< Yeremiya 31 >
1 “Pa nthawi imeneyo,” akutero Yehova, “Ndidzakhala Mulungu wa mafuko onse a Israeli, ndipo iwo adzakhala anthu anga.”
耶和华说:“那时,我必作以色列各家的 神;他们必作我的子民。”
2 Yehova akuti, “Anthu amene anapulumuka ku nkhondo ndinawakomera mtima mʼchipululu; pamene Aisraeli ankafuna kupumula.”
耶和华如此说: 脱离刀剑的就是以色列人。 我使他享安息的时候, 他曾在旷野蒙恩。
3 Ine ndinawaonekera ndili chapatali ndipo ndinati, “Ine ndakukondani ndi chikondi chopanda malire. Nʼchifukwa chake ndipitiriza kukukondani.
古时耶和华向以色列显现,说: 我以永远的爱爱你, 因此我以慈爱吸引你。
4 Ndidzakusamaliraninso, inu anthu a Israeli; mudzasangalala poyimba tizitoliro tanu, ndipo mudzapita kukavina nawo anthu ovina mwachimwemwe.
以色列的民哪, 我要再建立你,你就被建立; 你必再以击鼓为美, 与欢乐的人一同跳舞而出;
5 Mudzalimanso minda ya mpesa pa mapiri a Samariya; alimi adzadzala mphesa ndipo adzadya zipatso zake.
又必在撒马利亚的山上栽种葡萄园, 栽种的人要享用所结的果子。
6 Lidzafika tsiku pamene alonda adzafuwula pa mapiri a Efereimu nati, ‘Tiyeni tipite ku Ziyoni, kwa Yehova Mulungu wathu.’”
日子必到,以法莲山上守望的人必呼叫说: 起来吧!我们可以上锡安, 到耶和华—我们的 神那里去。
7 Yehova akuti, “Imbani mosangalala chifukwa cha Yakobo, fuwulani chifukwa cha mtundu wopambana mitundu yonse. Matamando anu amveke, ndipo munene kuti, ‘Yehova wapulumutsa anthu ake otsala a Israeli.’
耶和华如此说: 你们当为雅各欢乐歌唱, 因万国中为首的欢呼。 当传扬颂赞说: 耶和华啊, 求你拯救你的百姓以色列所剩下的人。
8 Taonani, ndidzabwera nawo kuchokera ku dziko la kumpoto, ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Anthu osaona, olumala, amayi oyembekezera ndi amene ali pa nthawi yawo yochira adzabwera nawo pamodzi. Chidzakhala chikhamu cha anthu obwerera kuno.
我必将他们从北方领来, 从地极招聚; 同着他们来的有瞎子、瘸子、孕妇、产妇; 他们必成为大帮回到这里来。
9 Adzabwera akulira; koma Ine ndikuwatonthoza mtima, ndidzawaperekeza. Ndidzawatsogolera ku mitsinje yamadzi mʼnjira yosalala mmene sadzapunthwamo. Chifukwa ndine abambo ake a Israeli, ndipo Efereimu ndi mwana wanga woyamba.
他们要哭泣而来。 我要照他们恳求的引导他们, 使他们在河水旁走正直的路, 在其上不致绊跌; 因为我是以色列的父, 以法莲是我的长子。
10 “Imvani mawu a Yehova inu anthu a mitundu ina; lalikirani mawuwa kwa anthu a mayiko akutali a mʼmbali mwa nyanja; ‘Iye amene anabalalitsa Israeli adzawasonkhanitsanso ndipo adzayangʼanira nkhosa zake ngati mʼbusa.’
列国啊,要听耶和华的话, 传扬在远处的海岛说: 赶散以色列的必招聚他, 又看守他,好像牧人看守羊群。
11 Pakuti Yehova wawombola fuko la Yakobo anawapulumutsa mʼdzanja la anthu owaposa mphamvu.
因耶和华救赎了雅各, 救赎他脱离比他更强之人的手。
12 Anthuwo adzabwera akuyimba mofuwula pa mapiri a Ziyoni; adzasangalala ndi zinthu zabwino zochokera kwa Yehova. Zinthu zabwinozo ndi izi: tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta, ana ankhosa ndi ana angʼombe. Iwo adzakhala ngati munda wothiriridwa bwino, ndipo sadzamvanso chisoni.
他们要来到锡安的高处歌唱, 又流归耶和华施恩之地, 就是有五谷、新酒,和油, 并羊羔、牛犊之地。 他们的心必像浇灌的园子; 他们也不再有一点愁烦。
13 Pamenepo anamwali adzavina ndi kusangalala. Anyamata ndi okalamba nawonso adzasangalala. Kulira kwawo ndidzakusandutsa chisangalalo; ndidzawasangalatsa nʼkuchotsa chisoni chawo.
