< Yeremiya 29 >

1 Yeremiya anatumiza kalata kuchokera ku Yerusalemu kupita kwa akuluakulu amene anali ku ukapolo, ndiponso kwa ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse amene Nebukadinezara anawatenga ku Yerusalemu kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
Tato jsou slova listu, kterýž poslal Jeremiáš prorok z Jeruzaléma k ostatku starších zajatých a k kněžím i k prorokům i ke všemu lidu, kterýž přestěhoval Nabuchodonozor z Jeruzaléma do Babylona,
2 Zimenezi zinachitika mfumu Yekoniya, amayi a mfumu, nduna za mfumu ndiponso atsogoleri a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, anthu aluso ndi amisiri atatengedwa ku Yerusalemu kupita ku ukapolo.
Když vyšel Jekoniáš král a královna, i komorníci, knížata Judská i Jeruzalémská, tolikéž tesaři i kováři z Jeruzaléma,
3 Yeremiya anapatsira kalatayo Eleasa mwana wa Safani ndi Gemariya mwana wa Hilikiya, amene Zedekiya mfumu ya Yuda anawatumiza kwa Mfumu Nebukadinezara ku Babuloni. Mʼkalatamo analembamo kuti:
Po Elasovi synu Safanovu, a Gemariášovi synu Helkiášovu, (kteréž byl poslal Sedechiáš král Judský k králi Babylonskému do Babylona), řka:
4 Anthu onse amene anatengedwa ukapolo kuchokera ku Yerusalemu kupita ku Babuloni, Yehova akuwawuza kuti,
Takto praví Hospodin zástupů, Bůh Izraelský, všechněm zajatým, kteréž jsem přestěhoval z Jeruzaléma do Babylona:
5 “Mangani nyumba ndipo muzikhalamo. Limani minda ndipo mudye zipatso zake.
Stavějte domy, a osazujte se, štěpujte také štěpnice, a jezte ovoce jejich.
6 Kwatirani ndipo mubereke ana aamuna ndi aakazi. Ana anu aamuna muwasankhire akazi ndipo muwasankhire amuna ana anu aakaziwo, kuti nawonso abale ana aamuna ndi aakazi. Muchulukane kumeneko. Chiwerengero chanu chisachepe.
Pojímejte ženy, a ploďte syny i dcery, dávejte také synům svým ženy, dcery též své dávejte za muže, ať rodí syny a dcery; množte se tam, a nebeřte umenšení.
7 Ndiponso muzifunafuna mtendere ndi ubwino wa mzinda umene ndinakupirikitsirani ku ukapoloko. Muzipempherera mzindawo kwa Yehova, kuti zikuyendereni bwino.”
A hledejte pokoje města toho, do kteréhož jsem zastěhoval vás, a modlívejte se za ně Hospodinu; nebo v pokoji jeho budete míti pokoj.
8 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akunena kuti, “Musalole kuti aneneri ndi owombeza amene ali pakati panu akunyengeni. Musamvere maloto awo.
Takto zajisté praví Hospodin zástupů, Bůh Izraelský: Nechť vás nesvodí proroci vaši, kteříž jsou mezi vámi, ani hadači vaši, a nespravujte se sny svými, jichž vy příčinou jste, aby je mívali.
9 Iwo akunenera zabodza kwa inu mʼdzina langa ngakhale Ine sindinawatume,” akutero Yehova.
Nebo vám oni lživě prorokují ve jménu mém; neposlalť jsem jich, dí Hospodin.
10 Yehova akuti, “Zaka 70 za ku Babuloni zikadzatha, ndidzabwera kudzakuchitirani zabwino zonse zimene ndinakulonjezani zija, ndipo ndidzakubwezerani ku malo ano.
Takto zajisté praví Hospodin: Že jakž se jen vyplní Babylonu sedmdesáte let, navštívím vás, a potvrdím vám slova svého výborného o navrácení vás na místo toto.
11 Pakuti Ine ndikudziwa zimene ndinakukonzerani,” akutero Yehova, “ndimalingalira zabwino zokhazokha za inu osati zoyipa, ayi. Ndimalingalira zinthu zokupatsani chiyembekezo chenicheni pa za mʼtsogolo.
