< Yeremiya 28 >

1 Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti,
Aynı yıl Yahuda Kralı Sidkiya'nın krallığının başlangıcında, dördüncü yılının beşinci ayında Givonlu Azzur oğlu Peygamber Hananya RAB'bin Tapınağı'nda kâhinlerle bütün halkın önünde bana şöyle dedi:
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.
“İsrail'in Tanrısı, Her Şeye Egemen RAB diyor ki, ‘Babil Kralı'nın boyunduruğunu kıracağım.
3 Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni.
Babil Kralı Nebukadnessar'ın buradan alıp Babil'e götürdüğü RAB'bin Tapınağı'na ait bütün eşyaları iki yıl içinde buraya geri getireceğim.
4 Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’”
Yahuda Kralı Yehoyakim oğlu Yehoyakin'le Babil'e sürgüne giden bütün Yahudalılar'ı buraya geri getireceğim’ diyor RAB, ‘Çünkü Babil Kralı'nın boyunduruğunu kıracağım.’”
5 Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova.
Bunun üzerine Peygamber Yeremya, kâhinlerin ve RAB'bin Tapınağı'ndaki halkın önünde Peygamber Hananya'yı yanıtladı.
6 Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni.
Yeremya şöyle dedi: “Amin! RAB aynısını yapsın! RAB, tapınağına ait eşyalarla bütün sürgünleri Babil'den buraya geri getirerek ettiğin peygamberlik sözlerini gerçekleştirsin!
7 Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse:
Yalnız şimdi sana ve halka söyleyeceğim şu sözü dinle:
8 Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu.
Çok önce, benden de senden de önce yaşamış peygamberler birçok ülke ve büyük krallığın başına savaş, felaket, salgın hastalık gelecek diye peygamberlik ettiler.
9 Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”
Ancak esenlik olacağını söyleyen peygamberin sözü yerine gelirse, onun gerçekten RAB'bin gönderdiği peygamber olduğu anlaşılır.”
10 Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola,
Bunun üzerine Peygamber Hananya, Peygamber Yeremya'nın boynundan boyunduruğu çıkarıp kırdı.
11 ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.
Sonra halkın önünde şöyle dedi: “RAB diyor ki, ‘Babil Kralı Nebukadnessar'ın bütün ulusların boynuna taktığı boyunduruğu iki yıl içinde işte böyle kıracağım.’” Böylece Peygamber Yeremya yoluna gitti.
12 Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Peygamber Hananya Peygamber Yeremya'nın boynundaki boyunduruğu kırdıktan sonra RAB Yeremya'ya şöyle seslendi:
13 “Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo.
“Git, Hananya'ya de ki, ‘RAB şöyle diyor: Sen tahtadan yapılmış boyunduruğu kırdın, ama yerine demir boyunduruk yapacaksın!
14 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’”
Çünkü İsrail'in Tanrısı, Her Şeye Egemen RAB diyor ki, Babil Kralı Nebukadnessar'a kulluk etmeleri için bütün bu ulusların boynuna demir boyunduruk geçirdim, ona kulluk edecekler. Yabanıl hayvanları da onun denetimine vereceğim.’”
15 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza.
Peygamber Yeremya Peygamber Hananya'ya, “Dinle, ey Hananya!” dedi, “Seni RAB göndermedi. Ama sen bu ulusu yalana inandırdın.
16 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’”
Bu nedenle RAB diyor ki, ‘Seni yeryüzünden silip atacağım. Bu yıl öleceksin. Çünkü halkı RAB'be karşı kışkırttın.’”
17 Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.
Peygamber Hananya o yılın yedinci ayında öldü.

< Yeremiya 28 >