那时,处女必欢乐跳舞; 年少的、年老的,也必一同欢乐; 因为我要使他们的悲哀变为欢喜, 并要安慰他们,使他们的愁烦转为快乐。
14 Ansembe ndidzawadyetsa chakudya chabwino, ndipo anthu anga adzakhuta ndi zabwino zanga,” akutero Yehova.
我必以肥油使祭司的心满足; 我的百姓也要因我的恩惠知足。 这是耶和华说的。
15 Yehova akuti, “Kulira kukumveka ku Rama, kulira kwakukulu, Rakele akulirira ana ake. Sakutonthozeka chifukwa ana akewo palibe.”
耶和华如此说: 在拉玛听见号咷痛哭的声音, 是拉结哭她儿女,不肯受安慰, 因为他们都不在了。
16 Yehova akuti, “Leka kulira ndi kukhetsa misozi pakuti udzalandira mphotho ya ntchito yako,” akutero Yehova. “Iwo adzabwerako ku dziko la adani.
耶和华如此说: 你禁止声音不要哀哭, 禁止眼目不要流泪, 因你所做之工必有赏赐; 他们必从敌国归回。 这是耶和华说的。
17 Tsono chiyembekezo chilipo pa zamʼtsogolo,” akutero Yehova. “Ana ako adzabwerera ku dziko lawo.
耶和华说:你末后必有指望; 你的儿女必回到自己的境界。
18 “Ndithu ndamva Efereimu akubuwula kuti, ‘Ife tinali ngati ana angʼombe osamva. Koma inu mwatiphunzitsa kumvera. Mutibweze kuti tithe kubwerera, chifukwa ndinu Yehova Mulungu wanga.
我听见以法莲为自己悲叹说: 你责罚我,我便受责罚, 像不惯负轭的牛犊一样。 求你使我回转,我便回转, 因为你是耶和华—我的 神。
19 Popeza tatembenuka mtima, ndiye tikumva chisoni; popeza tazindikira ndiye tikudziguguda pachifukwa. Tachita manyazi ndipo tanyazitsidwa chifukwa tinachimwa paubwana wathu.’
我回转以后就真正懊悔; 受教以后就拍腿叹息; 我因担当幼年的凌辱就抱愧蒙羞。
20 Kodi Efereimu si mwana wanga wokondedwa, mwana amene Ine ndimakondwera naye? Ngakhale nthawi zambiri ndimamudzudzula, ndimamukumbukirabe. Kotero mtima wanga ukumufunabe; ndimamumvera chifundo chachikulu kwambiri,” akutero Yehova.
耶和华说:以法莲是我的爱子吗? 是可喜悦的孩子吗? 我每逢责备他,仍深顾念他; 所以我的心肠恋慕他; 我必要怜悯他。
21 “Muyike zizindikiro za mu msewu; muyimike zikwangwani. Yangʼanitsitsani msewuwo, njira imene mukuyendamo. Bwerera, iwe namwali wa Israeli, bwerera ku mizinda yako ija.
以色列民哪, 你当为自己设立指路碑, 竖起引路柱。 你要留心向大路, 就是你所去的原路; 你当回转,回转到你这些城邑。
22 Udzakhala jenkha mpaka liti, iwe mwana wa mkazi wosakhulupirika? Yehova walenga chinthu chatsopano pa dziko lapansi; mkazi ndiye tsopano aziteteza mwamuna.”
背道的民哪, 你反来复去要到几时呢? 耶和华在地上造了一件新事, 就是女子护卫男子。
23 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Ndikadzabwera nawo anthuwa kuchokera ku ukapolo, anthu a mʼdziko la Yuda ndi amene akukhala mʼmizinda yake adzayankhulanso mawu akuti, ‘Yehova akudalitse, iwe malo achilungamo, iwe phiri lopatulika.’
万军之耶和华—以色列的 神如此说:“我使被掳之人归回的时候,他们在犹大地和其中的城邑必再这样说: 公义的居所啊, 圣山哪,愿耶和华赐福给你。
24 Anthu adzakhala ku Yuda ndi ku mizinda yake pamodzi ndi alimi ndi oweta nkhosa.
犹大和属犹大城邑的人,农夫和放羊的人,要一同住在其中。
25 Ndidzatsitsimutsa anthu otopa ndipo ndidzadyetsa anthu anjala.”
疲乏的人,我使他饱饫;愁烦的人,我使他知足。”
26 Pamenepo ndinadzuka nʼkuyangʼana uku ndi uku. Tulo tanga tinali tokoma.
先知说:“我醒了,觉着睡得香甜!”
27 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachulukitsa anthu pamodzi ndi ziweto mʼdziko la Israeli ndi la Yuda.
