< Yeremiya 23 >

1 “Tsoka kwa abusa amene akuwononga ndi kubalalitsa nkhosa za pabusa panga!” akutero Yehova.
Горко на пастирите, Които погубват и разпръсват овцете на паството Ми! казва Господ.
2 Nʼchifukwa chake Yehova, Mulungu wa Israeli, ponena za abusa amene akuweta anthu anga akuti, “Mwabalalitsa ndi kumwaza nkhosa zanga. Komanso simunazisamale bwino. Choncho ndidzakulangani chifukwa cha machimo anu,” akutero Yehova.
Затова, така говори Господ Израилевият Бог Против пастирите, които пасат людете Ми: Вие разпръснахте овцете Ми, и ги разпъдихте, И не ги посетихте; Ето, Аз ще ви накажа За злите ви дела, казва Господ.
3 “Pambuyo pake Ine mwini wakene ndidzasonkhanitsa nkhosa zanga zotsala, kuzichotsa ku mayiko onse kumene ndinazibalalitsira ndi kuzibweretsanso ku msipu wawo. Kumeneko zidzaswana ndi kuchulukana.
И ще събера останалите Си овце от всичките страни, гдето ги изпъдих, И ще ги върна пак в кошарите им, Гдето ще се наплодят и умножат.
4 Ndidzazipatsa abusa amene adzaziweta, ndipo sizidzaopanso kapena kuchita mantha, ndipo palibe imene idzasochera,” akutero Yehova.
И ще поставя над тях пастири, които ще ги пасат; И те няма да се плашат вече, нито ще треперят, Нито ще загине някоя, казва Господ.
5 Yehova akuti, “Masiku akubwera, pamene ndidzaphukitsira Davide Nthambi yowongoka. Imeneyi ndiye mfumu imene idzalamulira mwanzeru, mwachilungamo ndi mosakondera mʼdziko.
Ето, идат дни, казва Господ, Когато ще въздигна на Давида праведен отрасъл, Който като цар ще царува, ще благоденствува, И ще върши правосъдие и правда по земята.
6 Pa masiku a ulamuliro wake Yuda adzapulumuka ndipo Israeli adzakhala pamtendere. Dzina limene adzamutcha ndi ili: Yehova ndiye Chilungamo Chathu.
В неговите дни Юда ще бъде спасен, И Израил ще обитава в безопасност; И ето името, с което ще се нарича - Господ е Наша Правда.
7 Choncho, masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene anthu sadzanenanso polumbira kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa Aisraeli ku Igupto,’
Затова, ето, идат дни, казва Господ, Когато не ще рекат вече: Заклеваме се в в живота на Господа, Който възведе Израилтяните из Египетската земя!
8 koma adzanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo, amene anatulutsa zidzukulu za Israeli ku dziko lakumpoto ndi ku mayiko konse kumene anawabalalitsira.’ Ndipo iwo adzawabweretsa ku dziko lawolawo.”
Но: Заклеваме се в живота на Господа, Който възведе и който доведе потомството на Израилевия дом От северната земя, и от всичките страни, гдето ги бях изгонил! И ще се заселят в своята земя.
9 Kunena za aneneri awa: Mtima wanga wasweka; mʼnkhongono mwati zii. Ndakhala ngati munthu woledzera, ngati munthu amene wasokonezeka ndi vinyo, chifukwa cha Yehova ndi mawu ake opatulika.
За Пророците. Сърцето ми дълбоко се съкрушава Всичките ми кости треперят, Като пиян съм, И като човек, обладан от вино, Поради Господа, И поради светите Негови думи.
10 Dziko ladzaza ndi anthu achigololo; lili pansi pa matemberero. Dziko lasanduka chipululu ndipo msipu wawuma. Aneneri akuchita zoyipa ndipo akugwiritsa ntchito mphamvu zawo molakwika.
Защото земята е пълна с прелюбодейци; Защото поради проклятията земята плаче, Изсъхнаха пасбищата на степите; И стремежът им стана лош, И силата им неправедна.
11 “Mneneri ngakhale wansembe onse sapembedza Yehova. Amachita zoyipa ngakhale mʼnyumba yanga,” akutero Yehova.
Защото и пророкът и свещеникът се оскверниха; Дори в дома Си намерих нечестието им, казва Господ.
12 “Nʼchifukwa chake njira zawo zidzakhala zoterera; adzawapirikitsira ku mdima ndipo adzagwera kumeneko. Adzaona zosaona mʼnthawi ya chilango chawo,” akutero Yehova.
Затова, пътят им ще бъде Като плъзгави места в тъмнина, По който, като бъдат тласкани, ще паднат; Защото ще докарам зло върху тях В годината на наказанието им, казва Господ.
13 “Pakati pa aneneri a ku Samariya ndinaona chonyansa ichi: Ankanenera mʼdzina la Baala ndipo anasocheretsa anthu anga, Aisraeli.
Тоже в Самарийските пророци видях безумие; Те пророкуваха чрез Ваала, и заблудиха людете Ми Израиля.
