< Yeremiya 3 >

1 “Ngati munthu asudzula mkazi wake ndipo mkaziyo nʼkuchoka nakakwatiwa ndi mwamuna wina, kodi mwamuna woyambayo angathe kumutenganso mkaziyo? Kodi atatero sindiye kuti dzikolo layipitsidwa kwambiri? Koma iwe Israeli wachita zadama ndi zibwenzi zambiri. Komabe bwerera kwa ine,” akutero Yehova.
One could say, Behold, if a man send away his wife, and she go from him, and become another man's, can he return unto her again? would not that land be greatly polluted? and thou hast played the harlot with many companions, and wilt yet return to me, saith the Lord.
2 “Tayangʼana ku zitunda zowuma. Kodi aliponso malo ena amene iwe sunachitepo zadama? Iwe unkakhala mʼmbali mwa njira kumadikira zibwenzi zako, ngati Mluya wobisalira anthu mʼchipululu. Inu mwayipitsa dziko ndi zadama zanu ndi ntchito zanu zoyipa.
Lift up thy eyes unto the mountain-tops, and see where thou hast not been lain with. On public roads hast thou sat for them, as the Arab in the wilderness; and thou hast polluted the land with thy incests and with thy wickedness.
3 Nʼchifukwa chake Yehova wayimitsa mvula, ndipo mvula ya nthawi ya masika sinagwe. Komabe uli ndi maonekedwe a mkazi wachiwerewere; ndipo sukuchita manyazi ndi pangʼono pomwe.
And [though] the early showers were withholden, and the latter rain came not: yet hadst thou a forehead of an incestuous wife, thou refusedst to feel shame.
4 Kodi iwe siposachedwa pomwepa pamene wanena kuti, ‘Abambo anga, Inu bwenzi langa la unyamata wanga,
Wilt thou not from this time call out unto mem My father, the guide of my youth art thou?
5 kodi mudzandikwiyira nthawi zonse? Kodi ukali wanu udzakhalabe mpaka muyaya?’ Umu ndimo mmene umayankhulira, koma umapitirizabe kuchita zoyipa monga momwe umathera.”
Will he bear grudge for ever? will he keep it to eternity? Behold, thou hast spoken [this], and yet hast done the things that are evil as much as thou wast able.
6 Pa nthawi ya Mfumu Yosiya Yehova anandiwuza kuti, “Kodi waona zomwe Israeli wosakhulupirika uja wachita? Anakwera pa phiri lililonse lalitali ndi kupita pa tsinde pa mtengo uliwonse wogudira kukapembedza. Choncho anachita za chiwerewere kumeneko.
And the Lord said unto me in the days of Josiah the king, Hast thou seen what backsliding Israel hath done? she is gone upon every high mountain and under every green tree, and hath played the harlot there.
7 Ndinaganiza kuti atachita zonsezi, adzabwerera kwa Ine, koma sanabwerere, ndipo mlongo wake wosakhulupirika uja, Yuda, anaziona zimenezi.
And I thought that after she had done all these things, she would return unto me. But she returned not. And this saw her treacherous sister Judah.
8 Anaona kuti ndinasudzula Israeli wosakhulupirikayo ndi kumupirikitsa chifukwa cha zigololo zake. Komabe Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanaope, nayenso anapita kukachita chigololo.
And I saw, that, although because backsliding Israel had committed adultery, I had sent her away, and given her bill of divorce unto her, still treacherous Judah her sister feared not, but went and played herself the harlot also.
9 Chiwerewere cha Israeli chinali chochititsa manyazi kotero kuti chinayipitsa dziko lonse. Anachita chigololo popembedza mafano a miyala ndi mitengo.
And it came to pass through her giddy incest, that she defiled the land, and committed adultery with stone and with wood.
10 Israeli atachita zonsezi, Yuda mʼbale wake wosakhulupirika uja sanabwerere kwa Ine ndi mtima wake wonse, koma mwachiphamaso chabe,” akutero Yehova.
And yet with all this her treacherous sister Judah hath not returned unto me with all her heart, but with falsehood, saith the Lord.
11 Yehova anandiwuza kuti, “Kusakhulupirika kwa Israeli nʼkochepa kuyerekeza ndi kusakhulupirika kwa Yuda.
And the Lord said unto me, The backsliding Israel hath justified herself through the treacherous Judah.
12 Pita ukalalikire kumpoto uthenga wakuti, “‘Israeli wosakhulupirikawe, bwerera,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukalipira mpaka kalekale, pakuti ndine wachifundo,’ akutero Yehova. ‘Sindidzakukwiyira mpaka kalekale.
Go and proclaim these words toward the north, and say, Return, thou backsliding Israel, saith the Lord: I will not cause my anger to fall upon you; for I am full of kindness, saith the Lord, I will not hear grudge for ever.
13 Ungovomera kulakwa kwako kuti unawukira Yehova Mulungu wako. Vomera kuti unayendayenda kukapembedza milungu yachilendo pansi pa mtengo uliwonse wogudira, ndiponso kuti sunandimvere,’” akutero Yehova.
