< Yeremiya 26 >

1 Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
На поча́тку царюва́ння Єгоякима, сина Йосіїного, царя Юдиного, було оце слово від Господа, ка́жучи:
2 “Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
„Так говорить Господь: Стань на подві́р'ї Господнього дому, і будеш говорити всім Юдиним містам, що прихо́дять на поклі́н до Господнього дому, усі ті слова, що Я наказав був тобі, щоб до них говорити, — не вбав ані сло́ва.
3 Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
Може почують вони, і ве́рнуться кожен зо своєї злої дороги, й Я пожалую щодо зла, яке ду́маю вчинити їм через злі їхні вчи́нки!
4 Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
І скажеш до них: Так говорить Господь: Якщо ви не бу́дете прислу́хуватися до Мене, щоб ходити за Зако́ном Моїм, якого Я дав вам,
5 ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
щоб прислу́хуватися до слів Моїх рабів пророків, яких Я посилаю до вас рано та пізно, та не слу́хали ви,
6 ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
то вчиню́ з оцим домом, як з Шіло́, а місто це дам на прокля́ття для всіх наро́дів землі“.
7 Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
І чули священики, і пророки, і ввесь наро́д Єремію, що говорив ці слова в Господньому домі.
8 Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
І сталося, як Єремія закінчи́в говорити все, що наказав був Господь сказати до всього наро́ду, то схопи́ли його священики, і пророки, і ввесь наро́д, говорячи: „Ти конче помреш!
9 Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
На́що пророкував ти Господнім Ім'я́м, кажучи: Як Шіло́, буде дім цей, а місто це буде зруйно́ване, так що не буде в ньому ме́шканця?“І зібрався ввесь народ проти Єремії в Господньому домі.
10 Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
І почули ці слова Юдині князі, і відійшли з царсько́го дому до дому Господнього, і сіли при вході до ново́ї Господньої брами.
11 Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
І сказали священики та пророки до князі́в та до всього народу, говорячи: „Присуд смерти цьому́ чоловікові, бо він пророкував проти цього міста, як ви чули своїми ву́хами!“
12 Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
І сказав Єремія до всіх князі́в і до всього наро́ду, говорячи: „Господь послав мене пророкувати проти цього дому, і проти цього міста всі ті слова́, що ви чули.
13 Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
А тепер поліпші́ть ваші доро́ги та ваші чи́ни, і слухайтеся голосу Господа, вашого Бога, то пожалує Господь щодо зла, яке говорив був на вас.
14 Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
А я — ось я в вашій руці: робіть мені як добре, і як правдиве в ваших оча́х!
15 Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
Тільки справді пізна́єте ви, якщо ви вб'єте мене, що ви невинну кров спрова́дите на себе й на це місто та на ме́шканців його, бо Господь справді послав мене до вас говорити в ваші ву́ха всі ці слова́.“
16 Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
І сказали князі та ввесь наро́д до священиків та до пророків: „Цей чоловік не підлягає присуду смерти, бо він говорив до нас Ім'я́м Господа, нашого Бога!“
17 Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
І встали люди зо старши́х кра́ю, і сказали до всього збору наро́ду, гово́рячи:
18 “Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
„Міхей з Мораші пророкував за днів Єзекії, царя Юдиного, і сказав до всьо́го юдейського наро́ду, говорячи: Так говорить Господь Саваот: Сіон, як те поле, зао́раний буде, а Єрусалим за румо́вища стане, а гора цього храму — підгі́рками лісу.
19 Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
Чи справді забив його Єзекія, цар Юдин, та ввесь Юда? Чи ж він не побоявся Господа, і не зла́годив Господнього лиця? І Господь пожалував щодо того зла, яке говорив був на них. А ми вчинимо таке велике зло на свої душі?
20 (Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
І також пророкував був Господнім Ім'я́м один чоловік, Урі́йя, син Шемаї, з Кір'ят-Єаріму, і пророкував проти цього міста та проти цього кра́ю всі ті слова́, як Єремія.
21 Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
І почув був слова́ його цар Єгояким, і всі ли́царі його та всі князі́; і шукав цар способу забити його. І почув це Урійя, і злякався, й утік, і прийшов до Єгипту.
22 Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
I послав цар Єгояким людей до Єгипту, — Елнатана, Ахборового сина, і людей з ним до Єгипту.
23 Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
І вони ви́вели Урійю з Єгипту, і привели́ його до царя Єгоякима, а той ударив його мечем, а трупа його кинув до гробі́в про́стих людей“.
24 Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.
Але рука Ахикама, Шаханового сина, була з Єремією, щоб не дати його в руку наро́ду забити його.

< Yeremiya 26 >