< Yeremiya 23 >

1 “Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
Malheur aux pasteurs qui ruinent et dispersent les brebis de mon troupeau!" dit l’Eternel.
2 Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
C’Est pourquoi, voici ce que déclare l’Eternel, Dieu d’Israël, à l’encontre des pasteurs qui mènent mon peuple: "C’Est vous qui avez dispersé mes brebis, qui les avez fourvoyées et n’en avez pris nul soin. Eh bien, moi, j’aurai soin de vous châtier pour vos mauvaises actions, dit l’Eternel."
3 “Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
Moi, je rassemblerai les restes de mon troupeau de toutes les terres où je les ai relégués, je les ramènerai à leur pâturage, pour qu’ils y croissent et s’y multiplient.
4 Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
J’Établirai sur eux des pasteurs qui les feront paître, et ils n’auront plus de crainte, ils n’auront plus d’alarme, et il ne s’en perdra plus, dit l’Eternel.
5 Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
Voici que des jours viennent, dit l’Eternel, où je susciterai à David un rejeton juste, qui régnera en roi, agira avec sagesse et exercera le droit et la justice dans le pays.
6 Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
En ses jours, Juda sera sauf et Israël habitera en pleine sécurité, et voici le nom qu’on lui donnera: "L’Eternel est mon Droit!"
7 Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
En vérité, des jours viendront, dit l’Eternel, où l’on ne dira plus: "Vive l’Eternel qui a fait monter les enfants d’Israël du pays d’Egypte!"
8 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
mais "Vive l’Eternel qui a fait monter, qui a ramené les descendants de la maison d’Israël du pays du Nord et de toutes les contrées où je les avais relégués, pour qu’ils demeurent dans leur patrie!"
9 Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
Au sujet des prophètes: mon coeur s’est brisé en moi, tous mes membres sont frémissants, je suis comme un homme ivre, comme quelqu’un maîtrisé par le vin, à cause de l’Eternel et de ses saintes paroles.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
Car le pays est rempli de gens adultères; car par suite des parjures, le pays est en deuil, les pâturages de la campagne sont desséchés; ils se précipitent vers le mal et usent leur force pour le mensonge.
11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
Oui, même le prophète, même le prêtre sont infâmes; jusque dans ma maison, je constate leur perversité, dit l’Eternel.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
C’Est pourquoi la voie qu’ils suivent deviendra pour eux comme un terrain glissant en pleines ténèbres; ils seront bousculés et y tomberont, quand je ferai arriver sur eux la catastrophe, l’année de leur châtiment, dit l’Eternel.
13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
Aussi chez les prophètes de Samarie, j’avais vu des choses écoeurantes; ils prophétisaient au nom de Baal et égaraient mon peuple Israël.
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
Mais chez les prophètes de Jérusalem j’ai remarqué des abominations: ils pratiquent l’adultère, vivent dans le mensonge, prêtent main-forte aux malfaiteurs, de façon que personne ne revienne de sa perversité. Tous, ils sont devenus à mes yeux comme gens de Sodome, et les habitants de Jérusalem comme gens de Gomorrhe.
15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
C’Est pourquoi, ainsi parle l’Eternel-Cebaot au sujet des prophètes: Voici, je vais leur donner des plantes vénéneuses à manger et des eaux empoisonnées à boire, car c’est des prophètes de Jérusalem que la corruption s’est propagée dans tout le pays.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
Voici ce que dit l’Eternel-Cebaot: N’Écoutez point les discours des prophètes qui vous adressent des prophéties; ils vous bercent de chimères, ils vous débitent des visions de leur invention, que l’Eternel n’a point inspirées.
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
Ils ne cessent de répéter à mes détracteurs: "L’Eternel a parlé; vous aurez la paix." Tous ceux qui suivent les penchants de leur coeur, ils leur disent: "Aucun malheur ne vous atteindra."
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
Qui donc parmi eux a assisté au conseil de l’Eternel, de manière à voir, de manière à entendre sa parole? Qui a pu tendre l’oreille à ses discours et les recueillir?
