< Yeremiya 25 >

1 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni.
The word that came to Jeremiah about all the people of Judah, in the fourth year of Jehoiakim, the son of Josiah, the king of Judah. The same is the first year of Nebuchadnezzar, the king of Babylon.
2 Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti:
And the prophet Jeremiah spoke to all the people of Judah, and to all the inhabitants of Jerusalem, saying:
3 Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.
“From the thirteenth year of Josiah, the son of Amon, the king of Judah, even until this day, which is the twenty-third year, the word of the Lord has been given to me, and I have spoken to you, rising while it was still night, and speaking, and yet you have not listened.
4 Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu.
And the Lord has sent to you all his servants, the prophets, rising at first light, and sending, and yet you have not listened, and you have not inclined your ears, so that you would hear,
5 Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya.
when he said: Return, each one from his evil way, and from your wicked thoughts. And you shall dwell in the land, which the Lord has given to you and to your fathers, from ancient times and even forever.
6 Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.
And do not choose to go after strange gods, so that you would serve them and adore them. And do not provoke me to wrath by the works of your hands. And then I will not afflict you.
7 “Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”
And yet you have not listened to me, says the Lord, and so you have provoked me to anger with the works of your hands, to your own harm.”
8 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga,
Because of this, thus says the Lord of hosts: “Since you have not listened to my words,
9 ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya.
behold, I will send for and take all the associates of the north, says the Lord, and Nebuchadnezzar, the king of Babylon, my servant, and I will lead them over this land, and over its inhabitants, and over all the nations that are around it. And I will destroy them, and I will set them in the midst of stupor and hissing, and continual desolations.
10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale.
And I will perish from them the voice of gladness and the voice of rejoicing, the voice of the groom and the voice of the bride, the sound of the millstone and the light of the lamp.
11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.
And this entire land will be in desolation and in stupor. And all these nations will serve the king of Babylon, for seventy years.
12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya.
And when the seventy years have been completed, I will visit their iniquity upon the king of Babylon, and upon that nation, and upon the land of the Chaldeans, says the Lord. And I will set it in continual desolations.
13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa.
And I will lead over that land all my words, which I have spoken against it, all that has been written in this book, everything whatsoever that Jeremiah has prophesied against all the nations.
14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”
For they have served them, though these were populous nations and great kings. And I will repay them according to their works and according to the deeds of their hands.”
15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma.
For thus says the Lord of hosts, the God of Israel: “Take the chalice of the wine of this fury from my hand. And you shall cause all the nations, to which I will send you, to drink from it.
16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”
And they will drink, and be stirred up, and become maddened, before the face of the sword that I will send among them.”
17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako:
And I received the chalice from the hand of the Lord, and I caused all the nations, to which the Lord has sent me, to drink from it:
18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino.
Jerusalem, and the cities of Judah, and its kings, and its leaders, so that I gave them over to desolation, and stupor, and hissing, and a curse, just as it is this day.
19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse,
“But as for Pharaoh, the king of Egypt, and his servants, and his leaders, and all his people,
20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi;
and the entire populace in general: all the kings of the land of the south, and all the kings of the land of the Philistines, and Ashkelon, and Gaza, and Ekron, and the remnant of Ashdod,
21 Edomu, Mowabu ndi Amoni.
and Idumea, and Moab, and the sons of Ammon,
22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja;
and all the kings of Tyre, and all the kings of Sidon, and the kings of the land of the islands that are across the sea,
23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali.
and Dedan, and Tema, and Buz, and all those who have shaved off their hair,
24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu.
and all the kings of Arabia, and all the kings of the west, who live in the desert,
25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya;
and all the kings of Zimri, and all the kings of Elam, and all the kings of Media,
26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.
and likewise, all the kings of the north from near to far, each one facing his brother, and all the kingdoms upon the face of the earth, and the king of Sesac: all these shall drink after them.
27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’
And you shall say to them: Thus says the Lord of hosts, the God of Israel: Drink, and be inebriated, and vomit, and fall down. And you shall not rise up before the face of the sword that I will send among you.
28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’”
And if they refuse to receive the cup from your hand and to drink, you shall say to them: Thus says the Lord of hosts: Certainly, you shall drink!
29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.
For behold, I am beginning to afflict the city in which my name has been invoked, and will you be innocent and immune? You will not be immune! For I will call the sword over all the inhabitants of the earth, says the Lord of hosts.
30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti, “‘Yehova adzabangula kumwamba; mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika. Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake. Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa, kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
And you shall prophesy to them all these words, and you shall say to them: The Lord will roar from on high, and he will utter his voice from his holy habitation. When roaring, he will roar over the place of his beauty. He will call out, like those who chant in rhythm as they trample the grapes, against all the inhabitants of the earth.
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi, chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse; adzaweruza mtundu wonse wa anthu ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’” akutero Yehova.
The sound of it will penetrate even to the ends of the earth. For the Lord is entering into judgment with the nations. He himself is entering into judgment with all flesh. I have delivered the impious to the sword, says the Lord.”
32 Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Taonani! Mavuto akuti akachoka pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina; mphepo ya mkuntho ikuyambira ku malekezero a dziko.”
Thus says the Lord of hosts: “Behold, an affliction will go forth from nation to nation, and a great whirlwind will go forth from the ends of the earth.
33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.
And the slain of the Lord will be, on that day, from one end of the earth, even to the other end. They will not be mourned, and they will not be gathered, and they will not be buried. They will lie upon the face of the earth like dung.
34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu; gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa. Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika; mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
Wail, O shepherds, and cry out! And sprinkle yourselves with ashes, O nobles of the flock! For the days have been completed that lead to your slaughter and your destruction. And you will fall like precious vessels.
35 Abusa adzasowa kothawira, atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
And escape will flee from the shepherds, and safety will flee from the nobility of the flock.”
36 Imvani kulira kwa abusa, atsogoleri a nkhosa akulira, chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
There is a voice of outcry from the shepherds, and a wailing among the nobles among the flock! For the Lord has laid waste to their pastures.
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
And the fields of peace have been silenced before the face of the fury of the Lord.
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake, pakuti dziko lawo lasanduka chipululu chifukwa cha nkhondo ya owazunza ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
He has abandoned those he sheltered like a lion. For the earth has become a desolation before the face of the anger of the dove, and before the face of the fury of the Lord.

< Yeremiya 25 >