14 Ndipo pakati pa aneneri a ku Yerusalemu ndaonapo chinthu choopsa kwambiri: amachita chigololo, amanena bodza ndipo amalimbitsa mtima anthu ochita zoyipa. Choncho palibe amene amasiya zoyipa zake. Kwa Ine anthu onsewa ali ngati a ku Sodomu ndi Gomora.”
Още и в Ерусалимските пророци видях ужасно нещо; Прелюбодействуват, и ходят в лъжа, И подкрепват ръцете на злодейците, Тъй щото никой не се връща от злото си; Те всички станаха за Мене като Содом, И жителите му като Гомор.
15 Choncho ponena za aneneriwa Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndidzawadyetsa zakudya zowawa ndi kuwamwetsa madzi a ndulu, chifukwa uchimo umene wafalikira mʼdziko lonse ndi wochokera kwa aneneri a ku Yerusalemuwa.”
Затова, така казва Господ на Силите за пророците: Ето, Аз ще ги нахраня с пелин, И ще ги напоя с горчива вода; Защото от Ерусалимските пророци Се е разпространило нечестие по цялата страна.
16 Koma Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Musamvere zimene aneneri amenewa akulosera kwa inu; zomwe aloserazo nʼzachabechabe. Iwo akungoyankhula za masomphenya a mʼmitima mwawo basi, osati zochokera kwa Yehova.
Така казва Господ на Силите: Не слушайте думите на пророците, които ви пророкуват; Те ви учат суета, Изговарят видения от собственото си сърце, А не от устата Господни.
17 Iwo amapita ndi kumakawuza amene amandinyoza Ine kuti, ‘zinthu zidzakuyenderani bwino.’ Kwa iwo amene amawumirira kutsata zofuna za mitima yawo amakawawuza kuti, ‘palibe choyipa chimene chidzakugwereni.’”
На ония, които Ме презират, винаги казват: Господ рече: Ще имате мир; И на всекиго, който ходи по своето упорито сърце, казват: Няма да ви постигне зло.
18 Ine ndikuti, “Koma ndani wa iwo amene anakhalapo mu msonkhano wa Yehova? Ndani anaonapo kapena kumvapo mawu ake? Ndani mwa iwo analabadirako za mawu ake ndi kuwamvera?
Защото кой от тях е стоял в съвета на Господа Та е видял и чул Неговото слово? Кой от тях е внимавал в словото Му и е чул?
19 Taonani ukali wa Yehova uli ngati chimphepo chamkuntho, inde ngati namondwe. Ndipo adzakantha mitu ya anthu oyipa.
Ето, ураган от Господа, неговата ярост, излезе, Дори ураган-вихрушка; Ще избухне върху главата на нечестивите.
20 Mkwiyo wa Yehova sudzaleka mpaka atachita zonse zimene anatsimikiza mu mtima mwake. Mudzazizindikira bwino zimenezi masiku akubwerawa.”
Гневът на Господа няма да се върне Догдето Той не извърши, и догдето не изпълни Намеренията на сърцето Си; В послешните дни ще разберете това напълно.
21 Yehova anati, “Ine sindinatume aneneri amenewa, komabe iwo athamanga uku ndi uku kulalikira uthenga wawo; Ine sindinawayankhule, komabe iwo ananenera.
Аз не съм изпратил тия пророци, а при все това те се завтекоха; Не им съм говорил, а при все това те пророкуваха.
22 Iwo akanakhala pa msonkhano wanga ndiye kuti akanamayankhula mawu anga kwa anthu anga. Komanso bwenzi atawachotsa anthu anga mʼnjira zawo zoyipa kuti aleke machimo awo.”
Но ако бяха стояли в съвета Ми, Тогава те щяха да правят людете Ми да чуят думите Ми, И щяха да ги връщат от лошия им път И от злите им дела.
23 Yehova akuti, “Kodi ndimakhala Mulungu pokhapokha ndikakhala pafupi, ndiye sindine Mulungu?
Аз само отблизо ли съм Бог, казва Господ, А не Бог и отдалеч?
24 Kodi wina angathe kubisala Ine osamuona?” “Kodi Ine sindili ponseponse kumwamba ndi dziko lapansi?” Akutero Yehova.
Може ли някой да се скрие в тайни места, Та аз да го не видя? казва Господ. Не аз ли изпълвам небесата и земята? казва Господ.
25 “Ndamva zimene aneneri akuyankhula. Iwo amalosera zabodza mʼdzina langa nʼkumati, ‘Ndalota! Ndalota!’
Чух що говорят пророците, Които в Мое име пророкуват лъжа, Като казват: Видях сън, видях сън!
26 Kodi zabodzazi zidzakhalabe mʼmitima ya aneneriwa mpaka liti? Iwotu amalosera zonyenga za mʼmitima yawo.
До кога ще бъде това в сърцето на пророците, Които пророкуват лъжа, - На ония, които пророкуват измамата на своето сърце?
27 Aneneriwa amakhulupirira kuti anthu anga adzayiwala mawu anga akamamva za maloto awo amene amayankhulana ngati mmene anachitira makolo awo popembedza Baala.
Които мислят да направят людете Ми да забравят Моето име Чрез сънищата си, които разказват всеки за ближния си, Както забравиха бащите им името Ми заради Ваала.