Nebo já nejlépe znám myšlení, kteráž myslím o vás, dí Hospodin, myšlení o pokoji, a ne o trápení, abych učinil vašemu očekávání konec přežádostivý.
12 Nthawi imeneyo mudzandiyitana, ndi kunditama mopemba ndipo ndidzakumverani.
Když mne vzývati budete, a půjdete, a modliti se mně budete, tedy vyslyším vás.
13 Mudzandifunafuna ndipo mudzandipeza. Mukadzandifuna ndi mtima wanu wonse
A hledajíce mne, naleznete, když mne hledati budete celým srdcem svým.
14 mudzandipezadi,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubwezerani zabwino zanu. Ndidzakusonkhanitsani kuchokera ku mayiko onse ndi kumalo konse kumene munali,” akutero Yehova, “ndipo ndidzakubweretsani kumalo kumene munali ndisanakuchotseni kukupititsani ku ukapolo.”
Dám se zajisté nalezti vám, dí Hospodin, a přivedu zase zajaté vaše, a shromáždím vás ze všech národů i ze všech míst, kamžkoli jsem zahnal vás, dí Hospodin, a uvedu vás zase na místo toto, odkudž jsem vás zastěhoval,
15 Inu mumati, “Yehova watiwutsira aneneri athu ku Babuloni,”
Když řeknete: Vzbuzovalť nám Hospodin proroky v Babyloně.
16 koma zimene Yehova akunena za mfumu imene ikukhala pa mpando waufumu wa Davide pamodzi ndi anthu onse amene anatsala mu mzinda muno, abale anu amene sanapite nanu ku ukapolo ndi izi,
Nebo takto praví Hospodin o králi sedícím na stolici Davidově, a o všem lidu obývajícím v městě tomto, bratřích vašich, kteříž nevyšli s vámi v tom zajetí,
17 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawapha ndi nkhondo, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa ngati nkhuyu zowola kwambiri, zosati nʼkudya.
Takto dí Hospodin zástupů: Aj, já pošli na ně meč, hlad a mor, a naložím s nimi jako s fíky trpkými, kterýchž nelze jísti pro trpkost.
18 Ndidzawalondola ndi lupanga, njala ndi mliri ndipo ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa anthu amayiko onse a pa dziko lapansi. Adzakhala otembereredwa, ochititsa mantha, onyozeka ndiponso ochitidwa chipongwe pakati pa anthu a mitundu yonse kumene ndawapirikitsirako.
Nebo stihati je budu mečem, hladem i morem, a vydám je ku posmýkání po všech královstvích země, k proklínání, a k užasnutí, anobrž na odivu, a k utrhání mezi všemi národy, tam kdež je vypudím,
19 Zidzatero chifukwa sanamvere mawu anga amene ndinkawatumizira kudzera mwa atumiki anga, aneneri. Ngakhale inu amene muli ku ukapolo simunamverenso,” akutero Yehova.
Proto že neposlouchají slov mých, dí Hospodin, když posílám k nim služebníky své proroky, ráno přivstávaje, a to ustavičně, a neposlouchali jste, dí Hospodin.
20 Choncho, imvani mawu a Yehova, inu akapolo nonse amene ndinakuchotsani mu Yerusalemu ndi kukupititsani ku Babuloni.
Protož slyštež vy slovo Hospodinovo, všickni zajatí, kteréž jsem vyslal z Jeruzaléma do Babylona.
21 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti zokhudza Ahabu mwana wa Kolaya ndi Zedekiya mwana wa Maseya, amene akulosera zabodza kwa inu mʼdzina langa: “Taonani ndidzawapereka kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzawapha inu mukupenya.
Takto praví Hospodin zástupů, Bůh Izraelský, o Achabovi synu Kolaiášovu, a o Sedechiášovi synu Maaseiášovu, kteříž prorokují vám ve jménu mém lež: Aj, já vydám je v ruku Nabuchodonozora krále Babylonského, aby je zbil před očima vašima.
22 Chifukwa cha anthu awiriwo, akapolo onse ochokera ku Yuda amene ali ku Babuloni adzagwiritsa ntchito mawu awa potemberera: ‘Yehova achite nawe monga mmene anachitira ndi Zedekiya ndi Ahabu, amene mfumu ya ku Babuloni inawatentha.’
