< Yeremiya 25 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
KA olelo i hiki mai io Ieremia la no na kanaka a pau o ka Iuda, i ka makahiki aha o lehoiakima, ke keiki a losia, ke alii o ka Iuda, oia hoi ka makahiki akahi o Nebukaneza, ke alii o Babulona:
2 Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
Ka mea a Ieremia, ke kaula i olelo ai i na kanaka a pau o ka Iuda, a i ka poe a pau e noho ana ma Ierusalema, i mai la,
3 Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
Mai ka makahiki umikumamakolu o Iosia, ke keiki a Amona, ke alii o ka Iuda a hiki loa mai i keia la, eia hoi ka makahiki iwakaluakumamakolu, ua hiki mai no ka olelo a Iehova ia'u, a ua olelo aku no wau ia oukou, e ala ana i ka wanaao e olelo aku; aka, aole oukou i hoolohe mai.
4 Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
A ua hoouna mai o Iehova io oukou nei i kana mau kauwa a pau, i na kaula hoi, e ala ana i ka wanaao e hoouna; aka, aole oukou i hoolohe, aole hoi i haliu mai i ko oukou pepeiao e lohe ai.
5 Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
I mai la lakou, E huli hou kela mea keia mea, mai kona aoao hewa mai, a mai ka hewa mai o ka oukou hana ana, a e noho hoi i ka aina a Iehova i haawi mai ai ia oukou, a i ko oukou poe makua, a hiki a kau, a hiki loa aku.
6 Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
A mai hele hoi mamuli o na akua e, e malama ia lakou, a e hoomana ia lakou; a mai hoonaukiuki mai oukou ia'u i na hana a ko oukou mau lima; alaila, aole au e hana ino ia oukou.
7 “Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
Aka, aole oukou i hoolohe mai ia'u, wahi a Iehova, i hoonaukiuki mai oukou ia'u i na hana a ko oukou mau lima, i mea e hewa'i oukou.
8 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
Nolaila, ke olelo mai o Iehova o na kaua; No ko oukou hoolohe ole i ka'u mau olelo,
9 ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
Aia hoi, e hoouna au, a lawe mai i na ohana kanaka a pau o ke kukulu akau, wahi a Iehova, a me Nebukaneza, ke alii o Babulona, ka'u kauwa, a e lawe mai au ia lakou e ku e i keia aina, a e ku e i kolaila poe kanaka, a e ku e hoi i keia mau lahuikanaka a pau e puni ana, a e luku loa ia lakou, a hoolilo ia lakou i mea e pilihua ai, a i mea e hoowahawaha ai, a i neoneo mau loa.
10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
A e lawe no wau, mai o lakou aku, i ka leo o ka olioli, a me ka leo o ka hauoli, i ka leo o ke kane mare, a me ka leo o ka wahine mare, i ke kani ana o na pohaku kaapalaoa, a me ka malamalama o ke kukui.
11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
A e lilo no keia aina a pau i neoneo, a i mea e pilihua'i. A e hookauwa aku ko keia mau aina na ke alii o Babulona, i kanahiku makahiki.
12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
A hiki i ka manawa i hala'e na makahiki he kanahiku, alaila, e hoopai aku au i ke alii o Babulona, a me ia lahuikanaka, wahi a Iehova, no ko lakou hewa, a i ka aina hoi o ko Kaledea, a e hoolilo no wau ia wahi, i neoneo mau loa.
13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
A e lawe aku au maluna o ia aina i ka'u mau olelo a pau a'u i hai ku e ia ia, i na mea a pau hoi i kakauia maloko o ka buke a Ieremia i wanana ai e ku e i na aina a pau.
14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
No ka mea, e hookauwa aku lakou na na lahuikanaka he nui, a na na'lii kaulana no hoi. A e hoouku no wau ia lakou, e like me ka lakou hana ana, a e like hoi me na hana a ko lakou lima iho.
15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
No ka mea, ke olelo mai nei o Iehova, ke Akua o ka Iseraela ia'u penei; E lawe oe i ke kiaha waina o keia ukiuki ma kuu lima, a e hoohainu aku ia i na lahuikanaka a pau a'u e hoouna aku ai ia oe io lakou la.
16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
A e inu no lakou, a e haalulu no, a e hehena iho, imua o ka pahikaua a'u e hoouna aku ai iwaena o lakou.