19 Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
Voici, la tempête de l’Eternel éclate avec fureur, un ouragan se déchaîne, qui s’abattra sur la tête des coupables.
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
La colère de l’Eternel ne cessera de sévir que quand il aura exécuté, accompli les desseins de son coeur; plus tard, vous en comprendrez le sens.
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
Je n’avais point donné de mission à ces prophètes, et ils se sont mis à courir! Je ne leur avait point adressé la parole, et ils ont prophétisé!
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
S’Ils avaient assisté à mon conseil, mais alors ils auraient fait entendre mes paroles à mon peuple, ils l’auraient détourné de sa mauvaise voie et de ses mauvaises actions.
23 Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
Suis-je donc Dieu de près, dit l’Eternel, et non pas Dieu de loin?
24 Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
Quelqu’un peut-il se cacher dans un lieu occulte, sans que je le voie? dit l’Eternel. Est-ce que je ne remplis pas le ciel et la terre? dit l’Eternel.
25 “Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
J’Entends bien ce que disent les prophètes qui prophétisent faussement en mon nom, à savoir: "J’Ai eu un songe, j’ai eu un songe!"
26 Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
Jusques à quand en sera-t-il ainsi? Entre-t-il donc dans la pensée des prophètes, prophètes de mensonge, qui débitent les perfides inventions de leur coeur,
27 Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
entre-t-il dans leurs calculs de faire oublier mon nom à mon peuple, grâce à leurs songes qu’ils se content mutuellement, de même que leurs ancêtres ont oublié mon nom pour Baal?
28 Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
Que le prophète qui se targue d’un songe raconte ce songe! Mais que celui qui est favorisé de ma parole annonce fidèlement ma parole: que vient faire la paille avec le grain? dit l’Eternel.
29 Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
Est-ce que ma parole ne ressemble pas au feu, dit l’Eternel, et au marteau qui fait voler en éclats le rocher?
30 Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
Aussi vais-je prendre à partie, dit l’Eternel, les prophètes qui se dérobent les uns aux autres mes révélations.
31 Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
Je vais prendre à partie, dit l’Eternel, les prophètes qui font marcher leur langue et prononcent des oracles.
32 Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
Je vais prendre à partie, dit l’Eternel, les diseurs de songes trompeurs, qui les divulguent pour égarer mon peuple par leurs mensonges et leur verbiage frivole, alors que je ne leur ai donné ni mission ni ordre, et qu’ils ne peuvent rendre aucun service à ce peuple, dit l’Eternel.
33 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
Que si ce, peuple, si prophètes ou prêtres t’interrogent en ces termes: "Quel est l’oracle de l’Eternel?" tu leur répondras ce qu’est l’oracle: "Je vais vous rejeter!" dit l’Eternel.
34 Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
Quant au prophète, au prêtre, à l’homme du peuple qui dira: "Oracle de l’Eternel", je le châtierai, cet individu, ainsi que sa maison.
35 Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
Voici comme vous vous exprimerez en parlant entre vous: "Quelle réponse a faite l’Eternel? Quelle est la parole prononcée par l’Eternel?"
36 Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
Mais le mot "oracle" de l’Eternel (Massa), vous n’en ferez plus mention; car la parole de l’Eternel communiquée à l’homme est bien un oracle (Massa), mais vous dénaturez les paroles du Dieu vivant, de l’Eternel-Cebaot, notre Dieu.
37 Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
Voici donc ce que vous pourrez dire au prophète: "Quelle réponse t’a faite l’Eternel? Quelle est la parole prononcée par l’Eternel?"
38 Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
Mais si vous parlez de Massa de l’Eternel, assurément alors l’Eternel dira: "Puisque vous employez cette expression de Massa de l’Eternel, malgré cette défense que je vous ai fait adresser: Ne dites pas Massa de l’Eternel,
39 ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
voici, je vais vous repousser complètement, vous rejeter, vous et la ville que j’ai donnée à vous et à vos ancêtres, de devant ma face,
40 Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”
et je ferai peser sur vous un éternel déshonneur, un opprobre permanent et inoubliable.

< Yeremiya 23 >