< Yeremiya 33 >
1 Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
The word of Jehovah came also to Jeremiah the second time, while he was shut up in the court of the prison, and said: —
2 “Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
Thus saith Jehovah, who doeth it, Jehovah who disposeth it, to establish it; Jehovah is his name.
3 ‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
Call to me, and I will answer thee, And I will show thee great things, And hidden things which thou knowest not.
4 Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
For thus saith Jehovah, the God of Israel, Concerning the houses of this city, And concerning the houses of the kings of Judah, Which are thrown down toward the mounds and the sword,
5 Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
To fight with the Chaldaeans, And to fill them with the dead bodies of men, Whom I have smitten in mine anger and in my wrath, And for all whose wickedness I have hid my face from this city:
6 “‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
Behold, I will bind up her wounds, and heal them, And I will reveal to them abundance of peace and stability.
7 Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
And I will bring back the captives of Judah, And the captives of Israel, And I will build them, as at the first.
8 Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
And I will cleanse them from all their iniquity, Whereby they have sinned against me; And I will forgive all their iniquities, Whereby they have sinned, And have rebelled against me.
9 Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
And it [[the city]] shall be to me a name of joy, A praise and a glory among all the nations of the earth, Who shall hear of all the good which I do to them. And they shall fear and tremble because of all the good, And because of all the prosperity, which I bestow upon it.
10 “Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
Thus saith Jehovah: Yet again shall be heard in this place, Of which ye say, “It is desolate, without man and without beast,” In the cities of Judah, and in the streets of Jerusalem, Which are desolate, without man, Even without an inhabitant and without beast,
11 mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
The voice of joy and the voice of gladness, The voice of the bridegroom and the voice of the bride, The voice of them that say, “Praise ye Jehovah of hosts, For Jehovah is good, For his mercy endureth forever!” And of them that bring an offering of praise to the house of Jehovah. For I will restore the captives of the land, As at the first, saith Jehovah.
12 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
Thus saith Jehovah of hosts: Yet again shall there be in this place, Which is desolate, without man and without beast, And in all the cities thereof, A habitation of shepherds, who shall cause their flocks to rest;
13 Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
In the cities of the hill-country, and in the cities of the plain, And in the cities of the south, and in the land of Benjamin, And in the places about Jerusalem, and in the cities of Judah, Shall the flocks pass yet again Under the hands of him that numbereth them, saith Jehovah.
14 “‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
Behold, the days come, saith Jehovah, That I will perform that good thing Which I have spoken concerning the house of Israel, And concerning the house of Judah.
15 “‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
In those days and at that time Will I cause to grow up from David a righteous branch, Who shall maintain justice and equity in the land.
16 Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
In those days shall Judah be saved, And Jerusalem shall dwell securely; And this is the name which shall be given her, Jehovah-is-our-salvation.
17 Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
For thus saith Jehovah: There shall never fail from David A man to sit upon the throne of the house of Israel;
18 ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
Neither from the priests and the Levites Shall a man fail before me, To offer burnt-offerings, and to kindle meat-offerings, And to perform sacrifice continually.
19 Yehova anawuza Yeremiya kuti:
And the word of Jehovah came to Jeremiah and said,
20 Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
Thus saith Jehovah: If ye can break my covenant concerning the day, And my covenant concerning the night, So that there shall no more be day and night in their season,
21 Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
Then also may my covenant with David my servant be broken, So that he shall not have a son to reign upon his throne, And with the Levites, the priests, my servants.
22 Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
As the host of heaven cannot be numbered, Nor the sand of the sea measured, So will I multiply the posterity of David my servant, And the Levites who minister to me.
23 Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
The word of Jehovah came also to Jeremiah, saying:
24 “Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
Seest thou not what this people speaketh, saying, “The two families, which Jehovah chose, he hath cast off”? Therefore they despise my people, So that they are no more a people in their eyes.
25 ‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
Thus saith Jehovah: If my covenant concerning the day and the night be not maintained, And if I have not established the ordinances of the heaven and the earth,
26 monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”
Then will I cast away the posterity of Jacob, and of David, my servant, So as not to take of his posterity to be rulers Over the posterity of Abraham, Isaac, and Jacob; For I will bring them back from their captivity, And have mercy upon them.