< Yeremiya 26 >
1 Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti,
Au commencement du règne de Jehoïakim, fils de Josias, roi de Juda, cette parole vint de par l’Éternel, disant:
2 “Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe.
Ainsi dit l’Éternel: Tiens-toi dans le parvis de la maison de l’Éternel, et dis à toutes les villes de Juda, qui viennent pour se prosterner dans la maison de l’Éternel, toutes les paroles que je t’ai commandé de leur dire; n’en retranche pas une parole.
3 Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa.
Peut-être qu’ils écouteront, et qu’ils reviendront chacun de sa mauvaise voie; et je me repentirai du mal que je pense à leur faire à cause de l’iniquité de leurs actions.
4 Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani,
Et tu leur diras: Ainsi dit l’Éternel: Si vous ne m’écoutez pas, pour marcher dans ma loi que j’ai mise devant vous,
5 ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere,
pour écouter les paroles de mes serviteurs, les prophètes que je vous envoie, me levant de bonne heure et [les] envoyant, – mais vous ne les avez pas écoutés –
6 ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’”
je rendrai cette maison comme Silo, et je livrerai cette ville pour être une malédiction à toutes les nations de la terre.
7 Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova.
Et les sacrificateurs et les prophètes et tout le peuple entendirent Jérémie dire ces paroles dans la maison de l’Éternel.
8 Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa!
Et il arriva que, comme Jérémie achevait de dire tout ce que l’Éternel avait commandé de dire à tout le peuple, les sacrificateurs et les prophètes et tout le peuple le saisirent, disant: Tu mourras certainement!
9 Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.
Pourquoi prophétises-tu au nom de l’Éternel, disant: Cette maison sera comme Silo, et cette ville sera désolée, de sorte qu’il n’y aura pas d’habitant? Et tout le peuple s’assembla contre Jérémie dans la maison de l’Éternel.
10 Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova.
Et les princes de Juda entendirent ces choses, et ils montèrent de la maison du roi à la maison de l’Éternel, et s’assirent dans l’entrée de la porte neuve de l’Éternel.
11 Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”
Et les sacrificateurs et les prophètes parlèrent aux princes et à tout le peuple, disant: Cet homme mérite la mort; car il a prophétisé contre cette ville, comme vous avez entendu de vos oreilles.
12 Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno.
Et Jérémie parla à tous les princes et à tout le peuple, disant: L’Éternel m’a envoyé pour prophétiser contre cette maison et contre cette ville toutes les paroles que vous avez entendues.
13 Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni.
Et maintenant, amendez vos voies et vos actions, et écoutez la voix de l’Éternel, votre Dieu, et l’Éternel se repentira du mal qu’il a prononcé contre vous.
14 Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera.
Pour moi, me voici entre vos mains; faites-moi comme il est bon et droit à vos yeux.
15 Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”
Seulement, sachez bien que, si vous me faites mourir, vous mettrez du sang innocent sur vous, et sur cette ville, et sur ses habitants; car en vérité l’Éternel m’a envoyé vers vous pour prononcer à vos oreilles toutes ces paroles.
16 Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”
Et les princes et tout le peuple dirent aux sacrificateurs et aux prophètes: Cet homme ne mérite pas la mort; car il nous a parlé au nom de l’Éternel, notre Dieu.
17 Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti,
Et quelques hommes des anciens du pays se levèrent, et parlèrent à toute la congrégation du peuple, disant:
18 “Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti, “‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda, Yerusalemu adzasanduka bwinja, ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’
Michée, le Morashtite, prophétisait dans les jours d’Ézéchias, roi de Juda, et a parlé à tout le peuple de Juda, disant: Ainsi dit l’Éternel des armées: Sion sera labourée comme un champ, et Jérusalem sera des monceaux de pierres, et la montagne de la maison, les lieux hauts d’une forêt.
19 Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”
Ézéchias, le roi de Juda, avec tout Juda, le fit-il donc mourir? Ne craignit-il pas l’Éternel, et n’implora-t-il pas l’Éternel, de sorte que l’Éternel se repentit du mal qu’il avait prononcé contre eux? Et nous ferions un grand mal contre nos âmes. –
20 (Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya.
Il y avait aussi un homme qui prophétisait au nom de l’Éternel, Urie, fils de Shemahia, de Kiriath-Jéarim; et il prophétisait contre cette ville et contre ce pays, selon toutes les paroles de Jérémie;
21 Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto.
et le roi Jehoïakim, et tous ses hommes forts et tous les princes, entendirent ses paroles, et le roi chercha à le faire mourir; mais Urie l’apprit, et eut peur, et s’enfuit, et alla en Égypte.
22 Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto.
Et le roi Jehoïakim envoya des hommes en Égypte, Elnathan, fils d’Acbor, et des hommes avec lui, en Égypte;
23 Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).
et ils firent sortir d’Égypte Urie, et l’amenèrent au roi Jehoïakim, et il le frappa avec l’épée, et jeta son cadavre dans les sépulcres des fils du peuple. –
24 Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.
Toutefois la main d’Akhikam, fils de Shaphan, fut avec Jérémie, afin qu’on ne le livre point aux mains du peuple pour le faire mourir.