< Yeremiya 33 >

1 Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
Og Herrens Ord kom til Jeremias anden Gang, medens han endnu var indelukket i Fængselets Forgaard; det lød:
2 “Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
Saa siger Herren, som gør det, Herren, som beslutter det, saa at han udfører det, Herren er hans Navn:
3 ‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
Raab til mig, og jeg vil svare dig, og jeg vil tilkendegive dig store og velforvarede Ting, som du ikke ved.
4 Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
Thi saa siger Herren, Israels Gud, om denne Stads Huse og om Judas Kongers Huse, som ere slaaede ned formedelst Belejringsvoldene og formedelst Sværdet,
5 Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
og om dem, som kom ind for at stride imod Kaldæerne og for at fylde op med døde Kroppe af Mennesker, hvilke jeg slog i min Vrede og i min Harme, og idet jeg skjulte mit Ansigt for denne Stad for al deres Ondskabs Skyld:
6 “‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
Se, jeg vil lade dens Helbredelse og Lægedom tage til og læge dem, og jeg vil oplade dem en Rigdom af Fred og Sandhed.
7 Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
Og jeg vil omvende Judas Fangenskab og Israels Fangenskab, og jeg vil bygge dem som i Begyndelsen.
8 Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
Og jeg vil rense dem fra al deres Misgerning, med hvilken de syndede imod mig, og forlade dem alle deres Misgerninger, med hvilke de have syndet imod mig, og med hvilke de have forbrudt sig imod mig.
9 Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
Og det skal være mig til et glædeligt Navn, til Lov og til Ære for alle Jordens Folkeslag, som høre alt det gode, jeg gør dem; og de skulle forfærdes og skælve over alt det gode og over al den Fred, som jeg vil give dem.
10 “Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
Saa siger Herren: Endnu skal der paa dette Sted, om hvilket I sige: Det er øde, uden Folk og uden Fæ, i Judas Stæder og paa Jerusalems Gader, som ere ødelagte, uden Folk og uden Indbyggere og uden Fæ, høres
11 mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
Fryds Røst og Glædes Røst, Brudgoms Røst og Bruds Røst, deres Røst, som sige: Takker den Herre Zebaoth, thi Herren er god, thi hans Miskundhed er evindelig, og deres, som bringe Takoffer til Herrens Hus; thi jeg vil omvende Landets Fangenskab som i Begyndelsen, sagde Herren.
12 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
Saa siger den Herre Zebaoth: Endnu skal der være paa dette Sted, som er øde uden Folk og uden Fæ, og i alle dets Stæder Bolig for Hyrder, som lade Hjorden hvile.
13 Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
I Stæderne paa Bjerget, i Stæderne i Lavlandet og i Stæderne imod Sønden og i Benjamins Land og trindt omkring Jerusalem og i Judas Stæder skulle Hjordene endnu gaa forbi Tællerens Hænder, siger Herren.
14 “‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
Se, de Dage komme, siger Herren, da jeg vil stadfæste det gode Ord, hvilket jeg har talt til Israels Hus og om Judas Hus.
15 “‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
I de Dage og paa den Tid vil jeg lade for David en Retfærdigheds Vækst opvokse; og han skal øve Ret og Retfærdighed paa Jorden.
16 Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
I de Dage skal Juda frelses og Jerusalem bo tryggelig; og dette er Navnet, man skal give den: Herren vor Retfærdighed.
17 Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
Thi saa siger Herren: Der skal ikke fattes for David en Mand, som skal sidde paa Israels Hus's Trone.
18 ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
Og der skal ikke fattes for Præsterne, Leviterne, en Mand til at staa for mit Ansigt, som skal ofre Brændoffer og antænde Madoffer og lave Slagtoffer alle Dagene.
19 Yehova anawuza Yeremiya kuti:
Og Herrens Ord kom til Jeremias, saaledes:
20 Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
Saa siger Herren: Dersom I kunne bryde min Pagt med Dagen og min Pagt med Natten, saa at der ikke bliver Dag og Nat, naar Tiden er:
21 Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
Da skal ogsaa min Pagt med David, min Tjener, brydes, at han ikke skal have en Søn til at være Konge paa hans Trone, og med Leviterne, Præsterne, mine Tjenere.
22 Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
Thi ligesom Himmelens Hær ikke kan tælles og Havets Sand ikke maales, saaledes vil jeg formere Davids, min Tjeners, Sæd og Leviterne, som tjene mig.
23 Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
Og Herrens Ord kom til Jeremias, saalunde:
24 “Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
Har du ikke set, hvad dette Folk har talt, idet det siger: De to Slægter, som Herren havde udvalgt, dem har han forkastet? og de foragte mit Folk, saa at det ikke mere er et Folk for deres Ansigt.
25 ‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
Saa siger Herren: Dersom jeg ikke har fastsat min Pagt med Dag og Nat, Himmelens og Jordens Skikke,
26 monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”
da vil jeg ogsaa forkaste Jakobs og Davids, min Tjeners, Sæd, saa at jeg ikke af hans Sæd tager dem, som skulle herske over Abrahams, Isaks og Jakobs Sæd; thi jeg vil omvende deres Fangenskab og forbarme mig over dem.

< Yeremiya 33 >