< Yeremiya 30 >

1 Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Ma e wach mane obirone Jeremia koa kuom Jehova Nyasaye:
2 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Lemba mʼbuku mawu onse amene ndakuwuza.
“Ma e gima Jehova Nyasaye, Nyasach Israel, wacho: ‘Ndik e kitabu weche duto masewachoni.’
3 Nthawi ikubwera pamene ndidzachotse anthu anga, Israeli ndi Yuda kuchokera ku ukapolo ndi kuwabwezera dziko limene ndinapatsa makolo awo,’ akutero Yehova.”
Jehova Nyasaye wacho niya, ‘Ndalo biro ma anaduog joga Israel kod Juda koa e twech kendo achokgi e piny mane amiyo kweregi mondo okaw,’ Jehova Nyasaye owacho.”
4 Nawa mawu amene Yehova anayankhula ndi anthu a ku Israeli ndi Yuda:
Magi e weche mane Jehova Nyasaye owacho kuom Israel gi Juda:
5 “Yehova akuti: “Ndamva kulira chifukwa cha nkhawa, ndamva kulira kwa mantha popeza palibe mtendere.
“Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “‘Ywak mar luoro winjore, en bwok malich, to ok kwe.
6 Tsono khalani pansi ndi kudzifunsa kuti: Kodi munthu wamwamuna angathe kubereka mwana? Nanga nʼchifukwa chiyani ndikuona munthu aliyense wamwamuna atagwira manja ake pa mimba pake ngati mayi pa nthawi yake yochira? Chifukwa chiyani nkhope iliyonse ili yakugwa?
Koro lingʼuru mondo uparane: Bende dichwo nyalo nywolo nyithindo? To kare angʼo momiyo aneno dichwo ka dichwo maratego, komako iye ka dhako mamuoch kayo, ka luoro omakogi ka joma chiegni tho?
7 Mayo ine! Tsiku limeneli ndi lalikulu kwambiri! Sipadzakhala lina lofanana nalo. Idzakhala nthawi ya masautso kwa Yakobo, koma adzapulumuka ku masautsowo.”
Mano kaka odiechiengʼno nobed malich! Onge manochal kode. Enobed kinde mag chandruok ne Jakobo, to norese.’”
8 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Pa tsiku limenelo, ndidzathyola goli la ukapolo mʼkhosi mwawo ndipo ndidzadula zingwe zowamanga; Aisraeli sadzakhalanso akapolo a alendo.
Jehova Nyasaye Maratego wacho niya, “‘E odiechiengʼno anatur jok manie ngʼutgi, kendo anachod nyoroche motwegigo; joma welo ok nochak oketgi wasumbini mag-gi kendo.
9 Mʼmalo mwake, adzatumikira Yehova Mulungu wawo ndiponso Davide mfumu yawo, amene ndidzawasankhira.
To kata kamano ginitine Jehova Nyasaye ma Nyasachgi kod Daudi ruodhgi, ma anamigi.
10 “‘Tsono usachite mantha, iwe mtumiki wanga Yakobo; usade nkhawa, iwe Israeli,’ akutero Yehova. ‘Ndithu ndidzakupulumutsa kuchokera ku dziko lakutali, zidzukulu zako kuchokera ku dziko la ukapolo wawo. Yakobo adzabwerera ndipo adzakhala modekha pa mtendere, ndipo palibe amene adzamuchititsa mantha.
“‘Omiyo kik iluor, yaye Jakobo jatichna; kik ibwogi, yaye Israel,’ Jehova Nyasaye owacho. ‘Adier anaresi kia e piny mabor, in kaachiel gi nyikwayi koaye piny motwegie. Jakobo nobed gi kwe kendo norite maonge ngʼama nomiye luoro.
11 Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani,’ akutero Yehova. ‘Ngakhale ndidzawononga kotheratu mitundu yonse ya anthu kumene ndinakubalalitsirani, koma inu sindidzakuwonongani kotheratu. Sindidzakulekani kuti mukhale osalangidwa. Koma ndidzakulangani mwachilungamo.’”
Anabed kodi kendo anaresi,’ Jehova Nyasaye wacho. ‘Kata obedo ni atieko chuth ogendini duto ma akeyou e diergi, ok anatieki chuth. Anakumu ka angʼadonu bura makare; ok anaweu ma ok akumou.’
12 Yehova akuti, “Chilonda chanu nʼchosachizika, bala lanu ndi lonyeka.
“Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “‘Adhola mari ok nyal thiedhi, hinyruok mari okalo chango.
13 Palibe amene angathe kukutetezani pa mlandu wanu, palibe chiyembekezo choti inu nʼkuchira, palibe mankhwala ochiritsa inu.