17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
A lawe iho la au i ke kiaha ma ka lima o Iehova, hoohainu aku la i na lahuikanaka a pau a Iehova i hoouna mai ai ia'u ia lakou:
18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
Ia Ierusalema hoi, a i na kulanakauhale o Iuda, a i kona poe alii, a i kona poe kaukaualii, e haawi hoi ia lakou no ka hooneoneoia, i mea e pilihua ai, a i mea hoowahawaha, a i mea e poino ai, e like me ia i keia la;
19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
Ia Parao i ke alii o Aigupita, a i kana poe kauwa, a i kana poe alii, a i kona poe kanaka a pau;
20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
A i na malihini a pau, a i na a'lii o ka aina o Uza, a i na'lii a pau o na aina o ko Pilisetia, a me Asekelona, a me Aza, a me Ekerona, a me ke koena o Asedoda;
21 Edomu, Mowabu ndi Amoni.
Ia Edoma, a me Moaba, a me na mamo a Amona;
22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
I na'lii a pau o Turo, ai na'lii a pau o na aina o Zidona, a i na'lii o na aina ma kela aoao o ke kai;
23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
Ia Dedana, a me Tema, a me Buza, a me na mea a pau ma na mokuna loihi loa aku;
24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
A i na'lii a pau o Arabia, a i na'lii a pau o na malihini e noho ana ma ka waonahele;
25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
A i na'lii a pau o Zimeri, a i na'lii a pau o Elama, a i na'lii a pau o Media;
26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
A i na'lii a pau o ke kukuluakau, ma kahi loihi aku, a ma kahi kokoke mai, kekahi i kekahi, a i na aupuni a pau o keia ao, maluna o ka honua nei; a e inu ke alii, o Sesaka mahope o lakou.
27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
A e olelo no oe ia lakou, Ke olelo mai nei o Iehova o na kaua, ke Akua o ka Iseraela peneia; E inu oukou a ona, a e luai aku, a e hina, aole hoi e ala hou, no ka pahikaua a'u e hoouna aku ai iwaena o oukou.
28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
A ina hoole lakou aole lawe i ke kiaha ma kou lima e inu ai, alaila, e olelo oe ia lakou, Ke olelo mai nei o Iehova o na kaua penei; E inu io auanei oukou.
29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
No ka mea, aia hoi, ke hoomaka nei au e lawe mai i ka hewa maluna o ke kulanakauhale i kapaia ma ko'u inoa, a e hoopai ole loa ia anei oukou? Aole ole ko oukou hoopaiia; no ka mea, e hea aku no wau i ka pahikaua, e hele ae maluna o ka poe a pau e noho la ma ka honua, wahi a Iehova o na kaua.
30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
A e wanana ku e oe ia lakou i keia mau olelo a pau, a e olelo ia lakou, E uwo mai no o Iehova, mailuna mai, a e haawi mai oia i kona leo, mai kahi e noho ai kona hemolelo mai; e uwo nui loa oia maluna o kona wahi noho ai; e like me ka poe hahi, pela no oia e hooho ai e ku e i ka poe e noho la ma ka honua.
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
E hiki mai no ka uwalaau, mai na kukulu mai o ka honua; no ka mea, he paio no ka Iehova me ko na aina, e hooponopono no oia maluna o na mea io a pau; e haawi no hoi oia i ka poe hewa i ka pahikaua, wahi a Iehova.
32 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
Ke olelo mai nei o Iehova o na kaua penei, Aia hoi, e puka no ka hewa, mai kekahi aina, a i kekahi aina; a e hoalaia ka puahiohio, mai na kukulu o ka honua mai.
33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
A i kela la, e palahalaha auanei ka poe i pepehiia e Iehova, mai kekahi kukulu o ka honua, a i kekahi kukulu: aole lakou e kumakenaia, aole hoi e hoiliiliia, aole e kanuia; e lilo lakou i lepo maluna o ka aina.
34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
E aoa oukou, e na kahuhipa, a e uwe aku; a e kapi ia oukou iho i ka lehu, e ka poe malama hipa; no ka mea, ua lawa ko oukou mau la o ka pepehi, a me ka hoopuehu, a e haule no oukou, e like me ke kiaha maikai.
35 Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
Aohe wahi no na kahuhipa e pee aku ai; aohe wahi hoi e pakele ai ka malama hipa.
36 Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
He leo hoi no ka uwe ana o na kahuhipa, a me ka aoa ana o ka poe malama hipa, no ka mea, ua anai o Iehova i ko lakou wahi e ai ai.
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
Ua hoopauia ko lakou wahi e noho ai me ka malu, no ka ukiuki nui o Iehova.
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
Ua haalele oia i kona wahi huna me he liona la; no ka mea, ua neoneo ko lakou aina, no ka huhu nui o ka mea hookaumaha, a no kona ukiuki loa.

< Yeremiya 25 >