< Yeremiya 31 >

1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
At that time, says Jehovah, I will be the God of all the families of Israel, and they shall be my people.
2 Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
Thus says Jehovah: The people who were left of the sword found favor in the wilderness, even Israel, when I went to cause him to rest.
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
Jehovah appeared of old to me, saying, Yea, I have loved thee with an everlasting love. Therefore with loving kindness I have drawn thee.
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
Again I will build thee, and thou shall be built, O virgin of Israel. Again thou shall be adorned with thy tambourine, and shall go forth in the dances of those who make merry.
5 Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
Again thou shall plant vineyards upon the mountains of Samaria. The planters shall plant, and shall enjoy it.
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
For there shall be a day that the watchmen upon the hills of Ephraim shall cry, Arise ye, and let us go up to Zion to Jehovah our God.
7 Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
For thus says Jehovah: Sing with gladness for Jacob, and shout for the chief of the nations. Publish ye, praise ye, and say, O Jehovah, save thy people, the remnant of Israel.
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
Behold, I will bring them from the north country, and gather them from the outermost parts of the earth, and with them the blind man and the lame man, the woman with child, and she who travails with child together. They shall return here a great company.
9 Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
They shall come with weeping. And I will lead them with supplications. I will cause them to walk by rivers of waters, in a straight way in which they shall not stumble. For I am a father to Israel, and Ephraim is my firstborn.
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
Hear the word of Jehovah, O ye nations, and declare it in the isles afar off, and say, He who scattered Israel will gather him, and keep him, as a shepherd does his flock.
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
For Jehovah has ransomed Jacob, and redeemed him from the hand of him who was stronger than he.
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
And they shall come and sing in the height of Zion, and shall flow to the goodness of Jehovah, to the grain, and to the new wine, and to the oil, and to the young of the flock and of the herd. And their soul shall be as a watered garden, and they shall not sorrow any more at all.
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
Then the virgin shall rejoice in the dance, and the young men and the old together, for I will turn their mourning into joy, and will comfort them, and make them rejoice from their sorrow.
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
And I will satiate the soul of the priests with fatness, and my people shall be satisfied with my goodness, says Jehovah.
15 Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
Thus says Jehovah: A voice is heard in Ramah, lamentation, and bitter weeping. Rachel weeping for her children, she refused to be comforted for her children, because they are not.
16 Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
Thus says Jehovah: Refrain thy voice from weeping, and thine eyes from tears, for thy work shall be rewarded, says Jehovah, and they shall come again from the land of the enemy.
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
And there is hope for thy latter end, says Jehovah, and thy sons shall come again to their own border.
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
I have surely heard Ephraim bemoaning himself saying, Thou have chastised me, and I was chastised as a calf unaccustomed to the yoke. Turn thou me back, and I shall be turned back, for thou are Jehovah my God.
19 Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
Surely after that I was turned back. I repented, and after I was instructed, I smote upon my thigh. I was ashamed, yea, even confounded, because I bore the reproach of my youth.
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
Is Ephraim my dear son? Is he a darling child? For as often as I speak against him, I do earnestly remember him still. Therefore my heart yearns for him. I will surely have mercy upon him, says Jehovah.
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
Set thee up road marks. Make thee guideposts. Set thy heart toward the highway, even the way by which thou went. Turn again, O virgin of Israel, turn again to these thy cities.
22 Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
How long will thou go here and there, O thou backsliding daughter? For Jehovah has created a new thing in the earth: a woman shall encompass a man.
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
Thus says Jehovah of hosts, the God of Israel: Yet again they shall use this speech in the land of Judah and in the cities thereof when I shall bring again their captivity: Jehovah bless thee, O habitation of righteousness, O mountain of holiness.
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
And Judah and all the cities thereof shall dwell in there together, the husbandmen, and those who go about with flocks.
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
For I have satiated the weary soul, and every sorrowful soul I have replenished.
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
Upon this I awoke, and beheld, and my sleep was sweet to me.
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
Behold, the days come, says Jehovah, that I will sow the house of Israel and the house of Judah with the seed of man, and with the seed of beast.
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
And it shall come to pass that, just as I have watched over them to pluck up and to break down and to overthrow and to destroy and to afflict, so I will watch over them to build and to plant, says Jehovah.
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
In those days they shall no more say, The fathers have eaten sour grapes, and the son's teeth are set on edge.
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
But everyone shall die for his own iniquity. Every man who eats the sour grapes, his teeth shall be set on edge.
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
Behold, the days come, says Jehovah, that I will make a new covenant with the house of Israel, and with the house of Judah,
32 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
not according to the covenant that I made with their fathers in the day that I took them by the hand to bring them out of the land of Egypt, because they did not continue in my covenant, and I disregarded them, says Jehovah.
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
But this is the covenant that I will make with the house of Israel after those days, says Jehovah: I will give my laws into their mind, and I will write them on their hearts. And I will be their God, and they shall be my people.
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
And they shall teach no more every man his neighbor, and every man his brother, saying, Know Jehovah, for they shall all know me, from the least of them to the greatest of them, says Jehovah. For I will forgive their iniquity, and I will remember their sin no more.
35 Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Thus says Jehovah, who gives the sun for a light by day, and the ordinances of the moon and of the stars for a light by night, who stirs up the sea, so that the waves thereof roar. Jehovah of hosts is his name.
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
If these ordinances depart from before me, says Jehovah, then the seed of Israel also shall cease from being a nation before me forever.
37 Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
Thus says Jehovah: If heaven above can be measured, and the foundations of the earth searched out beneath, then I will also cast off all the seed of Israel for all that they have done, says Jehovah.
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
Behold, the days come, says Jehovah, that the city shall be built to Jehovah from the tower of Hananel to the gate of the corner.
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
And the measuring line shall go out further straight onward to the hill Gareb, and shall turn about to Goah.
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”
And the whole valley of the dead bodies and of the ashes, and all the fields, to the brook Kidron, to the corner of the horse gate toward the east, shall be holy to Jehovah. It shall not be plucked up, nor thrown down any more forever.

< Yeremiya 31 >