< Yeremiya 24 >
1 Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda pamodzi ndi nduna zake, anthu aluso ndi akatswiri a ku Yuda ndi kupita nawo ku Babuloni. Pambuyo pake Yehova anandionetsa madengu awiri a nkhuyu atayikidwa pa khomo pa Nyumba ya Yehova.
Bangʼ ka Jehoyakin wuod Jehoyakim ruodh Juda kod jotelo, jopecho kod jogoro mag Juda ne oseter e twech koa Jerusalem nyaka Babulon gi Nebukadneza ruodh Babulon, Jehova Nyasaye nonyisa kikepni ariyo mag ngʼope koketi e nyim hekalu mar Jehova Nyasaye.
2 Mʼdengu limodzi munali nkhuyu zabwino kwambiri, ngati nkhuyu zoyambirira kucha. Mʼdengu linalo munali nkhuyu zoyipa kwambiri zosati nʼkudya.
Okapu achiel ne nigi ngʼope mabeyo ahinya, kod mago mane osechiek chon; okapu machielo ne nigi ngʼope maricho, marach moloyo ma ok nyal cham.
3 Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ndinayankha kuti, “Ndikuona nkhuyu zabwino kwambiri ndi nkhuyu zoyipa zosati nʼkudya.”
Eka Jehova Nyasaye nopenja niya, “En angʼo mineno, Jeremia?” Ne odwoko niya, “Aneno ngʼope. Mabeyo to beyo ahinya, to maricho to richo ahinya ma ok nyal cham.”
4 Tsono Yehova anandiwuza kuti,
Eka wach Jehova Nyasaye nobirona:
5 “Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, ‘Anthu a ku Yuda amene ndinawachotsa ku malo ano nʼkupita nawo ku ukapolo ku dziko la Ababuloni ndikuwafanizira ndi nkhuyu zabwinozi.
“Ma e gima Jehova Nyasaye, Nyasach Israel, wacho: ‘Ka ngʼope mabeyogi, akawo jogo moa Juda kodhi e twech kaka joma beyo, mane agolo kae kadhi e piny jo-Babulon.
6 Ndidzaonetsesa kuti ndiwachitire zabwino ndipo ndidzabwera nawonso ku dziko lino. Ndidzawamanga osati kuwapasula; ndidzawadzala osati kuwazula.
Wengena nongʼigi mondo gidhi maber, kendo anadwog-gi e pinyni. Anagergi kendo ok anamukgi; anapidhgi kendo ok anapudhgi.
7 Ndidzawapatsa mtima woti andidziwe kuti ndine Yehova. Adzakhala anthu anga ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo, chifukwa adzabwerera kwa Ine ndi mtima wawo wonse.
Anamigi chuny mar ngʼeya ni an Jehova Nyasaye. Ginibed joga kendo anabed Nyasachgi, nimar giniduog ira gi chunygi duto.’
8 “‘Koma monga nkhuyu zoyipa zija, zomwe ndi zoyipa kwambiri zosati nʼkudya,’ Yehova akuti, ‘ndi mmene ndidzalangire Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi otsala a mu Yerusalemu, kaya adzakhala ali mʼdziko muno kapena mʼdziko la Igupto.
“Jehova Nyasaye wacho ni, ‘To mana kaka ngʼope maricho, ma ok nyal cham, e kaka anatimne Zedekia ruodh Juda, jotende kod jogo motony moa Jerusalem, kata obedo ni gidongʼ e pinyni kata gidak Misri.
9 Ndidzawasandutsa chinthu chonyansa kwa maufumu onse a dziko lapansi, chinthu chonyozeka ndi chopandapake, chinthu chochitidwa chipongwe ndi chotembereredwa kulikonse kumene ndidzawabalalitsira.
Abiro kelo kuomgi achaya kendo joma ok dwar gi pinjeruodhi duto manie piny, ma wangʼo ich kendo itiyo godo kaka ranyisi, gima ibwogogo ji kendo ikwongʼogo, ka moro amora ma aterogie.
10 Ndidzawatumizira nkhondo, njala ndi mliri mpaka atawonongedwa mʼdziko limene ndinawapatsa iwo ndi makolo awo.’”
Anakel ligangla, kech kod masira kuomgi nyaka tiekgi e piny mane amiyogi kod wuonegi.’”