< Yeremiya 26 >

1 Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Na začetku kraljevanja Jojakíma, Jošíjevega sina, Judovega kralja, je prišla ta beseda od Gospoda, rekoč:
2 “Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
»Tako govori Gospod: ›Stoj na dvoru Gospodove hiše in govori vsem Judovim mestom, ki pridejo oboževat v Gospodovo hišo, vse besede, ki sem ti jih zapovedal, da jim jih govoriš; ne zmanjšaj niti besede.
3 Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
Če bo tako, bodo prisluhnili in se obrnili, vsak človek iz svoje zle poti, da se lahko pokesam od zla, ki sem jim ga namenil storiti zaradi zla njihovih početij.
4 Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
Rekel jim boš: ›Tako govori Gospod: ›Če mi ne boste prisluhnili, da se ravnate po moji postavi, ki sem jo postavil pred vas,
5 ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
da prisluhnete besedam mojih služabnikov prerokov, ki sem jih pošiljal k vam; zgodaj sem jih vzdigoval in jih pošiljal, toda niste prisluhnili;
6 ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
potem bom to hišo naredil podobno Šilu in to mesto naredil prekletstvo vsem narodom zemlje.‹«
7 Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
Tako so duhovniki, preroki in vse ljudstvo slišali Jeremija govoriti te besede v Gospodovi hiši.
8 Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
Pripetilo se je torej, ko je Jeremija končal govorjenje vsega, kar mu je Gospod zapovedal, da govori vsemu ljudstvu, da so ga duhovniki in preroki in vse ljudstvo zgrabili, rekoč: »Zagotovo boš umrl.
9 Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
Zakaj si prerokoval v Gospodovem imenu, rekoč: ›Ta hiša bo podobna Šilu in to mesto bo zapuščeno, brez prebivalca?‹« In vse ljudstvo je bilo zbrano zoper Jeremija v Gospodovi hiši.
10 Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
Ko so Judovi princi slišali te stvari, potem so prišli gor iz kraljeve hiše h Gospodovi hiši in se usedli pri vhodu novih velikih vrat Gospodove hiše.
11 Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
Potem so duhovniki in preroki spregovorili princem in vsemu ljudstvu, rekoč: »Ta mož je vreden, da umre, kajti prerokoval je zoper to mesto, kakor ste slišali s svojimi ušesi.«
12 Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
Potem je Jeremija spregovoril vsem princem in vsemu ljudstvu, rekoč: » Gospod me je poslal, da prerokujem zoper to hišo in zoper to mesto vse besede, ki ste jih slišali.
13 Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
Zato sedaj poboljšajte svoje poti in svoja dejanja in ubogajte glas Gospoda, svojega Boga, in Gospod se bo pokesal od zla, ki ga je proglasil zoper vas.
14 Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
Poglejte, kar se mene tiče, jaz sem v vaši roki. Z menoj storite kakor se vam zdi dobro in primerno.
15 Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
Toda zagotovo vedite, da če me boste usmrtili, boste zagotovo privedli nedolžno kri nadse, nad to mesto in nad njegove prebivalce, kajti resnično me je k vam poslal Gospod, da v vaša ušesa govorim vse te besede.«
16 Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
Potem so princi in vse ljudstvo rekli duhovnikom in prerokom: »Ta mož ni vreden, da umre, kajti govoril nam je v imenu Gospoda, našega Boga.«
17 Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
Potem so vstali nekateri izmed starešin dežele in spregovorili vsemu zboru ljudstva, rekoč:
18 “Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
»Mihej Moréšečan je prerokoval v dneh Ezekíja, Judovega kralja in govoril vsemu Judovemu ljudstvu, rekoč: ›Tako govori Gospod nad bojevniki: ›Sion bo preoran kakor polje in Jeruzalem bo spremenjen v razvaline in gora hiše kakor visoki kraji gozda.
19 Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
Ali ga je Judov kralj Ezekíja in ves Juda sploh dal usmrtiti? Mar se ni bal Gospoda in rotil Gospoda in se je Gospod pokesal zla, ki ga je proglasil zoper njih? Tako bi lahko prihranili veliko zlo zoper naše duše.
20 (Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
Tam pa je bil tudi človek, ki je prerokoval v Gospodovem imenu, Urijá, sin Šemajája iz Kirját Jearíma, ki je prerokoval zoper to mesto in zoper to deželo, glede na vse Jeremijeve besede.
21 Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
Ko je kralj Jojakím, z vsemi svojimi mogočnimi možmi in vsemi princi, slišal njegove besede, je kralj iskal, da ga usmrti. Toda ko je Urijá to slišal, je bil prestrašen in pobegnil ter odšel v Egipt.
22 Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
Kralj Jojakím pa je poslal može v Egipt, in sicer Ahbórjevega sina Elnatána in nekatere može z njim v Egipt.
23 Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
Ti so Urijá spravili iz Egipta in ga privedli h kralju Jojakímu, ki ga je usmrtil z mečem in njegovo truplo vrgel v grobove preprostega ljudstva.
24 Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.
Kljub temu je bila roka Šafánovega sina Ahikáma z Jeremijem, da ga ne bi predali v roko ljudstva, da ga usmrti.

< Yeremiya 26 >