< Yeremiya 31 >

1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
“At that time—this is Yahweh's declaration—I will be the God of all the clans of Israel, and they will be my people.”
2 Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
Yahweh says this, “The people who have survived the sword have found favor in the wilderness; I will go out to give rest to Israel.”
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
Yahweh appeared to me in the past and said, “I have loved you, Israel, with everlasting love. So I have drawn you toward myself with covenant faithfulness.
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
I will build you up again so you will be built, virgin Israel. You will again pick up your tambourines and go out with happy dances.
5 Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
You will plant vineyards again on the mountains of Samaria; the farmers will plant and put the fruit to good use.
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
For a day will come when the watchmen in the mountains of Ephraim will proclaim, 'Arise, let us go up to Zion to Yahweh our God.'
7 Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
For Yahweh says this, “Shout for joy over Jacob! Shout in gladness for the chief people of the nations! Let praise be heard. Say, 'Yahweh has rescued his people, the remnant of Israel.'
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
See, I am about to bring them from the northern lands. I will gather them from the farthest parts of the earth. The blind and lame will be among them; pregnant women and those who are about to give birth will be with them. A great assembly will return here.
9 Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
They will come weeping; I will lead them as they make their pleas. I will have them journey to streams of water on a straight road. They will not stumble on it, for I will be a father to Israel, and Ephraim will be my firstborn.”
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
“Hear the word of Yahweh, nations. Report along the coasts in the distance. You nations must say, 'The one who scattered Israel is gathering her up and keeping her as a shepherd keeps his sheep.'
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
For Yahweh has ransomed Jacob and has redeemed him from the hand that was too strong for him.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
Then they will come and rejoice on the heights of Zion. Their faces will shine because of Yahweh's goodness, over the corn and the new wine, over the oil and the offspring of the flocks and herds. For their lives will become like a watered garden, and they will never again feel any more sorrow.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
Then virgins will rejoice with dancing, and young and old men will be together. For I will change their mourning into celebration. I will have compassion on them and cause them to rejoice instead of sorrowing.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
Then I will saturate the lives of the priests in abundance. My people will fill themselves with my goodness—this is Yahweh's declaration.”
15 Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
Yahweh says this: “A voice is heard in Ramah, wailing and bitter weeping. It is Rachel weeping for her children. She refuses to be comforted over them, for they live no longer.”
16 Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
Yahweh says this, “Hold your voice back from weeping and your eyes from tears; there is a reward for your work—this is Yahweh's declaration—your children will return from the land of the enemy.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
There is hope for your future—this is Yahweh's declaration—your descendants will return inside their borders.”
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
“I have certainly heard Ephraim sorrowing, 'You punished me, and I have been punished like an untrained calf. Bring me back and I will be brought back, for you are Yahweh my God.
19 Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
For after I turned back to you, I was sorry; after I was trained, I slapped my thigh. I was ashamed and humiliated, for I have borne the guilt of my youth.'
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
Is not Ephraim my precious child? Is he not my dear, delightful son? For whenever I speak against him, I certainly still call him to my loving mind. In this way my heart longs for him. I will certainly have compassion on him—this is Yahweh's declaration.”
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
Place road signs for yourself. Set up guideposts for yourself. Set your mind on the right path, the way you should take. Come back, virgin Israel! Come back to these cities of yours.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
How long will you waver, faithless daughter? For Yahweh has created something new on earth—a woman surrounds a strong man.
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
Yahweh of hosts, the God of Israel, says this, “When I bring back the people to their land, they will say this in the land of Judah and its cities, 'May Yahweh bless you, you righteous place where he lives, you holy mountain.'
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
For Judah and all its cities will live together there, as will farmers and those who set out with flocks.
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
For I will cause those who are weary to drink, and I fill up those who are faint.”
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
After this I awoke, and I realized that my sleep had been refreshing.
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
“Look, the days are coming—this is Yahweh's declaration—when I will sow the houses of Israel and Judah with the descendants of man and beast.
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
In the past, I kept them under surveillance in order to uproot them and to tear them down, to overthrow, destroy, and bring them harm. But in the coming days, I will watch over them, in order to build them up and to plant them—this is Yahweh's declaration.
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
In those days no one will say any longer, 'Fathers have eaten sour grapes, but the children's teeth are dulled.'
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
For each man will die in his own iniquity; everyone who eats sour grapes, his teeth will be dulled.
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
Look, the days are coming —this is Yahweh's declaration— when I will establish a new covenant with the house of Israel and the house of Judah.
32 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
It will not be like the covenant that I established with their fathers in the days when I took them by their hand to bring them out from the land of Egypt, because they broke my covenant, although I was a husband for them. —this is Yahweh's declaration.
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
This is the covenant that I will establish with the house of Israel after these days —this is Yahweh's declaration. I will place my law within them and will write it on their heart, for I will be their God, and they will be my people.
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
Then each man will no longer teach his neighbor, or a man teach his brother and say, 'Know Yahweh!' For all of them will know me, from the smallest of them to the greatest —this is Yahweh's declaration— for I will forgive their iniquity and will no longer call their sins to mind.”
35 Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Yahweh says this, it is he who makes the sun to shine by day and fixes the moon and stars to shine by night. He is the one who sets the sea in motion so that its waves roar— Yahweh of hosts is his name.
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
“Only if these permanent things vanish from my sight—this is Yahweh's declaration— will Israel's descendants ever stop from forever being a nation before me.”
37 Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
Yahweh says this, “Only if the highest heavens can be measured, and only if the earth's foundation below can be discovered, will I reject all of Israel's descendants because of all that they have done—this is Yahweh's declaration.”
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
“Look, the days are coming—this is Yahweh's declaration—when the city will be rebuilt for me, from the Tower of Hananel to the Corner Gate.
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
Then the measuring line will go out again farther, to the hill of Gareb and around Goah.
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”
The whole valley of the dead bodies and the ashes, and all the terraced fields going out to the Kidron Valley as far as the corner of the Horse Gate on the east, will be set apart for Yahweh. The city will not be pulled up or overthrown again, forever.”

< Yeremiya 31 >