< Yeremiya 29 >

1 Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Og disse ere Ordene i det Brev, som Profeten Jeremias sendte fra Jerusalem til de øvrige af de Ældste, som vare bortførte, og til Præsterne og til Profeterne og til alt Folket, som Nebukadnezar havde bortført fra Jerusalem til Babel,
2 Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
— efter at Kong Jekonias og Herskerinden og Hofmændene, Judas og Jerusalems Fyrster, og Tømmermændene og Smedene vare gangne ud af Jerusalem, —
3 Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
ved Eleasas, Safans Søns, og Gemarias, Hilkias Søns, Haand, hvilke Zedekias, Judas Konge, sendte til Babel til Nebukadnezar, Kongen i Babel; det lød saaledes:
4 Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
Saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud, til alle de bortførte, som jeg har ladet bortføre fra Jerusalem til Babel:
5 “Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
Bygger Huse og bosætter eder, og planter Haver og æder deres Frugt!
6 Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
Tager Hustruer og avler Sønner og Døtre, og tager Hustruer til eders Sønner og giver eders Døtre Mænd, at de maa føde Sønner og Døtre; og formerer eder der, og mindsker eder ikke!
7 Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
Og søger den Stads Bedste, til hvilken jeg bortførte eder, og beder for den til Herren, thi naar den har Fred, saa have og I Fred.
8 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
Thi saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud: Lader ikke eders Profeter, som ere midt iblandt eder, og eders Spaamænd bedrage eder, og hører ikke paa eders Drømme, som I komme til at drømme.
9 Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
Thi de spaa Løgn for eder i mit Navn; jeg har ikke sendt dem, siger Herren.
10 Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
Thi saa siger Herren: Naar halvfjerdsindstyve Aar ere forløbne for Babel, da vil jeg besøge eder ogstadfæste over eder mit gode Ord om at føre eder tilbage til dette Sted.
11 Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
Thi jeg kender de Tanker, som jeg tænker angaaende eder, siger Herren, Tanker om Fred og ikke om Ulykke, for at give eder en Fremtid og et Haab.
12 Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
Og I skulle paakalde mig og gaa hen og bede til mig, og jeg vil høre eder.
13 Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
Og I skulle søge og finde mig; thi I ville søge mig af eders ganske Hjerte.
14 mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
Og jeg skal lade mig finde af eder, siger Herren, og omvende eders Fangenskab og samle eder fra alle de Hedninger og fra alle de Steder, hvorhen jeg fordrev eder, siger Herren; og jeg skal lade eder komme tilbage til det Sted, hvorfra jeg bortførte eder.
15 Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
Thi I have sagt: Herren har opvakt os Profeter i Babel;
16 koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
men Herren har sagt saaledes om Kongen, som sidder paa Davids Trone, og om alt Folket, som bor i denne Stad, om eders Brødre, som ikke ere gangne ud med eder iblandt de bortførte,
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
ja, saaledes har den Herre Zebaoth sagt: Se, jeg sender Sværdet, Hungeren og Pesten over dem, og jeg vil gøre dem som de modbydelige Figener, der ikke kunde ædes, fordi de vare saa slette.
18 Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
Og jeg vil forfølge dem med Sværdet, med Hungeren og med Pesten og gøre dem til en Gru for alle Riger paa Jorden, til Forbandelse og til Forfærdelse og til Spot og til Forhaanelse iblandt alle Hedningerne, hvorhen jeg har fordrevet dem;
19 Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
fordi de ikke hørte paa mine Ord, siger Herren, jeg, som sendte mine Tjenere, Profeterne, til dem tidligt og ideligt, uden at de hørte mig, siger Herren.
20 Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
Men I, hører Herrens Ord, alle I bortførte, hvilke jeg sendte fra Jerusalem til Babel!
21 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
Saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud, om Akab, Kolajas Søn, og om Zedekias, Maasejas Søn, som spaa eder Løgn i mit Navn: Se, jeg giver dem i Nebukadnezar, Kongen af Babels Haand, og han skal dræbe dem for eders Øjne.
22 Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
Og der skal fra dem optages en Forbandelse iblandt alle de bortførte af Juda, som ere i Babel, idet man skal sige: Herren gøre dig som Zedekias og som Akab! hvilke Kongen af Babel stegte ved Ild,
23 Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
fordi de gjorde en Daarskab i Israel og bedreve Hor med deres Næstes Hustruer og i mit Navn talte løgnagtige Ord, hvilke jeg ikke havde befalet dem; jeg ved det og vidner det, siger Herren.
24 Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
Og om Semaja, Nekelamiten, skal du sige saaledes:
25 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
Saa siger den Herre Zebaoth, Israels Gud: Fordi du sendte Breve i dit Navn til alt Folket, som er i Jerusalem, og til Præsten Zefanja, Maasejas Søn, og til alle Præsterne saa lydende:
26 ‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
Herren har sat dig til Præst i Præsten Jojadas Sted, for at der maa være Opsynsmænd i Herrens Hus over hver Mand, som raser, og som spaar, at du kan lægge dem i Blok og Baand:
27 Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
Hvorfor har du da nu ikke truet Jeremias fra Anathoth, som spaar for eder?
28 Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
thi derfor har han sendt Bud til os til Babel og sagt: Det vil vare længe; bygger Huse og bosætter eder, og planter Haver og æder deres Frugt — —
29 Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
Og Præsten Zefanja læste dette Brev for Profeten Jeremias's Øren.
30 Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Og Herrens Ord kom til Jeremias saalunde:
31 “Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
Send Bud til alle de bortførte, og sig: Saa siger Herren om Nekelamiten Semaja: Fordi Semaja har spaaet for eder, skønt jeg ikke har sendt ham, og han har bragt eder til at forlade eder paa Løgn:
32 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.
Derfor, saa siger Herren: Se, jeg vil hjemsøge Nekelamiten Semaja og hans Afkom; han skal ikke have nogen, som skal bo midt iblandt dette Folk, og han skal ikke se det gode, som jeg vil gøre imod mit Folk, siger Herren; thi han har prædiket Frafald fra Herren.

< Yeremiya 29 >