< Yeremiya 26 >
1 Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Au commencement du règne de Joakim, fils de Josias, roi de Juda, cette parole du Seigneur me fut adressée, disant:
2 “Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
Voici ce que dit le Seigneur: Tiens-toi dans le parvis de la maison du Seigneur, et tu diras à toutes les cités de Juda d’où l’on vient afin d’adorer dans la maison du Seigneur, tous les discours que moi je t’ai commandé de leur adresser; ne retranche pas une parole,
3 Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
Pour voir si par hasard ils écouteront, et s’ils se convertiront, chacun de sa voie mauvaise, et je me repentirai du mal que je pense leur faire, à cause de la malice de leurs œuvres.
4 Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
Et tu leur diras: Voici ce que dit le Seigneur: Si vous ne m’écoutez pas, quand j’ordonne que vous marchiez dans ma loi que je vous ai donnée,
5 ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
Et que vous entendiez les paroles de mes serviteurs les prophètes, que moi j’ai envoyés vers vous, me levant durant la nuit et les dirigeant, et que vous n’avez pas écoutés,
6 ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
Je rendrai cette maison comme Silo, et je livrerai cette ville en malédiction à toutes les nations de la terre.
7 Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
Et les prêtres et les prophètes et tout le peuple entendirent Jérémie disant ces paroles dans la maison du Seigneur.
8 Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
Et lorsque Jérémie eut achevé de dire tout ce que le Seigneur lui avait ordonné de dire à tout le peuple, les prêtres et les prophètes et tout le peuple le saisirent, disant: Qu’il meure de mort.
9 Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
Pourquoi a-t-il prophétisé au nom du Seigneur, disant: Comme Silo, ainsi sera cette maison; et cette ville sera désolée, pour qu’il n’y ait pas d’habitant? Et tout le peuple s’assembla contre Jérémie dans la maison du Seigneur.
10 Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
Et les princes de Juda entendirent ces paroles; et ils montèrent de la maison du roi dans la maison du Seigneur, et ils s’assirent à l’entrée de la porte neuve de la maison du Seigneur.
11 Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
Et les prêtres et les prophètes parièrent aux princes et à tout le peuple, disant: Un jugement de mort est dû à cet homme, parce qu’il a prophétisé contre cette cité, comme vous l’avez entendu de vos oreilles.
12 Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
Et Jérémie parla à tous les princes et à tout le peuple, disant: Le Seigneur m’a envoyé, afin de prophétiser à cette maison et à cette cité toutes les choses que vous avez entendues.
13 Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
Maintenant donc rendez droites vos voies et vos œuvres, et écoutez la voix du Seigneur votre Dieu; et le Seigneur se repentira du mal qu’il a annoncé contre vous.
14 Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
Pour moi, voici que je suis entre vos mains; faites-moi ce qui paraît bon et juste à vos yeux;
15 Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
Mais cependant, sachez et apprenez bien que, si vous me faites mourir, vous répandrez un sang innocent contre vous et contre cette cité et ses habitants; car, en vérité, le Seigneur m’a envoyé vers vous, pour que je fisse entendre à vos oreilles toutes ces choses.
16 Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
Et les princes et tout le peuple dirent aux prêtres et aux prophètes: Un jugement de mort n’est pas dû à cet homme, parce que c’est au nom du Seigneur, notre Dieu, qu’il nous a parlé.
17 Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
Des hommes donc, d’entre les anciens du pays, se levèrent, et ils dirent à toute l’assemblée du peuple, en prenant la parole:
18 “Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
Michée de Morasthie fut prophète dans les jours d’Ezéchias, roi de Juda, et parla à tout le peuple de Juda, disant: Voici ce que dit le Seigneur des armées: Sion, comme un champ, sera labourée, et Jérusalem sera réduite en un monceau de pierres, et la montagne de la maison en une haute forêt.
19 Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
Est-ce qu’Ezéchias, roi de Juda, et tout Juda l’ont condamné à mort? Est-ce qu’ils ne craignirent pas le Seigneur, et ne supplièrent-ils pas la face du Seigneur, et le Seigneur ne se repentit-il pas des maux qu’il avait annoncés contre eux? C’est pourquoi nous faisons un grand mal contre nos âmes.
20 (Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
Il y eut aussi un homme prophétisant au nom du Seigneur, Urie, fils de Séméi, de Cariathiarim; et il prophétisa contre cette cité, et contre cette terre, selon toutes les paroles de Jérémie.
21 Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
Et le roi Joakim, et tous les puissants et ses princes entendirent ces paroles; et le roi chercha à le tuer. Et Urie l’apprit, et il craignit, et s’enfuit, et il entra en Egypte.
22 Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
Et le roi Joakim envoya des hommes en Egypte, Elnathan, fils d’Achabor, et des hommes avec lui en Egypte.
23 Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
Et ils tirèrent Urie d’Egypte, et ils l’amenèrent au roi Joakim, et il le frappa du glaive, et il jeta son cadavre dans les sépulcres des derniers du peuple.
24 Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.
Donc la main d’Ahicam, fils de Saphan, fut avec Jérémie, afin qu’il ne fût pas livré aux mains du peuple, et qu’on ne le tuât pas.