< Yeremiya 27 >

1 Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
In the bigynnyng of the rewme of Joachym, the sone of Josie, kyng of Juda, this word was maad of the Lord to Jeremye, and seide,
2 “Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
The Lord seith these thingis to me, Make thou to thee boondis and chaynes, and thou schalt putte tho in thi necke;
3 Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
and thou schalt sende tho to the kyng of Edom, and to the kyng of Moab, and to the kyng of the sones of Amon, and to the kyng of Tyre, and to the kyng of Sidon, bi the hond of messangeris that camen to Jerusalem, and to Sedechie, kyng of Juda.
4 Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
And thou schalt comaunde to hem, that thei speke to her lordis, The Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis, Ye schulen seie these thingis to youre lordis,
5 Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
Y made erthe, and man, and beestis that ben on the face of al erthe, in my greet strengthe, and in myn arm holdun forth; and Y yaf it to hym that plesyde bifore myn iyen.
6 Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
And now therfor Y yaf alle these londis in the hond of Nabugodonosor, my seruaunt, the kyng of Babiloyne; ferthermore and Y yaf to hym the beestis of the feeld, that thei serue hym.
7 Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
And alle folkis schulen serue hym, and his sone, and the sone of his sone, til the tyme of his lond and of hym come; and many folkis and grete kyngis schulen serue hym.
8 “‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
Forsothe the folk and rewme that serueth not Nabugodonosor, kyng of Babiloyne, and whoeuer bowith not his necke vndur the yok of the kyng of Babiloyne, Y schal visite on that folk in swerd, and hungur, and pestilence, seith the Lord, til Y waaste hem in his hond.
9 Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
Therfor nyle ye here youre profetis, and false dyuynouris, and dremeris, and dyuyneris bi chiteryng and fleyng of briddis, and witchis, that seien to you, Ye schulen not serue the kyng of Babiloyne;
10 Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
for thei profesien a lessyng to you, that thei make you fer fro youre lond, and caste out you, and ye perische.
11 Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
Certis the folk that makith suget her nol vndur the yok of the kyng of Babiloyne, and serueth hym, Y schal dismytte it in his lond, seith the Lord; and it schal tile that lond, and schal dwelle therynne.
12 Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
And Y spak bi alle these wordis to Sedechie, kyng of Juda, and Y seide, Make ye suget youre neckis vndur the yok of the kyng of Babiloyne, and serue ye hym, and his puple, and ye schulen lyue.
13 Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
Whi schulen ye die, thou and thi puple, bi swerd, and hungur, and pestilence, as the Lord spak to the folk, that nolde serue to the kyng of Babiloyne?
14 Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
Nyle ye here the wordis of profetis seiynge to you, Ye schulen not serue the kyng of Babiloyne; for thei speken leesyng to you, for Y sente not hem, seith the Lord;
15 Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
and thei profesien falsly in my name, that thei caste out you, and that ye perische, bothe ye and the profetis that profesien to you.
16 Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
And Y spak to the preestis, and to this puple, and Y seide, The Lord God seith these thingis, Nyle ye here the wordis of youre profetis, that profesien to you, and seien, Lo! the vessels of the Lord schulen turne ayen now soone fro Babiloyne; for thei profesien a leesyng to you.
17 Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
Therfor nyle ye here hem, but serue ye to the kyng of Babiloyne, that ye lyue; whi is this citee youun in to wildirnesse?
18 Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
And if thei ben profetis, and if the word of God is in hem, renne thei to the Lord of oostis, that the vessels whiche weren left in the hous of the Lord, and in the hous of the kyng of Juda, and in Jerusalem, come not in to Babiloyne.
19 Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
For the Lord of oostis seith these thingis to the pilers, and to the see, that is, a greet waischyng vessel, and to the foundementis, and to the remenauntis of vessels, that weren left in this citee,
20 Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
whiche Nabugodonosor, king of Babiloyne, took not, whanne he translatide Jeconye, the sone of Joachim, king of Juda, fro Jerusalem in to Babiloyne, and alle the principal men of Juda and of Jerusalem.
21 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
For the Lord of oostis, God of Israel, seith these thingis to the vessels that ben left in the hous of the Lord, and in the hous of the king of Juda, and in Jerusalem, Tho schulen be translatid in to Babiloyne,
22 ‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”
and schulen be there `til to the dai of her visitacioun, seith the Lord; and Y schal make tho to be brouyt, and to be restorid in this place.

< Yeremiya 27 >