Onge ngʼama nyalo chiwo kwayoni kari, kendo onge gima nyalo thiedhoni adhola, kata manyalo changi.
14 Abwenzi anu onse akuyiwalani; sasamalanso za inu. Ndakukanthani ngati mmene mdani akanachitira. Ndipo ndakulangani mwa nkhanza, chifukwa machimo anu ndi ambiri, ndipo kulakwa kwanu ndi kwakukulu.
Joma ne osiepeni duto wigi osewil kodi; kendo ok gidewi. Asegoyi mana ka jasigu kendo kumi mana ka ngʼama kwiny, nikech ketho mari duongʼ kendo richoni ngʼeny.
15 Chifukwa chiyani mukulira nacho chilonda chanu? Bala lanu silingapole ayi. Ine ndakuchitani zimenezi chifukwa machimo anu ndi ambiri ndipo kulakwa kwanu nʼkwakukulu.
Angʼo momiyo iywak kuom adhondi, to in-gi rem ma ok thiedhre? Asekumou kamano nikech richou ngʼeny, kendo nikech timbeu maricho lich.
16 “Tsono onse amene anakuwonongani, nawonso adzawonongedwa; adani anu onse adzapita ku ukapolo. Iwo amene anafunkha zinthu zanu, zinthu zawo zidzafunkhidwanso; onse amene anakusakazani nawonso adzasakazidwa.
“‘To jogo duto motiekou notieki; wasiku duto noter e twech. Jogo momayou nomagi; jogo moketonu obadho anaketnegi obadho.
17 Ndidzachiza matenda anu ndi kupoletsa zilonda zanu, akutero Yehova, ‘chifukwa mukutchedwa anthu otayika. Amati, ndi anthu a ku Ziyoni awa amene alibe wowasamala.’”
Anamiyi ngima maber kendo anathiedh adhondeni,’ Jehova Nyasaye ema owacho, ‘nikech iluongi ni ngʼama owit oko, Sayun maonge ngʼama dewo.’
18 Yehova akuti, “Ndidzabwera nalo banja la Yakobo ku dziko lawo ndipo ndidzachitira chifundo malo ake okhalamo; mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso pa bwinja pake, nyumba yaufumu idzamangidwanso pa malo pake penipeni.
“Ma e gima Jehova Nyasaye wacho: “‘Anaduog mwandu mag hembe Jakobo kendo abed gi ngʼwono e kuondege mag dak; dala maduongʼ noger kendo e kuondege mano okethe, kendo kar dak ruoth noger e kare malongʼo.
19 Anthuwo adzayimba nyimbo zoyamika Yehova ndipo kudzamveka phokoso lachisangalalo. Ndidzawachulukitsa, ndipo chiwerengero chawo sichidzatsika; ndidzawapatsa ulemerero, ndipo sadzanyozedwanso.
Jogi nodwok erokamano ka giwer kendo ka gikok gi mor. Anamed kwan mag-gi, kendo ok ginidog chien; mi anamigi duongʼ, kendo ok nokawgi matin.
20 Ana awo adzakhalanso monga mmene analili kale, ndipo gulu lawo ndidzalikhazikitsa pamaso panga; ndidzalanga onse owazunza.
Nyithindgi nochal kaka e ndalo machon, kendo anagur anywolagi motegno, mi anakum jogo duto ma thirogi.
21 Mtsogoleri wawo adzakhala mmodzi mwa iwo. Wodzawalamulira adzachokera pakati pawo. Choncho ndidzawakokera kufupi ndi Ine ndipo iye adzandiyandikira. Ndani angalimbe mtima payekha kuyandikana nane popanda kuyitanidwa?” akutero Yehova.
Jatendgi nobed achiel kuomgi; jatendgi noa e diergi. Anakele machiegni kendo enobi machiegni koda, nimar en ngʼa manyalo chiwore, mondo obed machiegni koda?’” Jehova Nyasaye ema owacho.
22 “Choncho inu mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.”
“‘Omiyo unubed joga, kendo anabed Nyasachu.’”
23 Taonani ukali wa Yehova wowomba ngati mphepo ya mkuntho. Mphepo ya namondwe ikuwomba pa mitu ya anthu oyipa.
Neuru, apaka mar Jehova Nyasaye biro mwomore gi mirimbe, yamo mafuto malich ka futo e wiye joma timbegi mono.
24 Mkwiyo woopsa wa Yehova sudzachoka mpaka atakwaniritsa zolinga za mu mtima mwake. Mudzamvetsa zimenezi masiku akubwerawo.
Mirima mager mar Jehova Nyasaye ok nodog chien nyaka one ni ochopo dwaro mar chunye. E ndalo ma biro iniwinj tiend wachni.

< Yeremiya 30 >