņš nu atmetis, un tie nievā Manus ļaudis, tā kā tie vairs nebūtu tauta viņu priekšā.
25 ‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
Tā saka Tas Kungs: ja Mana derība ar dienu un nakti nepastāv, ja Es debess un zemes likumus neesmu cēlis,
26 monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”
Tad Es arī atmetīšu Jēkaba un Sava kalpa Dāvida dzimumu, ka neņemu no viņa dzimuma valdītājus pār Ābrahāma, Īzaka un Jēkaba dzimumu. Jo Es vedīšu atpakaļ viņu cietumniekus un apžēlošos par viņiem.