< Yeremiya 27 >
1 Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti,
U početku kraljevanja Sidkije, sina Jošije, kralja judejskoga, uputi Jahve Jeremiji ovu riječ.
2 “Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako.
Ovako mi reče Jahve: “Načini sebi užad i jaram i stavi ga sebi na vrat.
3 Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda.
Zatim poruči kralju edomskom, kralju moapskom, kralju amonskom, kralju tirskom i kralju sidonskom, po njihovim izaslanicima koji su došli u Jeruzalem kralju judejskom Sidkiji.
4 Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti:
Naredi im da poruče svojim gospodarima: 'Ovako govori Jahve nad Vojskama, Bog Izraelov! Ovako poručite svojim gospodarima:
5 Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna.
Ja sam snagom svojom svesilnom i rukom ispruženom stvorio zemlju, ljude i životinje na zemlji. I ja to dajem kome hoću.
6 Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire.
Sada, dakle, sve te zemlje dajem u ruke Nabukodonozoru, kralju babilonskom, sluzi svojemu; dajem mu i poljsko zvijerje da mu služi.
7 Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.
I svi će narodi služiti njemu i njegovu sinu, i sinu njegova sina, dok i njegovoj zemlji ne kucne čas te i njega ne upokore moćni narodi i veliki kraljevi.
8 “‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu.
Ako koji narod, ili kraljevstvo, ne htjedne služiti Nabukodonozora, kralja babilonskoga, ne hoteć' se upregnuti u jaram kralja babilonskog, taj ću narod kazniti mačem, glađu i kugom - riječ je Jahvina - dok ga sasvim ne zatrem rukom njegovom.
9 Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’
Ne slušajte, dakle, svojih proroka, gatalaca, sanjara, zvjezdara svojih i čarobnjaka koji vam govore: 'Ne, vi nećete služiti kralju babilonskom!'
10 Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu.
Jer vam oni laž prorokuju samo da vas udalje iz vaše zemlje, da vas otjeram pa da propadnete.
11 Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’”
Ali narod koji se upregne u jaram kralja babilonskoga da mu služi ostavit ću na miru u zemlji njegovoj - riječ je Jahvina - da je obrađuje i u njoj živi.'”
12 Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo.
Sve sam to rekao Sidkiji, kralju judejskom, govoreći: “Upregnite se u jaram kralja babilonskoga i pokorite se njemu i narodu njegovu da ostanete živi.
13 Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni?
Zašto da poginete, ti i narod tvoj, od mača, gladi i kuge, kao što se Jahve zaprijetio narodu koji se ne podvrgne kralju babilonskom?
14 Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza.
Ne slušajte, dakle, riječi onih proroka koji vam govore: 'Vi nećete služiti kralju babilonskom.' Oni vam laž prorokuju.
15 Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”
'Jer nisam ih ja poslao da vam prorokuju - riječ je Jahvina - nego vam oni laž prorokuju u moje ime, da vas otjeram iz vaše zemlje, pa da propadnete - vi i proroci koji vam prorokuju.'”
16 Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu.
I svećenicima i svemu ovom narodu rekao sam: “Ovako govori Jahve: 'Ne slušajte riječi svojih proroka koji vam ovako prorokuju: Evo, posuđe Doma Jahvina bit će uskoro vraćeno iz Babilona.' Oni vam laži prorokuju.
17 Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja?
Ne slušajte ih! Pokorite se kralju babilonskom da ostanete živi! Zašto da ovaj grad postane ruševina?
18 Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni.
Ako su oni zaista proroci, te ako je u njima riječ Jahvina, neka mole Jahvu nad Vojskama da i posuđe što još ostade u Domu Jahvinu i u dvoru kraljeva judejskih i u Jeruzalemu ne dospije u Babilon!
19 Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu.
Jer ovako govori Jahve o stupovima, moru, podnožjima i o preostalom posuđu što još ostade u ovome gradu -
20 Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu.
što još Nabukodonozor, kralj babilonski, ne uze sa sobom onda kad odvede u izgnanstvo iz Jeruzalema u Babilon Jekoniju, sina Jojakimova, kralja judejskoga, i sve odličnike judejske i jeruzalemske.
21 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti,
Da, ovako govori Jahve nad Vojskama, Bog Izraelov, o posuđu koje preostade u Domu Jahvinu, u dvoru kralja judejskog, i u Jeruzalemu:
22 ‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’”
'U Babilon će ih odnijeti i ondje će ostati sve do dana kad ja odem po njih - riječ je Jahvina. I ja ću sve to donijeti i postaviti na ovo mjesto!'”