< Yeremiya 31 >

1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
En ce temps-là, dit le Seigneur, je serai le Dieu de toutes les familles d’Israël, et elles seront mon peuple.
2 Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
Voici ce que dit le Seigneur: Il a trouvé grâce dans le désert, un peuple qui avait échappé au glaive: Israël ira à son repos.
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
De loin le Seigneur m’a apparu. Et je t’ai aimée d’un amour éternel: c’est pour cela que je t’ai attirée ayant pitié de toi.
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
Et de nouveau je t’édifierai, et tu seras édifiée, vierge d’Israël; tu paraîtras encore ornée au milieu des tambours, et tu sortiras dans un chœur de joueurs d’instruments.
5 Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
Tu planteras encore des vignes sur les montagnes de Samarie; des planteurs les planteront, et jusqu’à ce que le temps arrive, ils ne vendangeront pas.
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
Car viendra un jour auquel les gardes crieront sur la montagne d’Ephraïm: Levez-vous, et montons en Sion vers le Seigneur notre Dieu.
7 Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
Parce que voici ce que dit le Seigneur: Exultez d’allégresse, Jacob, et poussez des cris éclatants à la tête des nations, faites retentir vos voix, chantez, et dites: Seigneur, sauvez votre peuple, les restes d’Israël.
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
Voilà que moi je les amènerai de la terre de l’aquilon, et que je les rassemblerai des extrémités de la terre; parmi eux seront l’aveugle et le boiteux, la femme enceinte et celle qui a enfanté, mêlés ensemble, grande assemblée d’hommes revenant ici.
9 Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
C’est dans le pleur qu’ils viendront, et c’est dans la miséricorde que je les ramènerai, et je les ramènerai à travers des torrents d’eau dans une voie droite, et ils n’y heurteront point, parce que je suis devenu pour Israël un père, et qu’Éphraïm est mon premier-né.
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
Ecoutez, nations, la parole du Seigneur, et annoncez-la aux îles qui sont au loin, et dites: Celui qui a dispersé Israël le rassemblera, et il le gardera comme un pasteur son troupeau.
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
Car le Seigneur a racheté Jacob, et l’a délivré de la main d’un plus puissant que lui.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
Et ils viendront, et ils chanteront des louanges sur la montagne de Sion; et ils accourront en foule vers les biens du Seigneur, vers le blé, et le vin, et l’huile, et le fruit des troupeaux de menu et de gros bétail; et leur âme sera comme un jardin arrosé; et ils n’auront plus faim.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
Alors se réjouira la vierge au milieu d’un chœur, ainsi que les jeunes hommes et les vieillards ensemble; et je changerai leur deuil en joie, et je les consolerai, et je les remplirai d’allégresse après leur douleur.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
Et j’enivrerai l’âme des prêtres de graisse, et mon peuple sera rempli de mes biens, dit le Seigneur.
15 Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
Voici ce que dit le Seigneur: Une voix a été entendue sur une hauteur, voix de lamentation, de deuil et de pleur, la voix de Rachel déplorant la perte de ses enfants, et ne voulant pas en être consolée, parce qu’ils ne sont plus,
16 Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
Voici ce que dit le Seigneur: Que ta voix cesse ses gémissements, et tes yeux leurs larmes; parce qu’il est une récompense à tes œuvres, dit le Seigneur, et ils reviendront de la terre de l’ennemi.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
Et il est un espoir pour tes derniers moments, dit le Seigneur, et tes fils reviendront dans tes confins.
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
Entendant, j’ai entendu Ephraïm dans sa transmigration: Vous m’avez châtié et j’ai été instruit, comme un jeune taureau indompté; convertissez-moi et je serai converti, parce que vous êtes le Seigneur mon Dieu.
19 Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
Car, après que vous m’avez converti, j’ai fait pénitence, et après que vous m’avez montré mon état, j’ai frappé ma cuisse, l’ai été confondu, et j’ai rougi, parce que j’ai supporté l’opprobre de ma jeunesse.
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
Est-ce qu’il n’est pas un fils honorable pour moi, Ephraïm, n’est-il pas un enfant de délices? parce que, depuis que j’ai parlé de lui, je me souviendrai encore de lui. C’est pour cela que mes entrailles sont émues sur lui; ayant pitié, j’aurai pitié de lui, dit le Seigneur.
