< Yeremiya 28 >
1 Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti,
It happened in that year, in the beginning of the reign of Zedekiah king of Judah, in the fourth year and the fifth month, Hananiah son of Azzur the prophet, who was from Gibeon, spoke to me in Yahweh's house in front of the priests and all the people. He said,
2 “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.
“Yahweh of hosts, God of Israel, says this: I have broken the yoke imposed by the king of Babylon.
3 Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni.
Within two years I will bring back to this place all the objects belonging to Yahweh's house that Nebuchadnezzar king of Babylon took from this place and transported to Babylon.
4 Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’”
Then I will bring back to this place Jehoiachin son of Jehoiakim, king of Judah, and all the captives of Judah who were sent to Babylon—this is Yahweh's declaration—for I will break the yoke of the king of Babylon.”
5 Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova.
So Jeremiah the prophet spoke to Hananiah the prophet in front of the priests and to all the people who stood in Yahweh's house.
6 Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni.
Jeremiah the prophet said, “May Yahweh do this! May Yahweh confirm the words that you prophesied and bring back to this place the objects belonging to Yahweh's house, and all the captives from Babylon.
7 Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse:
However, listen to the word that I am proclaiming in your hearing and in the hearing of all the people.
8 Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu.
The prophets who existed before me and you from long ago also prophesied about many nations and against great kingdoms, about war, famine, and plague.
9 Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”
So the prophet who prophesies that there will be peace—if his word comes true, then it will be known that he is indeed a prophet sent out by Yahweh.”
10 Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola,
But Hananiah the prophet took the yoke from the neck of Jeremiah the prophet and broke it.
11 ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.
Then Hananiah spoke in front of all the people and said, “Yahweh says this: Just like this, within two years I will break from off the neck of every nation the yoke imposed by Nebuchadnezzar king of Babylon.” Then Jeremiah the prophet went on his way.
12 Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
After Hananiah the prophet had broken the yoke from the neck of Jeremiah the prophet, the word of Yahweh came to Jeremiah, saying,
13 “Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo.
“Go and speak to Hananiah and say, 'Yahweh says this: You broke a yoke of wood, but I will make instead a yoke of iron.'
14 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’”
For Yahweh of hosts, God of Israel, says this: I have placed a yoke of iron on the neck of all of these nations to serve Nebuchadnezzar king of Babylon, and they will serve him. I have also given him the wild beasts in the fields to rule over.”
15 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza.
Next Jeremiah the prophet said to Hananiah the prophet, “Listen Hananiah! Yahweh has not sent you, but you yourself have caused this people to believe in lies.
16 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’”
So Yahweh says this: Look, I am about to send you out from the earth. You will die this year, since you proclaimed rebellion against Yahweh.”
17 Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.
In the seventh month of that same year, Hananiah the prophet died.