< Yeremiya 31 >

1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
W tym czasie, mówi PAN, będę Bogiem wszystkich rodów Izraela, a one będą moim ludem.
2 Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
Tak mówi PAN: Lud, który ocalał od miecza, znalazł łaskę na pustyni, gdy kroczyłem przed nim, aby dać odpoczynek Izraelowi.
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
[Powiedz]: Dawno PAN mi się ukazał, [mówiąc]: Owszem, umiłowałem cię wieczną miłością, dlatego przyciągam cię swoim miłosierdziem.
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
Odbuduję cię znowu i będziesz odbudowana, dziewico Izraela! Znowu przyozdobisz się w swe bębenki i wystąpisz wśród tańców pełnych wesela.
5 Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
Znów będziesz sadziła winnice na górach Samarii; siewcy będą sadzić i spożywać [z tego].
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
Nastanie bowiem dzień, kiedy stróże będą wołać na górze Efraim: Wstańcie, wejdźmy na Syjon do PANA, swego Boga.
7 Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
Tak bowiem mówi PAN: Śpiewajcie radośnie dla Jakuba i wykrzykujcie przed przodującym wśród narodów. Głoście, wychwalajcie i mówcie: PANIE, wybaw resztkę twego ludu Izraela.
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
Oto przyprowadzę ich z ziemi północnej i zgromadzę ich z krańców ziemi; wśród nich będą ślepi i chromi, brzemienne i rodzące. Powrócą tu wielką gromadą.
9 Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
Przyjdą z płaczem i przyprowadzę ich wśród modlitw, a poprowadzę ich nad strumienie wód prostą drogą, na której się nie potkną. Jestem bowiem ojcem dla Izraela, a Efraim jest moim pierworodnym.
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
Słuchajcie słowa PANA, o narody, głoście [je] na dalekich wyspach i mówcie: Ten, który rozproszył Izraela, zgromadzi go i będzie go strzec jak pasterz swoich trzód.
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
PAN bowiem wykupił Jakuba i wybawił go z ręki silniejszego od niego.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
Przyjdą więc i będą śpiewać na wyżynie Syjonu, i zbiegną się do dobroci PANA za zboże, za wino i za oliwę, za jagnięta i za cielęta, a ich dusza będzie jak nawodniony ogród i już nie będą się smucić.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
Wtedy dziewica będzie radować się wśród pląsów, także młodzieńcy i starcy razem. Zamienię bowiem ich żałobę w radość, pocieszę ich i rozraduję po ich smutku.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
I nasycę duszę ich kapłanów tłuszczem, a mój lud nasyci się moją dobrocią, mówi PAN.
15 Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
Tak mówi PAN: W Rama słychać głos, lament i gorzki płacz: Rachel opłakuje swoich synów, nie daje się pocieszyć po [stracie] swoich synów, bo ich już nie ma.
16 Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
Tak mówi PAN: Powstrzymaj swój głos od płaczu, a swe oczy od łez, bo otrzymasz zapłatę za swoją pracę, mówi PAN. Powrócą z ziemi wroga.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
Jest nadzieja na twój kres – mówi PAN – [twoi] synowie powrócą do swojej krainy.
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
Zaprawdę, usłyszałem jak Efraim się użala: Karciłeś mnie i poniosłem karę jak nieokiełznane cielę. Nawróć mnie, a będę nawrócony, bo ty jesteś PANEM, moim Bogiem.
19 Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
Bo po moim nawróceniu pokutowałem; gdy poznałem samego siebie, uderzyłem się w biodro; wstydzę się i rumienię, gdyż noszę hańbę swej młodości.
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
Czyż Efraim nie jest moim drogim synem? Czyż nie [jest] rozkoszny? Ilekroć bowiem mówię przeciwko niemu, nieustannie go wspominam. Dlatego wzrusza się moje wnętrze z jego powodu; na pewno zlituję się nad nim, mówi PAN.
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
Postaw sobie drogowskazy, połóż sobie stosy kamieni. Zwróć swoje serce na gościniec, na drogę, [którą] chodziłaś. Powróć, dziewico Izraela! Powróć do tych swoich miast.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
Jak długo będziesz się błąkać, córko uparta? PAN bowiem stworzył nową rzecz na ziemi: kobieta ogarnie mężczyznę.
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
Tak mówi PAN zastępów, Bóg Izraela: Jeszcze będą mówić to słowo w ziemi Judy i w jej miastach, gdy odwrócę ich niewolę: Niech PAN cię błogosławi, mieszkanie sprawiedliwości, góro świętości!
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
Zamieszkają bowiem w ziemi Judy i we wszystkich jego miastach razem rolnicy i ci, którzy chodzą za stadem.
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
Napoiłem spragnioną duszę i nasyciłem wszelką smutną duszę.
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
Wtedy się obudziłem i spojrzałem, a mój sen był dla mnie przyjemny.
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
Oto nadchodzą dni, mówi PAN, w których zasieję dom Izraela i dom Judy nasieniem ludzi i nasieniem zwierząt.
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
A jak się starałem ich wykorzeniać, burzyć, obalać, niszczyć i trapić, tak będę nad nimi czuwał, by ich budować i sadzić, mówi PAN.
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
W tych dniach już nie będą mówić: Ojcowie jedli cierpkie winogrona, a synom ścierpły zęby;
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
Lecz każdy umrze za swoją nieprawość. Każdemu człowiekowi, który zje cierpkie winogrona, ścierpną zęby.
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
Oto nadchodzą dni, mówi PAN, kiedy zawrę z domem Izraela i z domem Judy nowe przymierze;
32 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
Nie takie przymierze, jakie zawarłem z ich ojcami w dniu, kiedy ująłem ich za rękę, aby ich wyprowadzić z ziemi Egiptu. Oni bowiem złamali moje przymierze, chociaż ja byłem ich mężem, mówi PAN.
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
Ale takie będzie przymierze, które zawrę z domem Izraela po tych dniach, mówi PAN: Włożę moje prawo w ich wnętrzu i wypisze je na ich sercach. I będę ich Bogiem, a oni będą moim ludem.
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
I nikt nie będzie już uczył swego bliźniego ani nikt swego brata, mówiąc: Poznaj PANA, bo wszyscy będą mnie znali, od najmniejszego aż do największego z nich, mówi PAN. Przebaczę bowiem ich nieprawość, a ich grzechów nigdy więcej nie wspomnę.
35 Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Tak mówi PAN, który daje słońce na światłość w dzień, prawa księżyca i gwiazd na światłość w nocy; który rozdziela morze tak, że huczą jego fale; PAN zastępów – to jego imię.
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
Gdyby te prawa ustały przede mną, mówi PAN, wtedy [i] potomstwo Izraela przestanie być narodem przede mną na wieki.
37 Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
Tak mówi PAN: Jeśli można zmierzyć niebiosa w górze i zbadać fundamenty ziemi w dole, wtedy i ja odrzucę całe potomstwo Izraela za to wszystko, co uczynili, mówi PAN.
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
Oto nadchodzą dni, mówi PAN, w których to miasto zostanie odbudowane PANU od Wieży Chananeela aż do Bramy Narożnej;
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
I będzie się ciągnął dalej sznur mierniczy na wprost ku wzgórzu Gareb, a potem zwróci się ku Goa.
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”
I cała dolina trupów i popiołu, wszystkie pola aż do potoku Cedron i narożnika Bramy Końskiej ku wschodowi będą poświęcone PANU. Nie zostaną już wykorzenione ani zburzone na wieki.

< Yeremiya 31 >