< Yeremiya 29 >

1 Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
La ngamazwi encwadi umphrofethi uJeremiya ayithumela eseJerusalema ebadaleni abasindayo phakathi kwabathunjwayo lakubaphristi, abaphrofethi, lakubo bonke abantu uNebhukhadineza abathatha eJerusalema wabasa ekuthunjweni eBhabhiloni.
2 Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
(Lokhu kwakungemva kokuba inkosi uJekhoniya lendlovukazi engunina, izikhulu zasemthethwandaba kanye labadala bakoJuda labaseJerusalema, izingcitshi lezingcwethi basebeye ekuthunjweni besuka eJerusalema.)
3 Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
Incwadi leyo wayiphathisa u-Eleyasa indodana kaShafani loGemariya indodana kaHilikhiya, abathunywa nguZedekhiya inkosi yakoJuda kuNebhukhadineza eBhabhiloni. Yathi:
4 Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
UThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi kubo bonke labo engabasa ekuthunjweni eBhabhiloni besuka eJerusalema:
5 “Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
“Yakhani izindlu lihlale phansi; limani izivande lidle izithelo zazo.
6 Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
Thathani abafazi lizale amadodana lamadodakazi; dingelani amadodana enu abafazi lendise lamadodakazi enu, ukuze lawo abe lamadodana kanye lamadodakazi; inani lenu lande ngapho; lingehli.
7 Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
Funani ukuthula lokuphumelela kwedolobho engilise ekuthunjweni kulo. Likhulekeleni kuThixo, ngoba nxa liphumelela lani lizaphumelela.”
8 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
Ye, uThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi, “Lingavumeli ukuthi abaphrofethi labahlahluli abaphakathi kwenu balikhohlise. Lingawalaleli amaphupho elibakhuthaza ukuthi bawaphuphe.
9 Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
Baphrofetha amanga kini ngebizo lami. Kangibathumanga,” kutsho uThixo.
10 Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
UThixo uthi: “Lapho iminyaka engamatshumi ayisikhombisa isiphelile eBhabhiloni, ngizakuza kini ngigcwalise isithembiso sami somusa sokulibuyisela kule indawo.
11 Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
Ngoba ngiyawazi amacebo engilawo ngani,” kutsho uThixo, “amacebo okuliphumelelisa hatshi ukulilimaza, amacebo okulinika ithemba kanye lesikhathi esizayo.
12 Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
Ngalesosikhathi lizangibiza lizekhuleka kimi, njalo ngizalizwa.
13 Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
Lizangidinga lingifumane nxa lingidinga ngenhliziyo yenu yonke.
14 mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
Lizangifumana,” kutsho uThixo, “njalo ngizalibuyisa livela ekuthunjweni. Ngizaliqoqa ezizweni zonke lasezindaweni zonke engalixotshela kuzo,” kutsho uThixo, “njalo ngilibuyise endaweni engalithatha kuyo ngilisa ekuthunjweni.”
15 Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
Lingatsho lithi, “UThixo usesiphe abaphrofethi eBhabhiloni,”
16 koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
kodwa uThixo uthi mayelana lenkosi ehlala esihlalweni sobukhosi sikaDavida labantu bonke abasala kulelidolobho, abantu bakini abangahambanga lani ekuthunjweni,
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
yebo, uThixo uSomandla uthi, “Ngizabathumela inkemba, lendlala lesifo njalo ngizabenza babe njengomkhiwa obolileyo ongeke udliwe.
18 Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
Ngizaxotshana labo ngenkemba, ngendlala langesifo njalo ngizabenza benyanyeke kuyo yonke imibuso yasemhlabeni njalo babe yinto yokuqalekiswa lokwesatshwa, ukuklolodelwa lokuthukwa, phakathi kwezizwe zonke engibaxotshela kuzo.
19 Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
Ngoba kabawalalelanga amazwi ami,” kutsho uThixo, “amazwi engawathumela kubo njalonjalo ngezinceku zami abaphrofethi. Lani abasekuthunjweni kalilalelanga,” kutsho uThixo.
20 Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
Ngakho, zwanini ilizwi likaThixo, lonke lina elisekuthunjweni engalisusa eJerusalema ngalisa eBhabhiloni.
21 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
Mayelana lo-Ahabi indodana kaKholaya loZedekhiya indodana kaMaseya, abaphrofetha amanga kini ngebizo lami, uThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi: “Ngizabanikela kuNebhukhadineza inkosi yaseBhabhiloni ozababulala phambi kobuso benu.
22 Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
Ngenxa yabo, bonke abathunjiweyo abavela koJuda abaseBhabhiloni bazasebenzisa isiqalekiso lesi sokuthi: ‘UThixo makenze kini njengalokhu akwenze kuZedekhiya lo-Ahabi, abatshiswa yinkosi yaseBhabhiloni ngomlilo.’
23 Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
Ngoba benze izinto ezimbi kakhulu ko-Israyeli; bafeba labafazi babomakhelwane babo, baqamba amanga ngebizo lami, engingazange ngithi bakwenze. Ngiyakwazi njalo ngingufakazi kukho,” kutsho uThixo.
24 Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
Tshela uShemaya umNehelami uthi,
25 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
“UThixo uSomandla, uNkulunkulu ka-Israyeli uthi: ‘Wathumela izincwadi ngebizo lakho kubo bonke abantu baseJerusalema, lakuZefaniya indodana kaMaseya umphristi, lakwabanye abaphristi bonke.’ KuZefaniya wathi,
26 ‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
‘UThixo usekubeke ukuba ngumphristi esikhundleni sikaJehoyada ukuba ube ngumphathi wendlu kaThixo; umuntu ohlanyayo ozenza umphrofethi ubomfaka esitokisini umfake lezankosi zentanyeni.
27 Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
Pho kungani ungamkhuzanga uJeremiya wase-Anathothi, ozenza umphrofethi phakathi kwenu?
28 Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
Uthumele ilizwi leli kithi eBhabhiloni elithi: Kuzakuba yisikhathi eside. Ngakho yakhani izindlu lihlale phansi; limani izivande lidle izithelo zazo.’”
29 Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
Kodwa, uZefaniya umphristi incwadi le wayibalela uJeremiya umphrofethi.
30 Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Ilizwi likaThixo laselifika kuJeremiya lisithi,
31 “Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
“Thumela ilizwi leli kubo bonke abathunjiweyo uthi, Mayelana loShemaya umNehelami uThixo uthi: ‘Njengoba uShemaya esephrofitha kini, lanxa mina ngingamthumanga, walenza lakholwa amanga,
32 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.
ngeqiniso ngizamjezisa uShemaya umNehelami kanye lenzalo yakhe. Kakuyikuba lowakibo ozasala ekhona phakathi kwalababantu, njalo lezinto ezinhle engizazenzela abantu bami kasoze azibone, kutsho uThixo, ngoba uphrofetha ukungihlamukela.’”

< Yeremiya 29 >