< Yeremiya 3 >
1 “Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
« On dit: « Si un homme répudie sa femme, qu'elle s'éloigne de lui et devient la propriété d'un autre homme, doit-il revenir à elle? ». Cette terre ne serait-elle pas grandement polluée? Mais toi, tu t'es prostitué avec plusieurs amants, et tu reviendras vers moi, dit Yahvé.
2 “Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
« Lève tes yeux vers les hauteurs dénudées, et regarde! Où n'as-tu pas été couché? Tu les as attendus au bord du chemin, comme un Arabe dans le désert. Tu as souillé le pays par ta prostitution et par ta méchanceté.
3 Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
C'est pourquoi les pluies ont été retenues, et il n'y a pas eu d'arrière-saison; mais tu as eu le front d'une prostituée, et tu n'as pas voulu avoir honte.
4 Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
Ne me crieras-tu pas dès maintenant: « Mon Père, tu es le guide de ma jeunesse »?
5 kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
« Gardera-t-il toujours sa colère? La gardera-t-il jusqu'à la fin? Voici que vous avez parlé et fait des choses mauvaises, et que vous avez fait ce que vous vouliez. »
6 Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
Et Yahvé m'a dit, au temps du roi Josias: « As-tu vu ce qu'a fait l'infidèle Israël? Elle est montée sur toute haute montagne et sous tout arbre vert, et elle s'y est prostituée.
7 Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
J'ai dit, après qu'elle eut fait toutes ces choses: « Elle reviendra vers moi »; mais elle n'est pas revenue, et sa perfide sœur Juda l'a vu.
8 Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
J'ai vu que lorsque, pour cette même raison, Israël rebelle avait commis un adultère, je l'ai répudiée et lui ai donné un certificat de divorce, la perfide Juda, sa sœur, n'a pas eu peur, mais elle est aussi allée se prostituer.
9 Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
Parce qu'elle s'est prostituée à la légère, le pays a été souillé, et elle a commis l'adultère avec des pierres et avec du bois.
10 Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
Et à cause de tout cela, Juda, sa sœur perfide, n'est pas revenue à moi de tout son cœur, mais seulement en faisant semblant, dit l'Éternel.
11 Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
L'Éternel m'a dit: « L'infidèle Israël s'est montré plus juste que le perfide Juda.
12 Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
Va, proclame ces paroles vers le nord, et dis: « Reviens, Israël rebelle, dit l'Éternel; je ne regarderai pas avec colère contre toi, car je suis miséricordieux, dit l'Éternel. Je ne garderai pas ma colère pour toujours.
13 Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
Reconnais seulement ton iniquité, parce que tu as transgressé l'Éternel, ton Dieu, et que tu as dispersé tes voies parmi les étrangers, sous tout arbre vert, et que tu n'as pas écouté ma voix, dit l'Éternel.
14 “Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
« Revenez, enfants rebelles, dit Yahvé, car je suis votre mari. Je prendrai l'un de vous dans une ville, et deux dans une famille, et je vous amènerai à Sion.
15 Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
Je vous donnerai des bergers selon mon cœur, qui vous paîtront avec connaissance et intelligence.
16 Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
En ces jours-là, quand vous serez nombreux et que vous vous multiplierez dans le pays, dit l'Éternel, on ne dira plus: « L'arche de l'alliance de l'Éternel ». Ils ne s'en souviendront pas. Ils ne s'en souviendront pas. Elle ne leur manquera pas, et il n'y en aura pas d'autre.
17 Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
En ce temps-là, on appellera Jérusalem « le trône de Yahvé », et toutes les nations seront rassemblées autour d'elle, autour du nom de Yahvé, autour de Jérusalem. Elles ne marcheront plus selon l'obstination de leur mauvais cœur.
18 Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
En ces jours-là, la maison de Juda marchera avec la maison d'Israël, et elles viendront ensemble du pays du nord au pays que j'ai donné en héritage à vos pères.
19 “Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
« Mais moi, j'ai dit: « Comme je veux te mettre au milieu des enfants, et te donner un pays agréable, un bel héritage des armées des nations! » Et j'ai dit: « Tu m'appelleras « mon père », et tu ne te détourneras pas de moi ».
20 Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
« Comme une femme abandonne son mari par trahison, ainsi vous m'avez trahi, maison d'Israël », dit l'Éternel.
21 Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
Une voix se fait entendre sur les hauteurs dénudées, Les pleurs et les supplications des enfants d'Israël; Car ils ont perverti leur voie, Ils ont oublié Yahvé, leur Dieu.
22 Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
Revenez, enfants égarés, et je guérirai votre égarement. « Voici, nous sommes venus à toi, car tu es Yahvé notre Dieu.
23 Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
En vérité, le secours des collines, le tumulte des montagnes, c'est en vain. C'est en Yahvé notre Dieu que réside le salut d'Israël.
24 Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
Mais l'ignominie a dévoré le travail de nos pères dès notre jeunesse, leurs troupeaux et leurs bêtes, leurs fils et leurs filles.
25 Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”
Couchons-nous dans notre honte, et que notre confusion nous couvre; car nous avons péché contre Yahvé notre Dieu, nous et nos pères, depuis notre jeunesse jusqu'à ce jour. Nous n'avons pas obéi à la voix de Yahvé notre Dieu. »