耶和华说:“日子将到,我要把人的种和牲畜的种播种在以色列家和犹大家。
28 Monga momwe ndinasamalira powazula, powagwetsa, powagumula, powawononga ndi powachita zoyipa, momwemonso ndidzasamala powamanga ndi powadzala” akutero Yehova.
我先前怎样留意将他们拔出、拆毁、毁坏、倾覆、苦害,也必照样留意将他们建立、栽植。这是耶和华说的。
29 “Mʼmasiku amenewo anthu sadzanenanso kuti, “Makolo adya mphesa zosapsa, koma mano a ana ndiye achita dziru.
当那些日子,人不再说: 父亲吃了酸葡萄, 儿子的牙酸倒了。
30 Mʼmalo wake, munthu aliyense adzafa chifukwa cha tchimo lake. Iye amene adzadye mphesa zosapsazo ndiye amene mano ake adzachite dziru.”
但各人必因自己的罪死亡;凡吃酸葡萄的,自己的牙必酸倒。”
31 “Masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzachita pangano latsopano ndi Aisraeli ndiponso nyumba ya Yuda.
耶和华说:“日子将到,我要与以色列家和犹大家另立新约,
32 Silidzakhala ngati pangano limene ndinachita ndi makolo awo pamene ndinawagwira padzanja nʼkuwatulutsa ku Igupto; chifukwa anaphwanya pangano langa, ngakhale ndinali mwamuna wawo,” akutero Yehova.
不像我拉着他们祖宗的手,领他们出埃及地的时候,与他们所立的约。我虽作他们的丈夫,他们却背了我的约。这是耶和华说的。”
33 “Ili ndi pangano limene ndidzachita ndi Aisraeli atapita masiku amenewo,” akutero Yehova. “Ndidzayika lamulo langa mʼmitima mwawo ndi kulilemba mʼmaganizo mwawo. Ine ndidzakhala Mulungu wawo ndipo iwo adzakhala anthu anga.
耶和华说:“那些日子以后,我与以色列家所立的约乃是这样:我要将我的律法放在他们里面,写在他们心上。我要作他们的 神,他们要作我的子民。
34 Sipadzafunikanso kuti wina aphunzitse mnzake, kapena munthu wina kuphunzitsa mʼbale wake, kunena kuti, ‘Mudziwe Yehova,’ chifukwa onse adzandidziwa Ine, kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu,” akutero Yehova. “Ndidzawakhululukira zoyipa zawo ndipo sindidzakumbukiranso machimo awo.”
他们各人不再教导自己的邻舍和自己的弟兄说:‘你该认识耶和华’,因为他们从最小的到至大的都必认识我。我要赦免他们的罪孽,不再记念他们的罪恶。这是耶和华说的。”
35 Yehova akuti, Iye amene amakhazikitsa dzuwa kuti liziwala masana, amene amalamula kuti mwezi ndi nyenyezi ziziwala usiku, amene amavundula nyanja kuti mafunde akokome, dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
那使太阳白日发光, 使星月有定例,黑夜发亮, 又搅动大海,使海中波浪匉訇的, 万军之耶和华是他的名。 他如此说:
36 Ngati zimenezi zilekeka pamaso panga, akutero Yehova, pamenepo padzakhala pamathero a fuko la Israeli pamaso panga.
这些定例若能在我面前废掉, 以色列的后裔也就在我面前断绝, 永远不再成国。 这是耶和华说的。
37 Yehova akuti, “Ndidzataya fuko la Israeli chifukwa cha machimo awo. Ngati patapezeka munthu amene angathe kupima zakuthambo nʼkufufuza maziko a dziko lapansi.”
耶和华如此说: 若能量度上天, 寻察下地的根基, 我就因以色列后裔一切所行的弃绝他们。 这是耶和华说的。
38 “Taonani masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene mzinda wa Yehova udzamangidwanso kuyambira ku Nsanja ya Hananeli mpaka ku Chipata cha Ngodya.
耶和华说:“日子将到,这城必为耶和华建造,从哈楠业楼直到角门。
39 Malire ake adzayambira pamenepo kupita ku phiri la Garebu, nʼkudzakhota kuloza ku Gowa.
准绳要往外量出,直到迦立山,又转到歌亚。
40 Chigwa chonse mʼmene amatayiramo mitembo ndi phulusa, ndiponso minda yonse kuyambira ku Chigwa cha Kidroni mpaka ku ngodya ya Chipata cha Akavalo mbali ya kummawa, adzakhala malo opatulika a Yehova. Mzindawu sadzawuzulanso kapena kuwuwononga.”
抛尸的全谷和倒灰之处,并一切田地,直到汲沦溪,又直到东方马门的拐角,都要归耶和华为圣,不再拔出,不再倾覆,直到永远。”