< Yeremiya 29 >

1 Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
and these word [the] scroll: document which to send: depart Jeremiah [the] prophet from Jerusalem to(wards) remainder old: elder [the] captivity and to(wards) [the] priest and to(wards) [the] prophet and to(wards) all [the] people which to reveal: remove Nebuchadnezzar from Jerusalem Babylon [to]
2 Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
after to come out: come Jeconiah [the] king and [the] queen and [the] eunuch ruler Judah and Jerusalem and [the] artificer and [the] locksmith from Jerusalem
3 Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
in/on/with hand Elasah son: child Shaphan and Gemariah son: child Hilkiah which to send: depart Zedekiah king Judah to(wards) Nebuchadnezzar king Babylon Babylon [to] to/for to say
4 Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
thus to say LORD Hosts God Israel to/for all [the] captivity which to reveal: remove from Jerusalem Babylon [to]
5 “Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
to build house: home and to dwell and to plant garden and to eat [obj] fruit their
6 Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
to take: take woman: wife and to beget son: child and daughter and to take: take to/for son: child your woman: wife and [obj] daughter your to give: give(marriage) to/for human and to beget son: child and daughter and to multiply there and not to diminish
7 Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
and to seek [obj] peace: well-being [the] city which to reveal: remove [obj] you there [to] and to pray about/through/for her to(wards) LORD for in/on/with peace: well-being her to be to/for you peace: well-being
8 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
for thus to say LORD Hosts God Israel not to deceive to/for you prophet your which in/on/with entrails: among your and to divine your and not to hear: hear to(wards) dream your which you(m. p.) to dream
9 Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
for in/on/with deception they(masc.) to prophesy to/for you in/on/with name my not to send: depart them utterance LORD
10 Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
for thus to say LORD for to/for lip to fill to/for Babylon seventy year to reckon: visit [obj] you and to arise: establish upon you [obj] word: promised my [the] pleasant to/for to return: return [obj] you to(wards) [the] place [the] this
11 Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
for I to know [obj] [the] plot which I to devise: devise upon you utterance LORD plot peace: well-being and not to/for distress: evil to/for to give: give to/for you end and hope
12 Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
and to call: call to [obj] me and to go: come and to pray to(wards) me and to hear: hear to(wards) you
13 Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
and to seek [obj] me and to find for to seek me in/on/with all heart your
14 mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
and to find to/for you utterance LORD and to return: rescue [obj] (captivity your *Q(k)*) and to gather [obj] you from all [the] nation and from all [the] place which to banish [obj] you there utterance LORD and to return: return [obj] you to(wards) [the] place which to reveal: remove [obj] you from there
15 Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
for to say to arise: rise to/for us LORD prophet Babylon [to]
16 koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
for thus to say LORD to(wards) [the] king [the] to dwell to(wards) throne David and to(wards) all [the] people [the] to dwell in/on/with city [the] this brother: male-relative your which not to come out: come with you in/on/with captivity
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
thus to say LORD Hosts look! I to send: depart in/on/with them [obj] [the] sword [obj] [the] famine and [obj] [the] pestilence and to give: make [obj] them like/as fig [the] disgusting which not to eat from evil
18 Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
and to pursue after them in/on/with sword in/on/with famine and in/on/with pestilence and to give: make them (to/for horror *Q(K)*) to/for all kingdom [the] land: country/planet to/for oath and to/for horror: appalled and to/for hissing and to/for reproach in/on/with all [the] nation which to banish them there
19 Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
underneath: because of which not to hear: hear to(wards) word my utterance LORD which to send: depart to(wards) them [obj] servant/slave my [the] prophet to rise and to send: depart and not to hear: hear utterance LORD
20 Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
and you(m. p.) to hear: hear word LORD all [the] captivity which to send: depart from Jerusalem Babylon [to]
21 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
thus to say LORD Hosts God Israel to(wards) Ahab son: child Kolaiah and to(wards) Zedekiah son: child Maaseiah [the] to prophesy to/for you in/on/with name my deception look! I to give: give [obj] them in/on/with hand: power Nebuchadnezzar king Babylon and to smite them to/for eye your
22 Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
and to take: bring from them curse to/for all captivity Judah which in/on/with Babylon to/for to say to set: make you LORD like/as Zedekiah and like/as Ahab which to roast them king Babylon in/on/with fire
23 Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
because which to make folly in/on/with Israel and to commit adultery [obj] woman: wife neighbor their and to speak: speak word in/on/with name my deception which not to command them and I ([the] to know *Q(K)*) and witness utterance LORD
24 Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
and to(wards) Shemaiah [the] Nehelam to say to/for to say
25 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
thus to say LORD Hosts God Israel to/for to say because which you(m. s.) to send: depart in/on/with name your scroll: document to(wards) all [the] people which in/on/with Jerusalem and to(wards) Zephaniah son: child Maaseiah [the] priest and to(wards) all [the] priest to/for to say
26 ‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
LORD to give: make you priest underneath: instead Jehoiada [the] priest to/for to be overseer house: temple LORD to/for all man be mad and to prophesy and to give: put [obj] him to(wards) [the] stocks and to(wards) [the] stocks
27 Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
and now to/for what? not to rebuke in/on/with Jeremiah [the] Anathoth [the] to prophesy to/for you
28 Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
for as that: since as as to send: depart to(wards) us Babylon to/for to say long he/she/it to build house: home and to dwell and to plant garden and to eat [obj] fruit their
29 Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
and to call: read out Zephaniah [the] priest [obj] [the] scroll: document [the] this in/on/with ear: hearing Jeremiah [the] prophet
30 Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
and to be word LORD to(wards) Jeremiah to/for to say
31 “Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
to send: depart upon all [the] captivity to/for to say thus to say LORD to(wards) Shemaiah [the] Nehelam because which to prophesy to/for you Shemaiah and I not to send: depart him and to trust [obj] you upon deception
32 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.
to/for so thus to say LORD look! I to reckon: punish upon Shemaiah [the] Nehelam and upon seed: children his not to be to/for him man: anyone to dwell in/on/with midst [the] people [the] this and not to see: see in/on/with good which I to make: do to/for people my utterance LORD for revolt to speak: speak upon LORD

< Yeremiya 29 >