I bude vzato na nich klnutí mezi všecky zajaté Judské, kteříž jsou v Babyloně, aby říkali: Nechť nakládá Hospodin s tebou, jako s Sedechiášem a jako s Echabem, kteréž upekl král Babylonský na ohni,
23 Pakuti anthu amenewa achita zoyipa kwambiri mu Israeli; achita chigololo ndi akazi a eni ake ndipo mʼdzina langa ankayankhula zabodza zimene sindinawawuze kuti atero. Ine ndikuzidziwa ndipo ndine mboni ya zimenezi,” akutero Yehova.
Proto že páchali nešlechetnost v Izraeli, cizoložíce s ženami bližních svých, a mluvíce slovo ve jménu mém lživě, čehož jsem nepřikázal jim. Já pak o tom vím, a jsem toho i svědkem, dí Hospodin.
24 Ukamuwuze Semaya wa ku Nehelamu kuti,
Semaiášovi Nechelamitskému mluv, řka:
25 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Iwe unatumiza kalata mʼdzina lako kwa anthu onse a mu Yerusalemu, kwa Zefaniya mwana wa wansembe Maseya, ndi kwa ansembe onse. Unalemba mu kalatayo kuti,
Takto praví Hospodin zástupů, Bůh Izraelský, řka: Proto že jsi poslal jménem svým listy ke všemu lidu, kterýž jest v Jeruzalémě, a Sofoniášovi synu Maaseiášovu knězi i ke všechněm kněžím, řka:
26 ‘Yehova wakusankha kukhala wansembe mʼmalo mwa Yehoyada kuti ukhale wamkulu woyangʼanira Nyumba ya Yehova. Munthu aliyense wamisala amene akudziyesa kuti ndi mneneri uzimuponya mʼndende ndi kumuveka goli lachitsulo.
Hospodin dal tě za kněze na místo Joiady kněze, abyste pozor měli v domě Hospodinově na každého muže pošetilého a vystavujícího se za proroka, a abys dal takového do žaláře a do klady.
27 Nanga tsono chifukwa chiyani simunamuchitire zimenezi Yeremiya wa ku Anatoti, amene amakhala ngati mneneri pakati panu?
Pročež jsi pak nyní neokřikl Jeremiáše Anatotského, kterýž se vám vystavuje za proroka?
28 Yeremiyayo watitumizira uthenga uwu kuno ku Babuloni: Ukapolo wanu ukhala wa nthawi yayitali. Choncho mangani nyumba ndipo muzikhalamo; limani minda ndipo mudye zipatso zake.’”
Nebo posílal k nám do Babylona, řka: Protáhneť se to dlouho, stavějte domy, a osazujte se, štěpujte také štěpnice, a jezte ovoce jejich.
29 Koma wansembe Zefaniya anayiwerenga kalatayo pamaso pa mneneri Yeremiya.
Nebo Sofoniáš kněz četl ten list před Jeremiášem prorokem.
30 Ndipo Yehova anawuza Yeremiya kuti,
I stalo se slovo Hospodinovo k Jeremiášovi, řkoucí:
31 “Tumiza uthenga uwu kwa akapolo onse: ‘Yehova akuti zokhudza Semaya wa ku Nehelamu: Semaya wakuloserani, ngakhale kuti Ine sindinamutume, ndipo wakunyengani kuti muzikhulupirira bodza.
Pošli ke všechněm zajatým, řka: Takto praví Hospodin o Semaiášovi Nechelamitském: Proto že prorokuje vám Semaiáš, ješto jsem já ho neposlal, a přivodí vás k tomu, abyste doufání skládali ve lži,
32 Nʼchifukwa chake Ine Yehova ndikuti: Mʼbanja lakelo sipadzakhala munthu pakati pa mtundu uno wa anthu amene adzaone zinthu zabwino zimene ndidzachitira anthu anga chifukwa analalika zondiwukira,’” akutero Yehova.
Protož takto praví Hospodin: Aj, já trestati budu Semaiáše Nechelamitského i símě jeho. Nebude míti žádného, kdo by bydlil u prostřed lidu tohoto, aniž uzří toho dobrého, kteréž já učiním lidu svému, dí Hospodin; nebo mluvil to, čímž by odvrátil lid od Hospodina.

< Yeremiya 29 >