< Yeremiya 27 >

1 Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
У почетку царовања Јоакима сина Јосијиног цара Јудиног дође ова реч Јеремији од Господа говорећи:
2 “Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
Овако ми рече Господ: Начини себи свезе и јарам, и метни себи око врата.
3 Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
По том пошљи их цару едомском и цару моавском и цару синова Амонових и цару тирском и цару сидонском, по посланицима који ће доћи у Јерусалим к Седекији цару Јудином.
4 Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
И наручи им нека кажу својим господарима: Овако вели Господ над војскама Бог Израиљев: овако реците својим господарима:
5 Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
Ја сам створио земљу и људе и стоку, што је по земљи, силом својом великом и мишицом својом подигнутом; и дајем је коме ми је драго.
6 Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
И сада ја дадох све те земље у руке Навуходоносору цару вавилонском слузи свом, дадох му и зверје пољско да му служи.
7 Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
И сви ће народи служити њему и сину његовом и унуку његовом докле дође време и његовој земљи, и велики народи и силни цареви покоре га.
8 “‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
А који народ или царство не би хтео служити Навуходоносору цару вавилонском, и не би хтео савити врата свог у јарам цара вавилонског, такав ћу народ походити мачем и глађу и помором, говори Господ, докле их не истребим руком његовом.
9 Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
Не слушајте дакле пророка својих ни врача својих ни сањача својих ни гатара својих ни бајача својих, који вам говоре и веле: Нећете служити цару вавилонском.
10 Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
Јер вам они лаж пророкују, како бих вас далеко одвео из земље ваше и изагнао вас да изгинете.
11 Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
А народ који би савио врат свој под јарам цара вавилонског и служио му, оставићу га на земљи његовој, говори Господ, да је ради и станује у њој.
12 Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
И Седекији цару Јудином рекох све ово говорећи: Савијте врат свој под јарам цара вавилонског и служите њему и народу његовом, па ћете остати живи.
13 Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
Зашто да погинете ти и народ твој од мача и од глади и од помора, како рече Господ за народ који не би служио цару вавилонском?
14 Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
Не слушајте, дакле, шта говоре пророци који вам кажу и веле: Нећете служити цару вавилонском, јер вам они пророкују лаж.
15 Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
Јер их ја нисам послао, говори Господ, него лажно пророкују у моје име, како бих вас прогнао да изгинете и ви и пророци који вам пророкују.
16 Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
И свештеницима и свему народу говорих и рекох: Овако вели Господ: не слушајте шта говоре ваши пророци који вам пророкују говорећи: Ево, посуђе дома Господњег вратиће се из Вавилона скоро. Јер вам они пророкују лаж.
17 Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
Не слушајте их; служите цару вавилонском, и остаћете живи; зашто тај град да опусти?
18 Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
Ако ли су пророци и ако је реч Господња у њих, нека моле Господа над војскама да судови што су остали у дому Господњем и у дому цара Јудиног и у Јерусалиму не отиду у Вавилон.
19 Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
Јер овако вели Господ над војскама за ступове и за море и за подножја и за друге судове што су остали у том граду,
20 Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
Којих не узе Навуходоносор цар вавилонски кад одведе у ропство Јехонију сина Јоакимовог, цара Јудиног, из Јерусалима у Вавилон, и све главаре Јудине и јерусалимске;
21 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
Јер овако вели Господ над војскама, Бог Израиљев, за судове што осташе у дому Господњем и у дому цара Јудиног у Јерусалиму:
22 ‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”
У Вавилон ће се однети и онде ће бити до дана кад ћу их походити, вели Господ, кад ћу их донети и вратити на ово место.

< Yeremiya 27 >