< Yeremiya 32 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
[the] word which to be to(wards) Jeremiah from with LORD (in/on/with year *Q(K)*) [the] tenth to/for Zedekiah king Judah he/she/it [the] year eight ten year to/for Nebuchadnezzar
2 Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
and then strength: soldiers king Babylon to confine upon Jerusalem and Jeremiah [the] prophet to be to restrain in/on/with court [the] guardhouse which house: home king Judah
3 Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
which to restrain him Zedekiah king Judah to/for to say why? you(m. s.) to prophesy to/for to say thus to say LORD look! I to give: give [obj] [the] city [the] this in/on/with hand: power king Babylon and to capture her
4 Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
and Zedekiah king Judah not to escape from hand: power [the] Chaldea for to give: give to give: give in/on/with hand: power king Babylon and to speak: speak lip his with lip his and eye his [obj] (eye his *Q(K)*) to see: see
5 Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
and Babylon to go: take [obj] Zedekiah and there to be till to reckon: visit I [obj] him utterance LORD for to fight with [the] Chaldea not to prosper
6 Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
and to say Jeremiah to be word LORD to(wards) me to/for to say
7 Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
behold Hanamel son: child Shallum beloved: male relative your to come (in): come to(wards) you to/for to say to buy to/for you [obj] land: country my which in/on/with Anathoth for to/for you justice [the] redemption to/for to buy
8 Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
and to come (in): come to(wards) me Hanamel son: descendant/people beloved: male relative my like/as word LORD to(wards) court [the] guardhouse and to say to(wards) me to buy please [obj] land: country my which in/on/with Anathoth which in/on/with land: country/planet Benjamin for to/for you justice [the] possession and to/for you [the] redemption to buy to/for you and to know for word LORD he/she/it
9 choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
and to buy [obj] [the] land: country from with Hanamel son: descendant/people beloved: male relative my which in/on/with Anathoth and to weigh [emph?] to/for him [obj] [the] silver: money seven shekel and ten [the] silver: money
10 Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
and to write in/on/with scroll: document and to seal and to testify witness and to weigh [the] silver: money in/on/with balance
11 Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
and to take: take [obj] scroll: document [the] purchase [obj] [the] to seal [the] commandment and [the] statute: decree and [obj] [the] to reveal: uncover
12 Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
and to give: give [obj] [the] scroll: document [the] purchase to(wards) Baruch son: child Neriah son: child Mahseiah to/for eye: before(the eyes) Hanamel beloved: male relative my and to/for eye: before(the eyes) [the] witness [the] to write in/on/with scroll: document [the] purchase to/for eye: before(the eyes) all [the] Jew [the] to dwell in/on/with court [the] guardhouse
13 “Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
and to command [obj] Baruch to/for eye: before(the eyes) their to/for to say
14 ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
thus to say LORD Hosts God Israel to take: take [obj] [the] scroll: document [the] these [obj] scroll: document [the] purchase [the] this and [obj] [the] to seal and [obj] scroll: document [the] to reveal: uncover [the] this and to give: put them in/on/with article/utensil earthenware because to stand: stand day many
15 Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
for thus to say LORD Hosts God Israel still to buy house: home and land: country and vineyard in/on/with land: country/planet [the] this
16 Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
and to pray to(wards) LORD after to give: give I [obj] scroll: document [the] purchase to(wards) Baruch son: child Neriah to/for to say
17 “Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
alas! Lord YHWH/God behold you(m. s.) to make [obj] [the] heaven and [obj] [the] land: country/planet in/on/with strength your [the] great: large and in/on/with arm your [the] to stretch not to wonder from you all word: thing
18 Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
to make: do kindness to/for thousand and to complete iniquity: guilt father to(wards) bosom: lap son: child their after them [the] God [the] great: large [the] mighty man LORD Hosts name his
19 Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
great: large [the] counsel and many [the] deed which eye your to open upon all way: conduct son: child man to/for to give: give to/for man: anyone like/as way: conduct his and like/as fruit deed his
20 Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
which to set: make sign: miraculous and wonder in/on/with land: country/planet Egypt till [the] day: today [the] this and in/on/with Israel and in/on/with man and to make to/for you name like/as day: today [the] this
21 Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
and to come out: send [obj] people your [obj] Israel from land: country/planet Egypt in/on/with sign: miraculous and in/on/with wonder and in/on/with hand: power strong and in/on/with arm to stretch and in/on/with fear great: large
22 Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
and to give: give to/for them [obj] [the] land: country/planet [the] this which to swear to/for father their to/for to give: give to/for them land: country/planet to flow: flowing milk and honey
23 Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
