< Yeremiya 28 >

1 Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti,
Et il arriva, en cette même année, au commencement du règne de Sédécias, roi de Juda, en la quatrième année, au cinquième mois, que Hanania, fils d’Azzur, le prophète, qui était de Gabaon, me parla dans la maison de l’Éternel, aux yeux des sacrificateurs et de tout le peuple, disant:
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.
Ainsi a parlé l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël, disant: J’ai brisé le joug du roi de Babylone.
3 Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni.
Encore deux années, et je ferai revenir en ce lieu tous les ustensiles de la maison de l’Éternel que Nebucadnetsar, roi de Babylone, a pris de ce lieu et a transportés à Babylone;
4 Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’”
et Jéconias, fils de Jehoïakim, roi de Juda, et tous les transportés de Juda qui sont allés à Babylone, je les ramènerai dans ce lieu, dit l’Éternel; car je briserai le joug du roi de Babylone.
5 Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova.
Et Jérémie le prophète parla à Hanania, le prophète, aux yeux des sacrificateurs et aux yeux de tout le peuple, qui se tenaient dans la maison de l’Éternel.
6 Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni.
Et Jérémie le prophète dit: Amen! Qu’ainsi fasse l’Éternel! Que l’Éternel confirme tes paroles, que tu as prophétisées, pour faire revenir de Babylone en ce lieu les ustensiles de la maison de l’Éternel et tous les captifs!
7 Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse:
Toutefois, écoute, je te prie, cette parole que je prononce à tes oreilles et aux oreilles de tout le peuple:
8 Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu.
Les prophètes qui ont été avant moi et avant toi, d’ancienneté, ont aussi prophétisé, touchant plusieurs pays et touchant de grands royaumes, la guerre, et le malheur, et la peste;
9 Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”
le prophète qui prophétise la paix, quand la parole de ce prophète arrivera, on saura que c’est un prophète que l’Éternel a véritablement envoyé.
10 Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola,
Et Hanania le prophète prit le joug de dessus le cou de Jérémie le prophète, et le brisa.
11 ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.
Et Hanania parla aux yeux de tout le peuple, disant: Ainsi dit l’Éternel: Encore deux années, et je briserai ainsi le joug de Nebucadnetsar, roi de Babylone, de dessus le cou de toutes les nations. Et Jérémie le prophète s’en alla son chemin.
12 Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
Et la parole de l’Éternel vint à Jérémie, après que Hanania le prophète eut brisé le joug de dessus le cou de Jérémie le prophète, disant:
13 “Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo.
Va, et parle à Hanania, disant: Ainsi dit l’Éternel: Tu as brisé les jougs de bois, et tu as fait à leur place des jougs de fer.
14 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’”
Car ainsi dit l’Éternel des armées, le Dieu d’Israël: J’ai mis un joug de fer sur le cou de toutes ces nations, afin qu’elles servent Nebucadnetsar, roi de Babylone; et elles le serviront; et je lui ai aussi donné les bêtes des champs.
15 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza.
Et Jérémie le prophète dit à Hanania le prophète: Écoute, Hanania! L’Éternel ne t’a point envoyé; mais tu as fait que ce peuple s’est confié au mensonge.
16 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’”
C’est pourquoi, ainsi dit l’Éternel: Voici, je te renvoie de dessus la face de la terre; tu mourras cette année, car tu as parlé de révolte contre l’Éternel.
17 Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.
Et Hanania le prophète mourut cette année-là, au septième mois.

< Yeremiya 28 >