< Yeremiya 30 >

1 Yehova anawuza Yeremiya kuti,
The word that came to Jeremiah from the LORD, saying,
2 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
Thus speaketh the LORD, the God of Israel, saying, Write thee all the words that I have spoken unto thee in a book.
3 Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
For, lo, the days come, saith the LORD, that I will turn again the captivity of my people Israel and Judah, saith the LORD: and I will cause them to return to the land that I gave to their fathers, and they shall possess it.
4 Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
And these are the words that the LORD spake concerning Israel and concerning Judah.
5 “Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
For thus saith the LORD: We have heard a voice of trembling, of fear, and not of peace.
6 Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
Ask ye now, and see whether a man doth travail with child: wherefore do I see every man with his hands on his loins, as a woman in travail, and all faces are turned into paleness?
7 Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
Alas! for that day is great, so that none is like it: it is even the time of Jacob’s trouble; but he shall be saved out of it.
8 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
And it shall come to pass in that day, saith the LORD of hosts, that I will break his yoke from off thy neck, and will burst thy bands; and strangers shall no more serve themselves of him:
9 Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
but they shall serve the LORD their God, and David their king, whom I will raise up unto them.
10 “‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
Therefore fear thou not, O Jacob my servant, saith the LORD; neither be dismayed, O Israel: for, lo, I will save thee from afar, and thy seed from the land of their captivity; and Jacob shall return, and shall be quiet and at ease, and none shall make him afraid.
11 Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
For I am with thee, saith the LORD, to save thee: for I will make a full end of all the nations whither I have scattered thee, but I will not make a full end of thee; but I will correct thee with judgment, and will in no wise leave thee unpunished.
12 Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
For thus saith the LORD, Thy hurt is incurable, and thy wound grievous.
13 Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
There is none to plead thy cause, that thou mayest be bound up: thou hast no healing medicines.
14 Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
All thy lovers have forgotten thee; they seek thee not: for I have wounded thee with the wound of an enemy, with the chastisement of a cruel one; for the greatness of thine iniquity, because thy sins were increased.
15 Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
Why criest thou for thy hurt? thy pain is incurable: for the greatness of thine iniquity, because thy sins were increased, I have done these things unto thee.
16 “Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
Therefore all they that devour thee shall be devoured; and all thine adversaries, every one of them, shall go into captivity; and they that spoil thee shall be a spoil, and all that prey upon thee will I give for a prey.
17 Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
For I will restore health unto thee, and I will heal thee of thy wounds, saith the LORD; because they have called thee an outcast, [saying], It is Zion, whom no man seeketh after.
18 Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
Thus saith the LORD: Behold, I will turn again the captivity of Jacob’s tents, and have compassion on his dwelling places; and the city shall be builded upon her own heap, and the palace shall remain after the manner thereof.
19 Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
And out of them shall proceed thanksgiving and the voice of them that make merry: and I will multiply them, and they shall not be few; I will also glorify them, and they shall not be small.
20 Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
Their children also shall be as aforetime, and their congregation shall be established before me, and I will punish all that oppress them.
21 Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
And their prince shall be of themselves, and their ruler shall proceed from the midst of them; and I will cause him to draw near, and he shall approach unto me: for who is he that hath had boldness to approach unto me? saith the LORD.
22 “Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
And ye shall be my people, and I will be your God.
23 Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
Behold, the tempest of the LORD, [even his] fury, is gone forth, a sweeping tempest: it shall burst upon the head of the wicked.
24 Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.
The fierce anger of the LORD shall not return, until he have executed, and till he have performed the intents of his heart: in the latter days ye shall understand it.

< Yeremiya 30 >