and to come (in): come and to possess: take [obj] her and not to hear: obey in/on/with voice your (and in/on/with instruction your *Q(K)*) not to go: walk [obj] all which to command to/for them to/for to make: do not to make: do and to encounter: chanced [obj] them [obj] all [the] distress: harm [the] this
24 “Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
behold [the] mound to come (in): come [the] city to/for to capture her and [the] city to give: give in/on/with hand: power [the] Chaldea [the] to fight upon her from face: because [the] sword and [the] famine and [the] pestilence and which to speak: speak to be and look! you to see: see
25 Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
and you(m. s.) to say to(wards) me Lord YHWH/God to buy to/for you [the] land: country in/on/with silver: money and to testify witness and [the] city to give: give in/on/with hand: power [the] Chaldea
26 Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
and to be word LORD to(wards) Jeremiah to/for to say
27 “Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
behold I LORD God all flesh from me to wonder all word: thing
28 Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
to/for so thus to say LORD look! I to give: give [obj] [the] city [the] this in/on/with hand: power [the] Chaldea and in/on/with hand: power Nebuchadnezzar king Babylon and to capture her
29 Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
and to come (in): come [the] Chaldea [the] to fight upon [the] city [the] this and to kindle [obj] [the] city [the] this in/on/with fire and to burn her and [obj] [the] house: home which to offer: burn upon roof their to/for Baal and to pour drink offering to/for God another because to provoke me
30 “Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
for to be son: child Israel and son: child Judah surely to make: do [the] bad: evil in/on/with eye: seeing my from youth their for son: child Israel surely to provoke [obj] me in/on/with deed: work hand their utterance LORD
31 Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
for upon face: anger my and upon rage my to be to/for me [the] city [the] this to/for from [the] day: today which to build [obj] her and till [the] day: today [the] this to/for to turn aside: remove her from upon face my
32 Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
upon all distress: evil son: child Israel and son: child Judah which to make: do to/for to provoke me they(masc.) king their ruler their priest their and prophet their and man: anyone Judah and to dwell Jerusalem
33 Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
and to turn to(wards) me neck and not face and to learn: teach [obj] them to rise and to learn: teach and nothing they to hear: hear to/for to take: recieve discipline: instruction
34 Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
and to set: make abomination their in/on/with house: temple which to call: call by name my upon him to/for to defile him
35 Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
and to build [obj] high place [the] Baal which in/on/with valley son: child (Topheth of son of) Hinnom to/for to pass [obj] son: child their and [obj] daughter their to/for Molech which not to command them and not to ascend: rise upon heart my to/for to make: do [the] abomination [the] this because (to sin *Q(k)*) [obj] Judah
36 “Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
and now to/for so thus to say LORD God Israel to(wards) [the] city [the] this which you(m. p.) to say to give: give in/on/with hand: power king Babylon in/on/with sword and in/on/with famine and in/on/with pestilence
37 Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
look! I to gather them from all [the] land: country/planet which to banish them there in/on/with face: anger my and in/on/with rage my and in/on/with wrath great: large and to return: return them to(wards) [the] place [the] this and to dwell them to/for security
38 Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
and to be to/for me to/for people and I to be to/for them to/for God
39 Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
and to give: give to/for them heart one and way: conduct one to/for to fear: revere [obj] me all [the] day: always to/for good to/for them and to/for son: child their after them
40 Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
and to cut: make(covenant) to/for them covenant forever: enduring which not to return: return from after them to/for be good me [obj] them and [obj] fear my to give: put in/on/with heart their to/for lest to turn aside: turn aside from upon me
41 Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
and to rejoice upon them to/for be good [obj] them and to plant them in/on/with land: country/planet [the] this in/on/with truth: faithful in/on/with all heart my and in/on/with all soul my
42 “Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
for thus to say LORD like/as as which to come (in): bring to(wards) [the] people [the] this [obj] all [the] distress: harm [the] great: large [the] this so I to come (in): bring upon them [obj] all [the] welfare which I to speak: promise upon them
43 Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
and to buy [the] land: country in/on/with land: country/planet [the] this which you(m. p.) to say devastation he/she/it from nothing man and animal to give: give in/on/with hand: power [the] Chaldea
44 Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”
land: country in/on/with silver: money to buy and to write in/on/with scroll: document and to seal and to testify witness in/on/with land: country/planet Benjamin and in/on/with around Jerusalem and in/on/with city Judah and in/on/with city [the] mountain: hill country and in/on/with city [the] Shephelah and in/on/with city [the] Negeb for to return: rescue [obj] captivity their utterance LORD

< Yeremiya 32 >