< Yeremiya 25 >
1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
[the] word which to be upon Jeremiah upon all people Judah in/on/with year [the] fourth to/for Jehoiakim son: child Josiah king Judah he/she/it [the] year [the] first to/for Nebuchadnezzar king Babylon
2 Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
which to speak: speak Jeremiah [the] prophet upon all people Judah and to(wards) all to dwell Jerusalem to/for to say
3 Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
from three ten year to/for Josiah son: child Amon king Judah and till [the] day: today [the] this this three and twenty year to be word LORD to(wards) me and to speak: speak to(wards) you to rise and to speak: speak and not to hear: hear
4 Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
and to send: depart LORD to(wards) you [obj] all servant/slave his [the] prophet to rise and to send: depart and not to hear: hear and not to stretch [obj] ear your to/for to hear: hear
5 Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
to/for to say to return: repent please man: anyone from way: conduct his [the] bad: evil and from evil deed your and to dwell upon [the] land: soil which to give: give LORD to/for you and to/for father your to/for from forever: antiquity and till forever: enduring
6 Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
and not to go: went after God another to/for to serve: minister them and to/for to bow to/for them and not to provoke [obj] me in/on/with deed: work hand your and not be evil to/for you
7 “Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
and not to hear: hear to(wards) me utterance LORD because (to provoke me *Q(K)*) in/on/with deed: work hand your to/for bad: evil to/for you
8 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
to/for so thus to say LORD Hosts because which not to hear: obey [obj] word my
9 ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
look! I to send: depart and to take: bring [obj] all family north utterance LORD and to(wards) Nebuchadnezzar king Babylon servant/slave my and to come (in): bring them upon [the] land: country/planet [the] this and upon to dwell her and upon all [the] nation [the] these around and to devote/destroy them and to set: make them to/for horror: appalled and to/for hissing and to/for desolation forever: enduring
10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
and to perish from them voice rejoicing and voice joy voice son-in-law and voice daughter-in-law: bride voice: sound millstone and light lamp
11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
and to be all [the] land: country/planet [the] this to/for desolation to/for horror: destroyed and to serve [the] nation [the] these [obj] king Babylon seventy year
12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
and to be like/as to fill seventy year to reckon: punish upon king Babylon and upon [the] nation [the] he/she/it utterance LORD [obj] iniquity: crime their and upon land: country/planet Chaldea and to set: make [obj] him to/for devastation forever: enduring
13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
(and to come (in): bring *Q(k)*) upon [the] land: country/planet [the] he/she/it [obj] all word my which to speak: speak upon her [obj] all [the] to write in/on/with scroll: book [the] this which to prophesy Jeremiah upon all [the] nation
14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
for to serve in/on/with them also they(masc.) nation many and king great: large and to complete to/for them like/as work their and like/as deed: work hand their
15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
for thus to say LORD God Israel to(wards) me to take: take [obj] cup [the] wine [the] rage [the] this from hand my and to water: drink [obj] him [obj] all [the] nation which I to send: depart [obj] you to(wards) them
16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
and to drink and to shake and to be foolish from face: because [the] sword which I to send: depart between: among them
17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
and to take: take [obj] [the] cup from hand LORD and to water: drink [obj] all [the] nation which to send: depart me LORD to(wards) them
18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
[obj] Jerusalem and [obj] city Judah and [obj] king her [obj] ruler her to/for to give: make [obj] them to/for desolation to/for horror: destroyed to/for hissing and to/for curse like/as day: today [the] this
19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
[obj] Pharaoh king Egypt and [obj] servant/slave his and [obj] ruler his and [obj] all people his
20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
and [obj] all [the] racial-mix and [obj] all king land: country/planet [the] Uz and [obj] all king land: country/planet Philistine and [obj] Ashkelon and [obj] Gaza and [obj] Ekron and [obj] remnant Ashdod
21 Edomu, Mowabu ndi Amoni.
[obj] Edom and [obj] Moab and [obj] son: descendant/people Ammon
22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
and [obj] all king Tyre and [obj] all king Sidon and [obj] king [the] coastland which in/on/with side: beyond [the] sea
23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
and [obj] Dedan and [obj] Tema and [obj] Buz and [obj] all to cut side
24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
and [obj] all king Arabia and [obj] all king [the] Arabia [the] to dwell in/on/with wilderness
25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
and [obj] all king Zimri and [obj] all king Elam and [obj] all king Media
26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
and [obj] all king [the] north [the] near and [the] distant man: anyone to(wards) brother: compatriot his and [obj] all [the] kingdom [the] land: country/planet which upon face: surface [the] land: planet and king Babylon to drink after them
27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
and to say to(wards) them thus to say LORD Hosts God Israel to drink and be drunk and to vomit and to fall: fall and not to arise: rise from face: because [the] sword which I to send: depart between: among you
28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
and to be for to refuse to/for to take: recieve [the] cup from hand your to/for to drink and to say to(wards) them thus to say LORD Hosts to drink to drink
29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
for behold in/on/with city which to call: call to name my upon her I to profane/begin: begin to/for be evil and you(m. p.) to clear to clear not to clear for sword I to call: call to upon all to dwell [the] land: country/planet utterance LORD Hosts
30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
and you(m. s.) to prophesy to(wards) them [obj] all [the] word [the] these and to say to(wards) them LORD from height to roar and from habitation holiness his to give: cry out voice his to roar to roar upon pasture his shout like/as to tread to sing to(wards) all to dwell [the] land: country/planet
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
to come (in): come roar till end [the] land: country/planet for strife to/for LORD in/on/with nation to judge he/she/it to/for all flesh [the] wicked to give: put them to/for sword utterance LORD
32 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
thus to say LORD Hosts behold distress: harm to come out: come from nation to(wards) nation and tempest great: large to rouse from flank land: country/planet
33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
and to be slain: killed LORD in/on/with day [the] he/she/it from end [the] land: country/planet and till end [the] land: country/planet not to mourn and not to gather and not to bury to/for dung upon face: surface [the] land: soil to be
34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
to wail [the] to pasture and to cry out and to wallow great [the] flock for to fill day your to/for to slaughter and dispersion your and to fall: fall like/as article/utensil desire
35 Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
and to perish refuge from [the] to pasture and survivor from great [the] flock
36 Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
voice cry [the] to pasture and wailing great [the] flock for to ruin LORD [obj] pasturing their
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
and to silence: destroyed habitation [the] peace from face: because burning anger face: anger LORD
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
to leave: forsake like/as lion lair his for to be land: country/planet their to/for horror: destroyed from face: because burning anger [the] to oppress and from face: because burning anger face: anger his