< Yeremiya 33 >
1 Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
And it came [the] word of Yahweh to Jeremiah a second [time] and he still he [was] shut up in [the] courtyard of the guard saying.
2 “Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
Thus he says Yahweh [who] made it Yahweh [who] formed it to establish it [is] Yahweh name his.
3 ‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
Call to me and I will answer you and I will tell to you great [things] and incomprehensible [things] [which] not you know them.
4 Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
For thus he says Yahweh [the] God of Israel on [the] houses of the city this and on [the] houses of [the] kings of Judah which have been pulled down because of the mounds and because of the sword.
5 Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
Going to fight with the Chaldeans and to fill them with [the] corpses of humankind which I struck down in anger my and in rage my and whom I have hidden face my from the city this on all evil their.
6 “‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
Here I [will] bring up for it healing and healing and I will heal them and I will uncover to them an abundance of well-being and faithfulness.
7 Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
And I will turn back [the] captivity of Judah and [the] captivity of Israel and I will rebuild them as at the former [time].
8 Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
And I will cleanse them from all iniquity their which they have sinned to me and I will forgive (all *Q(K)*) iniquities their which they have sinned to me and which they have rebelled against me.
9 Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
And it will become to me a name of joy praise and honor to all [the] nations of the earth who they will hear all the good which I [will be] doing them and they will be in awe and they will tremble on all the good and on all the well-being which I [will be] doing for it.
10 “Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
Thus - he says Yahweh again it will be heard in the place this which you [are] saying [is] desolate it from not human being and from not animal in [the] cities of Judah and in [the] streets of Jerusalem which are made desolate from not human being and from not inhabitant and from not animal.
11 mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
[the] sound of Joy and [the] sound of gladness [the] sound of a bridegroom and [the] sound of a bride [the] sound of [those who] say give thanks to Yahweh of hosts for [is] good Yahweh for [is] for ever covenant loyalty of his [those who] bring a thank-offering [the] house of Yahweh for I will turn back [the] captivity of the land as at the former [time] he says Yahweh.
12 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
Thus he says Yahweh of hosts again it will be - in the place this desolate from not human being and unto an animal and in all cities its pasture of shepherds [who] make to lie down flock[s].
13 Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
In [the] cities of the hill country in [the] cities of the Shephelah and in [the] cities of the Negev and in [the] land of Benjamin and in [the] surroundings of Jerusalem and in [the] cities of Judah again they will pass the flock on [the] hands of [one who] counts he says Yahweh.
14 “‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
Here! days [are] coming [the] utterance of Yahweh and I will carry out the word good which I have spoken to [the] house of Israel and to [the] house of Judah.
15 “‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
In the days those and at the time that I will cause to sprout for David a branch of righteousness and he will do justice and righteousness in the land.
16 Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
In the days those it will be saved Judah and Jerusalem it will dwell to security and this [is that] which anyone will call it Yahweh - [is] righteousness our.
17 Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
For thus he says Yahweh not it will be cut off to David a man [who] sits on [the] throne of [the] house of Israel.
18 ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
And to the priests the Levites not it will be cut off a man from to before me [who] offers up a burnt offering and [who] makes smoke a grain offering and [who] makes a sacrifice all the days.
19 Yehova anawuza Yeremiya kuti:
And it came [the] word of Yahweh to Jeremiah saying.
20 Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
Thus he says Yahweh if you will break covenant of my the day and covenant of my the night and to not to be daytime and night at appropriate time their.
21 Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
Also covenant my it will be broken with David servant my from belonging to him a son [who] reigns on throne his and with the Levites the priests servants my.
22 Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
Which not it will be counted [the] host of the heavens and not it will be measured [the] sand of the sea so I will increase [the] offspring of David servant my and the Levites [the] servants of me.
23 Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
And it came [the] word of Yahweh to Jeremiah saying.
24 “Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
¿ Not have you seen what? the people this have they said saying [the] two the clans which he chose Yahweh them and he has rejected them and people my they spurn! from being again a nation before them.
25 ‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
Thus he says Yahweh if not covenant of my daytime and night [the] fixed order of heaven and earth not I have ordained.
26 monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”
Also [the] offspring of Jacob and David servant my I will reject from taking any of offspring his rulers to [the] offspring of Abraham Isaac and Jacob for (I will cause to turn back *Q(K)*) captivity their and I will have compassion on them.