< Yeremiya 24 >
1 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
Le Seigneur me fit voir, et voici deux paniers pleins de figues, placés devant le temple du Seigneur, après que Nabuchodonosor, roi de Babylone, eut transféré Jéchonias, fils de Joakim, roi de Juda, et ses princes, et l’artisan, et le lapidaire, loin de Jérusalem, et qu’il les eut emmenés à Babylone.
2 Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
L’un de ces paniers contenait des figues très bonnes, comme ont coutume d’être les figues de la première saison, et l’autre panier contenait des figues très mauvaises, qu’on ne pouvait manger, parce qu’elles étaient mauvaises.
3 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
Et le Seigneur me dit: Que vois-tu, Jérémie? Et je dis: Je vois des figues bonnes, très bonnes; et des mauvaises, très mauvaises, qui ne peuvent être mangées, parce qu’elles sont mauvaises.
4 Tsono Yehova anandiwuza kuti,
Et la parole du Seigneur me fut adressée, disant:
5 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
Voici ce que dit le Seigneur, Dieu d’Israël: Comme ces figues sont bonnes, ainsi je traiterai bien les fils de la transmigration que j’ai envoyés de ce lieu dans la terre des Chaldéens.
6 Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
Et je porterai sur eux un regard favorable, et je les ramènerai dans cette terre; je les rétablirai, et je ne les détruirai pas; je les planterai, et je ne les arracherai pas.
7 Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
Et je leur donnerai un cœur, afin qu’ils me connaissent, parce que moi je suis le Seigneur; et ils seront mon peuple, et je serai leur Dieu, parce qu’ils reviendront à moi en tout leur cœur.
8 “‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
Quant à ces figues très mauvaises, qui ne peuvent être mangées, parce qu’elles sont mauvaises, voici ce que dit le Seigneur: Ainsi je traiterai Sédécias, roi de Juda, et ses princes, et les restes de Jérusalem qui sont demeurés dans cette ville, et ceux qui habitent dans la terre d’Egypte.
9 Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
Je les livrerai en vexation et en affliction, dans tous les royaumes de la terre; en opprobre et en parabole, et en proverbe, et en malédiction dans tous les lieux dans lesquels je les aurai jetés.
10 Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”
Et j’enverrai contre eux le glaive, et la famine, et la peste, jusqu’à ce qu’ils soient exterminés de la terre que je leur ai donnée, à eux et à leurs pères.