Only acknowledge thy iniquity, that against the Lord thy God thou hast rebelled, and hast scattered thy ways to the strangers under every green tree, and that unto my voice ye have not hearkened, saith the Lord.
14 “Bwererani, ana osakhulupirika, pakuti ndine mbuye wanu,” akutero Yehova. “Ndinakusankhani, mmodzimmodzi kuchokera ku mudzi uliwonse ndiponso awiriawiri kuchokera ku banja lililonse.
Return, O backsliding children, saith the Lord; for I am become your husband; and I will take you one of a city, and two of a family, and bring you to Zion:
15 Ndipo ndidzakupatsani abusa a pamtima panga amene adzakutsogolerani mwanzeru ndi mwaluntha.
And I will give you shepherds after my own heart, and they shall feed you with knowledge and intelligence.
16 Masiku amenewo mukadzachulukana kwambiri mʼdzikomo, anthu sadzanenanso za ‘Bokosi la Chipangano la Yehova’ kapena kuliganizira. Sadzalikumbukiranso kapena kulifuna, ndipo sadzapanganso lina,” akutero Yehova.
And it shall come to pass, when ye multiply and increase in the land, in those days, saith the Lord, that men shall not say any more, “The ark of the covenant of the Lord;” nor shall it come any more to mind; nor shall they remember it; nor shall they mention it; nor shall any thing be done any more [with it].
17 Nthawi imeneyo adzatcha Yerusalemu Mpando Waufumu wa Yehova, ndipo mitundu yonse ya anthu idzasonkhana mu Yerusalemu pamaso pa Yehova. Sadzawumiriranso kutsata mitima yawo yoyipa.
At that time shall they call Jerusalem, The throne of the Lord; and all the nations shall be gathered unto it, to the name of the Lord, to Jerusalem: and they shall not walk any more after the stubbornness of their evil heart.
18 Masiku amenewo fuko la Yuda lidzaphatikizana ndi fuko la Israeli, onse pamodzi adzachokera ku dziko la kumpoto kupita ku dziko limene ndinapatsa makolo awo, kuti likhale cholowa.
In those days shall the house of Judah walk with the house of Israel, and they shall come together out of the land of the north unto the land that I have given for an inheritance unto your fathers.
19 “Ine mwini ndinati, “‘Ndikanakonda bwanji kukukhazikani pakati pa ana anga ndikukupatsani dziko labwino kwambiri, cholowa chokongola kwambiri kuposa cha mitundu ina ya anthu.’ Ndinaganiza kuti mudzanditcha Ine ‘Atate’ ndi kuti simudzaleka kunditsata.
But I had thought, How shall I establish thee among the [other] sons [of man], and give thee a desirable land, a heritage of glory of the hosts of nations? and I thought, My father thou wouldst call me, and that from me thou wouldst not turn away.
20 Koma monga mkazi wosakhulupirika amasiya mwamuna wake, momwemonso inu mwakhala osakhulupirika kwa Ine, inu fuko la Israeli,” akutero Yehova.
But truly as a wife treacherously departeth from her husband, so have ye dealt treacherously with me, O house of Israel, saith the Lord.
21 Mawu akumveka pa magomo, Aisraeli akulira ndi kupempha chifundo chifukwa anatsata njira zoyipa ndi kuyiwala Yehova Mulungu wawo.
A voice is now heard upon the mountain-tops, the supplicatory weeping of the children of Israel; for they have perverted their way, they have forgotten the Lord their God.
22 Inu mukuti, “Bwererani, anthu osakhulupirika; ndidzachiritsa kubwerera mʼmbuyo kwanu.” “Inde, tidzabwerera kwa Inu pakuti ndinu Yehova Mulungu wathu.
Return, ye backsliding children, I will heal your backslidings. “Behold, we come unto thee; for thou art the Lord our God.
23 Ndithu kupembedza pa magomo komanso kuchita maphwando pa mapiri zilibe phindu. Zoonadi chipulumutso cha Israeli chili mwa Yehova Mulungu wathu basi.
Truly deceptive was [what we hoped for] from the hills, and the multitude on the mountains; truly in the Lord our God is the salvation of Israel.
24 Kuyambira pa ubwana wathu milungu yochititsa manyazi ija yakhala ikutiwonongetsa phindu la ntchito za makolo athu, nkhosa ndi ngʼombe zawo, ana awo aamuna ndi aakazi.
And shame hath devoured the acquisition of our fathers from our youth, their flocks and their herds, their sons and their daughters.
25 Tilekeni tigone pansi mwa manyazi, ndipo kunyozeka kwathu kutiphimbe. Paja tachimwira Yehova Mulungu wathu, ife pamodzi ndi makolo athu kuyambira nthawi ya ubwana wathu mpaka lero lino sitinamvere Yehova Mulungu wathu.”
We lie down in our shame, and our confusion covereth us; for against the Lord our God have we sinned, we and our fathers, from our youth even until this day; and we have not hearkened to the voice of the Lord our God.”

< Yeremiya 3 >