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
Etablis-toi un lieu d’observation, abandonne-toi à l’amertume, dirige ton cœur vers la voie droite, dans laquelle tu as marché: retourne, vierge d’Israël, retourne vers ces cités tiennes.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
Jusques à quand seras-tu énervée par les délices, fille vagabonde? parce que le Seigneur a créé un nouveau prodige sur la terre: UNE FEMME ENVIRONNERÀ UN HOMME.
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
Voici ce que dit le Seigneur, Dieu d’Israël: Ils diront encore cette parole dans la terre de Juda et dans ses villes, lorsque j’aurai ramené leurs captifs: Que le Seigneur te bénisse, beauté de justice, montagne sainte;
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
Et y habiteront Juda et toutes ses cités ensemble, les laboureurs et ceux qui conduisent les troupeaux.
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
Parce que j’ai enivré l’âme fatiguée, et j’ai rassasié toute âme qui avait faim.
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
C’est pour cela que je me suis comme éveillé de mon sommeil; et j’ai vu, et mon sommeil m’a été doux.
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
Voilà que des jours viennent, dit le Seigneur, et je sèmerai la maison d’Israël et la maison de Juda d’une semence d’hommes et d’une semence de bêtes,
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
Et comme j’ai veillé sur eux, afin de les arracher, et de les détruire, et de les dissiper, et de les perdre, et de les affliger, ainsi je veillerai sur eux, afin de les édifier et de les planter, dit le Seigneur.
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
En ces jours-là, on ne dira plus: Les pères ont mangé des raisins verts, et les dents des fils ont été agacées.
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
Mais chacun mourra dans son iniquité; tout homme qui aura mangé le raisin vert, ses dents seront agacées.
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
Voilà que des jours viendront, dit le Seigneur, et je ferai une nouvelle alliance avec la maison d’Israël et avec la maison de Juda,
32 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
Non pas selon l’alliance que j’ai formée avec leurs pères, au jour auquel je pris leur main, afin de les faire sortir de la terre d’Egypte; alliance qu’ils ont rendue vaine, et moi je les ai maîtrisés, dit le Seigneur.
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
Mais voici l’alliance que je ferai avec la maison d’Israël après ces jours-là, dit le Seigneur: Je mettrai ma loi dans leurs entrailles, et je l’écrirai dans leur cœur; et je serai leur Dieu, et eux seront mon peuple.
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
Et un homme n’instruira plus son prochain, et un homme son frère, disant: Connais le Seigneur; car tous me connaîtront, depuis le plus petit d’entre eux jusqu’au plus grand, dit le Seigneur; parce que je pardonnerai leur iniquité, et que de leur péché je ne me souviendrai plus.
35 Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Voici ce que dit le Seigneur, qui donne le soleil pour éclairer dans le jour, et le cours réglé de la lune et des étoiles pour éclairer pendant la nuit; qui agite la mer, et ses flots mugissent; le Seigneur des armées est son nom.
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
Si ces lois défaillent devant moi, dit le Seigneur, alors aussi la race d’Israël défaudra pour n’être plus à jamais un peuple devant moi.
37 Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
Voici ce que dit le Seigneur: Si les cieux peuvent être mesurés dans leur hauteur, et les fondements de la terre sondés dans leur profondeur; moi aussi je rejetterai toute la race d’Israël, à cause de tout ce qu’ils ont fait, dit le Seigneur.
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
Voilà que des jours viennent, dit le Seigneur, et la cité sera édifiée pour le Seigneur, depuis la tour d’Hananéel, jusqu’à la porte de l’angle.
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
Et le cordeau sortira encore au-delà à sa vue sur la colline de Gareb; et fera le tour de Goatha,
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”
Et de toute la vallée des cadavres et de la cendre, et de toute la région de la mort, jusqu’au torrent de Cédron, et jusqu’à l’angle de la porte orientale des chevaux; le lieu saint du Seigneur ne sera pas renversé, et il ne sera jamais plus détruit.

< Yeremiya 31 >