28 Mneneri amene ali ndi maloto afotokoze malotowo. Koma iye amene ali ndi mawu anga alalikire mawuwo mokhulupirika. Kodi phesi lingafanane ndi chimanga?
Пророк, който има истински сън, нека разказва съня, И оня, който има послание от Мене, нека говори Моето послание вярно. Що има плявата с житото? казва Господ.
29 Kodi suja mawu anga amatentha ngati moto? Suja mawu anga amaphwanya monga ichitira nyundo kuphwanya miyala?” Akutero Yehova.
Не е ли словото Ми като огън? казва Господ, И като чук, който строшава скалата?
30 Yehova akuti, “Nʼchifukwa chake, Ine ndikudana nawo aneneri amene amaberana okhaokha mawu nʼkumati mawuwo ndi a Yehova.”
Затова, ето, Аз съм против пророците, казва Господ, Които крадат думите Ми всеки от ближния си.
31 Yehova akuti, “Inde, Ine ndikudana ndi aneneri amene amakonda kuyankhula zabodza nʼkumanena kuti, ‘Amenewa ndi mawu a Yehova.’”
Ето, Аз съм против пророците, казва Господ, Които клатят езиците си и казват: Той говори.
32 Yehova akuti, “Ndithudi, Ine ndikudana ndi aneneri a maloto abodzawa. Iwo amafotokoza malotowo nʼkumasocheretsa anthu anga ndi bodza lawo losachita nalo manyazilo, chonsecho Ine sindinawatume kapena kuwalamula. Iwo sathandiza anthuwa ndi pangʼono pomwe,” akutero Yehova.
Ето, аз съм против ония, които пророкуват лъжливи сънища, казва Господ, И, като ги разказват, с лъжите си и с надменността си Правят людете Ми да се заблуждават, Тогаз когато Аз не съм ги изпратил, нито им съм заповядал; Прочее, те никак няма да ползуват тия люде, казва Господ.
33 Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Anthu awa, kapena mneneri, kapenanso wansembe, akakufunsa kuti, ‘Kodi uthenga wolemetsa wa Yehova ukuti chiyani?’ uwawuze kuti, ‘Inuyo ndinu katundu wolemetsa Yehova, ndipo adzakutayani.’
И когато тия люде, Или някой пророк или свещеник, те попитат като рекат: Какво е наложеното върху тебе от Господа слово? Тогава да им кажеш що е наложеното, - Че Господ дума: Аз ще ви отхвърля.
34 Ngati mneneri kapena wansembe kapenanso munthu wina aliyense anena kuti, ‘Uthenga wolemetsa wa Yehova ndi uwu,’ Ine ndidzalanga munthu ameneyo pamodzi ndi banja lake.
А колкото за пророка, свещеника и оня от людете, Който би рекъл: Наложеното от Господа слово! Аз ще накажа оня човек и дома ум.
35 Koma chimene aliyense wa inu azifunsa kwa mnzake kapena mʼbale wake ndi ichi: ‘Kodi Yehova wayankha chiyani?’ kapena ‘Yehova wayankhula chiyani?’
Така да речете всеки на ближния си И всеки на брата си: Какво е отговорил Господ? Или: Що е рекъл Господ?
36 Koma musanenenso kuti ‘nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ chifukwa mawu a munthu aliyense ndiwo uthenga wa iye mwini, kotero kuti inu mumakhotetsa mawu a Mulungu wamoyo, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wathu.
А да не споменете вече - Наложеното от Господа слово; Понеже товар ще бъде на всекиго Неговото слово; Защото извратихте думите на живия Бог, На Господа на Силите, нашия Бог.
37 Tsono iwe Yeremiya udzamufunse mneneri kuti, ‘Kodi Yehova wakuyankha chiyani?’ kapena, ‘Kodi Yehova wayankhula chiyani?’
Така да кажеш на пророка: Какво ти е отговорил Господ? Или: Що е рекъл Господ?
38 Ngati mudzanena kuti, ‘Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova,’ ndiye tsono Yehova akuti, ‘Popeza mwagwiritsa ntchito mawu akuti: Nawu uthenga wolemetsa wa Yehova, mawu amene ndinakuletsani kuti musawatchule,
Но понеже казвате: Наложеното от Господа слово, Затова, така казва Господ: Понеже употребяват това изречение - Наложеното от Господа слово, При все, че Аз пратих до вас да ви кажат Да не казвате - Наложеното от Господа слово,
39 ndiye kuti Ine ndidzakunyamulani ngati katundu nʼkukuponyani kutali. Ndidzakuchotsani pamaso panga, inuyo pamodzi ndi mzinda umene ndinakupatsani inu ndi makolo anu.
Затова, ето, Аз ще ви забравя съвсем, И ще отхвърля от присъствието си вас И град, който дадох вам и на бащите ви;
40 Ndidzakunyozani mpaka muyaya. Ndidzakuchititsani manyazi osayiwalika.’”
И ще докарам върху вас вечен укор, И вечно посрамление, което няма да се забрави.

< Yeremiya 23 >