< Yeremiya 29 >

1 Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
And these [are] [the] words of the letter which he sent Jeremiah the prophet from Jerusalem to [the] remainder of [the] elders of the exile[s] and to the priests and to the prophets and to all the people which he had taken into exile Nebuchadnezzar from Jerusalem Babylon towards.
2 Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
After went out Jeconiah the king and the queen-mother and the court-officials [the] officials of Judah and Jerusalem and the craftsman and the smith from Jerusalem.
3 Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
By [the] hand of Eleasah [the] son of Shaphan and Gemariah [the] son of Hilkiah whom he sent Zedekiah [the] king of Judah to Nebuchadnezzar [the] king of Babylon Babylon towards saying.
4 Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel to all the exile[s] whom I sent into exile from Jerusalem Babylon towards.
5 “Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
Build houses and dwell and plant gardens and eat produce their.
6 Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
Take wives and father sons and daughters and take for sons your wives and daughters your give to husbands so they may bear sons and daughters and multiply there and may not you diminish.
7 Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
And seek [the] welfare of the city where I have sent into exile you there towards and pray for it to Yahweh for in welfare its it will belong to you welfare.
8 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
For thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel may not they deceive you prophets your who [are] in midst your and diviners your and may not you listen to dreams your which you [are] dreaming.
9 Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
For with falsehood they [are] prophesying to you in name my not I sent them [the] utterance of Yahweh.
10 Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
That thus he says Yahweh if to [the] mouth will be completed for Babylon seventy year[s] I will give attention to you and I will carry out on you word my good by bringing back you to the place this.
11 Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
For I I know the plans which I [am] planning on you [the] utterance of Yahweh plans of well-being and not for harm to give to you a future and a hope.
12 Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
And you will call on me and you will come and you will pray to me and I will listen to you.
13 Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
And you will seek me and you will find [me] if you will seek me with all heart your.
14 mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
And I will let myself be found by you [the] utterance of Yahweh and I will turn back (captivity your *Q(k)*) and I will gather you from all the nations and from all the places where I banished you there [the] utterance of Yahweh and I will bring back you to the place where I sent into exile you from there.
15 Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
For you have said he has raised up for us Yahweh prophets Babylon.
16 koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
For thus - he says Yahweh concerning the king who sits to [the] throne of David and concerning all the people which dwells in the city this countrymen your who not they went out with you in the exile.
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
Thus he says Yahweh of hosts here I [am] about to send on them the sword famine and pestilence and I will make them like figs rotten which not they will be eaten from badness.
18 Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
And I will pursue after them with the sword with famine and with pestilence and I will make them (into a terror *Q(K)*) to all - [the] kingdoms of the earth into a curse and into a waste and into a hissing and into a reproach among all the nations where I have banished them there.
19 Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
Because that not they listened to words my [the] utterance of Yahweh [those] whom I sent to them servants my the prophets rising early and sending and not you listened [the] utterance of Yahweh.
20 Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
And you hear [the] word of Yahweh O all the exile[s] whom I sent from Jerusalem Babylon towards.
21 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel concerning Ahab [the] son of Kolaiah and to Zedekiah [the] son of Maaseiah who are prophesying to you in name my falsehood here I - [am] about to give them in [the] hand of Nebuchadnezzar [the] king of Babylon and he will strike down them to eyes your.
22 Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
And it will be taken from them a curse by all [the] exile[s] of Judah who [are] in Babylon saying may he make you Yahweh like Zedekiah and like Ahab whom he roasted them [the] king of Babylon in the fire.
23 Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
Because that they did folly in Israel and they committed adultery [the] wives of neighbors their and they spoke a word in name my falsehood which not I commanded them and I ([am he] who knows *Q(K)*) and a witness [the] utterance of Yahweh.
24 Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
And to Shemaiah the Nehelamite you will say saying.
25 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
Thus he says Yahweh of hosts [the] God of Israel saying because that you you sent in own name your letters to all the people which [is] in Jerusalem and to Zephaniah [the] son of Maaseiah the priest and to all the priests saying.
26 ‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
Yahweh he has made you priest in place of Jehoiada the priest to be overseers [the] house of Yahweh to every person [who] is mad and [who] prophesies and you will put him into the stock[s] and into the iron collar.
27 Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
And therefore why? not have you rebuked Jeremiah the Anathothite who is prophesying to you.
28 Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
For since he has sent to us Babylon saying [will be] a long [time] it build houses and dwell and plant gardens and eat produce their.
29 Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
And he read aloud Zephaniah the priest the letter this in [the] ears of Jeremiah the prophet.
30 Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
And it came [the] word of Yahweh to Jeremiah saying.
31 “Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
Send to all the exile[s] saying thus he says Yahweh concerning Shemaiah the Nehelamite because that he has prophesied to you Shemaiah and I not I sent him and he has made rely you on falsehood.
32 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.
Therefore thus he says Yahweh here I [am] about to visit [judgment] on Shemaiah the Nehelamite and on offspring his not he will belong to him anyone - dwelling - in among the people this and not he will look on the good which I [will be] doing for people my [the] utterance of Yahweh for rebellion he has spoken on Yahweh.

< Yeremiya 29 >