< Yeremiya 23 >
1 “Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
Biada pasterzom gubiącym i rozpraszającym trzodę pastwiska mego! mówi Pan.
2 Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
Przetoż tak mówi Pan, Bóg Izraelski, do pasterzy, którzy pasą lud mój: Wy rozpraszacie owce moje, owszem, rozganiacie je, a nie nawiedzacie ich; oto Ja nawiedzę was dla złości spraw waszych, mówi Pan.
3 “Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
A ostatek owiec moich Ja zgromadzę ze wszystkich ziem, do którychem je rozegnał, i przywrócę je do obór ich, gdzie się rozpłodzą i rozmnożą.
4 Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
Nadto posanowię nad niemi pasterzy, którzyby je paśli, aby się więcej nie lękały, ani strachały, i żeby ich nie ubywało, mówi Pan.
5 Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
Oto idą dni, mówi Pan, których wzbudzę Dawidowi latorośl sprawiedliwą, i będzie królował król, a poszczęści mu się; sąd zaiste i sprawiedliwość będzie czynił na ziemi.
6 Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
Za dni jego Juda zbawiony będzie, a Izrael bezpiecznie mieszkać będzie; a toć jest imię jego, którem go zwać będą: Pan sprawiedliwość nasza.
7 Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
Przetoż oto przychodzą dni, mówi Pan, których nie rzeką więcej: Jako żyje Pan, który wywiódł synów Izraelskich z ziemi Egipskiej.
8 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
Ale: Jako żyje Pan, który wywiódł, i który sprowadził nasienie domu Izraelskiego z ziemi północnej i ze wszystkich ziem, do którychem ich był rozegnał; gdyż będą mieszkać w ziemi swoiej.
9 Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
Dla proroków skruszyło się serce moje we mnie, poruszyły się wszystkie kości moje, stałem się jako człowiek pijany, a jako mąż, po którym się rozeszło wino, dla Pana i dla słów świętobliwości jego.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
Bo ta ziemia pełna jest cudzołożników, a dla krzywoprzysięstwa płacze ta ziemia, pastwiska na puszczy poschły; zaiste zły jest bieg ich, a moc ich nieprawa.
11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
Bo i prorok i kapłan są obłudnikami, a domu moim znajduje się złość ich, mówi Pan.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
Przetoż im będzie droga ich jako ślizgawica w ciemności, na którą wepchnieni będą i upadną, gdy przywiodę na nich biedę czasu nawiedzenia ich, mówi Pan.
13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
Także przy prorokach Samaryjskich widziałem głupstwo, prorokowali przez Baale, i zwodzili lud mój Izraelski.
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
Ale przy prorokach Jeruzalemskich widzę rzecz brzydką, że cudzołożąc i kłamliwie się obchodząc utwierdzają też ręce złośników, aby się nie nawracali żaden od złości swojej; stali się wszyscy przedemną jako Sodoma, a obywatele jego jako Gomora.
15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
Dlategoż tak mówi Pan zastępów o tych prorokach: Oto Ja nakarmię ich piołunem, a napoję ich wodą gorzką; bo od proroków Jeruzalemskich wyszło splugawienie na tę wszystkę ziemię.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
Tak mówi Pan zastępów: Nie słuchajcie słów tych proroków, którzy wam prorokują, i zwodzą was, widzenie serca swego opowiadają, a nie z ust Pańskich;
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
Ustawicznie mówią tym, którzy mną gardzą: Pan mówił, pokój mieć będziecie; i każdemu chodzącemu według uporu serca swego, mówią: Nie przyjdzie na was nic złego.
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
Bo któż stanął w radzie Pańskiej, a widział i słyszał słowo jego? kto pilnował słowa jego, i słuchał go?
19 Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
Oto wicher Pański z zapalczywością wyjdzie, a wicher trwały nad głową niepobożnych zostanie;
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
Nie odwróci się gniew Pański, aż uczyni i wykona myśli serca swego; w ostateczne dni to doskonale zrozumiecie.
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
Nie posyłałem tych proroków, a wszakże bieżeli; nie mówiłem do nich, a wszakże oni prorokowali,
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
Bo gdyby byli stali w radzie mojej, tedyby byli ogłaszali słowa moje ludowi memu, a byliby ich odwracali od drogi ich złej, i od złości spraw ich.
23 Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
Izalim Ja tylko Bogiem z bliska? mówi Pan, a nie jestem Bogiem i z daleka?
24 Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
Izali się kto skryje w skrytości, abym go Ja nie widział? mówi Pan. Izali Ja nieba i ziemi nie napełniam? mówi Pan.
25 “Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
Słyszęć Ja, co mówią prorocy, którzy prorokują, kłamstwo w imieniu mojem, mówiąc: Śniło mi się, śniło mi się!
26 Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
Długoż tego będzie? Izali w sercu tych proroków, którzy prorokują, niemasz kłamstwa? owszem, są prorokami zdrady serca swego;
27 Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
Którzy myślą, jakoby z pamięci wywieść ludowi mojemu imię moje snami swemi, które powiadają każdy bliźniemu swemu, jako zapomnieli ojcowie ich na imię moje dla Baala.
28 Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
Prorok, który ma sen, niech powiada sen: ale który ma słowo moje, niech mówi słowo moje w prawdzie. Cóż plewie do pszenicy? mówi Pan.
29 Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
Izali słowo moje nie jest jako ogień? mówi Pan, i jako młot kruszący skałę?
30 Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
Przetoż oto Ja powstaję przeciwko tym prorokom, mówi Pan, którzy kradną słowa moje, każdy przed bliźnim swoim.
31 Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
Oto Ja powstaję przeciwko tym prorokom, mówi Pan, którzy używają języka swego, aby mówili: Mówi Pan.
32 Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
Oto Ja powstaję, mówi Pan, przeciwko tym, którzy prorokują sny kłamliwe, a opowiadając je zwodzą lud mój kłamstwami swemi i plotkami swemi, chociażem Ja ich nie posłał, anim im rozkazał; skąd zgoła nic nie pomagają ludowi twemu, mówi Pan.
33 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
Przetoż gdyby się ciebie pytał lud ten, albo prorok, albo kapłan, mówiąc: Cóż jest za brzemię Pańskie? Tedy rzeczesz do nich które brzemię. To: Opuszczę was, mówi Pan.
34 Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
Bo proroka i kapłana tego, i lud ten, któryby rzekł: Toć jest brzemię Pańskie, pewnie nawiedzę męża tego i dom jego.
35 Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
Ale tak mówcie każdy do bliźniego swego, i każdy do brata swego: Cóż odpowiedział Pan? albo: Cóż mówił Pan?
36 Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
A brzmienia Pańskiego nie wspominajcie więcej; bo brzmieniem będzie każdemu słowo jego, gdyżeście wy wywrócili słowa Boga żywego, Pana zastępów, Boga naszego.
37 Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
Tak tedy rzeczesz do proroka: Cóż ci odpowiedział Pan? albo: Co mówił Pan?
38 Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
Ale ponieważ mówicie: Brzemię Pańskie, tedy tak mówi Pan: Ponieważ mówicie to słowo: Brzemię Pańskie, chociażem do was posyłał, mówiąc: Nie mówcie: Brzemię Pańskie;
39 ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
Przetoż oto i Ja was zapomnę do końca, i odrzucę was i to miasto, którem wam dał i ojcom waszym, od oblicza mego;
40 Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”
I podam was na urąganie wieczne, i na hańbę wieczną, która nigdy nie przyjdzie w zapamiętanie.