< Yeremiya 24 >

1 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
PAN ukazał mi [widzenie], a oto dwa kosze fig [były] postawione przed świątynią PANA, gdy Nabuchodonozor, król Babilonu, uprowadził do niewoli Jechoniasza, syna Joakima, króla Judy, oraz książąt Judy, cieśli i kowali z Jerozolimy, i przyprowadził ich do Babilonu.
2 Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
Jeden kosz zawierał bardzo dobre figi, jakimi [są] figi dojrzałe, a drugi kosz zawierał bardzo złe figi, tak złe, że nie można było ich jeść.
3 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
I PAN zapytał mnie: Co widzisz, Jeremiaszu? Odpowiedziałem: Figi. Dobre figi [są] bardzo dobre, a złe [są] bardzo złe, tak złe, że nie można było ich jeść.
4 Tsono Yehova anandiwuza kuti,
I doszło do mnie słowo PANA mówiące:
5 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
Tak mówi PAN, Bóg Izraela: Jak [na] te dobre figi, tak spojrzę łaskawie na tych z Judy, którzy zostali uprowadzeni do niewoli, których wysłałem z tego miejsca do ziemi Chaldejczyków, dla ich dobra.
6 Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
I zwrócę na nich swoje oko dla [ich] dobra i przyprowadzę ich do tej ziemi, gdzie ich odbuduję, a nie zburzę, i zasadzę, a nie wykorzenię.
7 Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
Dam im bowiem serce, aby mnie poznali, że ja jestem PAN. Oni będą moim ludem, a ja będę ich Bogiem, gdyż nawrócą się do mnie całym swoim sercem.
8 “‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
A jak te złe figi, których nie można jeść, bo są tak złe, tak mówi PAN: Tak samo postąpię z Sedekiaszem, królem Judy, z jego książętami, z resztką Jerozolimy, która pozostała w tej ziemi, oraz z tymi, którzy mieszkają w ziemi Egiptu.
9 Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
Wydam ich na wysiedlenie i na ucisk we wszystkich królestwach ziemi, na pohańbienie i na przysłowie, na pośmiewisko i na przekleństwo we wszystkich miejscach, do których ich wypędzę.
10 Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”
I będę posyłał na nich miecz, głód i zarazę, aż będą wytraceni z ziemi, którą dałem im oraz ich ojcom.

< Yeremiya 24 >