< Yeremiya 22 >
1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
Detta säger Herren: Gack ned i Juda Konungs hus, och tala der detta ordet:
2 ‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
Och säg: Hör Herrans ord, du Juda Konung, som på Davids stol sitter, både du, och dine tjenare, och ditt folk, som igenom dessa portarna ingån;
3 Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
Så säger Herren: Håller rätt och rättviso, Och hjelper den beröfvada utu våldsverkarens hand; och oförrätter icke främlingen, den faderlösa och enkona, och görer ingom öfvervåld, och utgjuter icke oskyldigt; blod i detta rummet.
4 Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
Om I detta gören, så skola Konungarna, som på Davids stol sitta, infara genom desses hus portar, både till vagn och till häst, samt med deras tjenare och folk.
5 Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
Men om I detta, icke hören, så hafver jag svorit vid mig sjelf, säger Herren: Detta hus skall förstördt varda.
6 Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
Ty så säger Herren om Juda Konungs hus: Gilead, du äst mig hufvudet i Libanon; hvad gäller, jag skall göra dig till öde, och städerna utan inbyggare?
7 Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
Ty jag hafver beställt förderfvare öfver dig, hvar och en med sin vapen; de skola omkullhugga, din utvalda cedreträ, och kasta dem i elden.
8 “Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
Så skola månge Hedningar gå framom denna staden, och säga emellan sig: Hvi hafver Herren alltså, handlat med denna stora stadenom?
9 Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
Och man skall svara: Derföre, att de Herrans sins Guds förbund öfvergifvit hafva, och tillbedit andra gudar, och tjent dem.
10 Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
Gråter icke öfver de döda, och grämer eder icke öfver dem; men gråter öfver den der bortfar, och skall aldrig igenkomma, att han sitt fädernesland mer se må.
11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
Ty så säger Herren om Sallum, Josia son, Juda Konungs, som Konung är uti sins faders Josia stad, som utfaren är af detta rum: Han skall intet komma här igen;
12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
Utan måste dö uti det rum, dit han för en fånga förd är, och skall detta land intet mer se.
13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
Ve honom, som uppbygger sitt hus med synd, och sin mak med orätt; den sin nästa för intet arbeta låter, och icke gifver honom sin lön;
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
Och tänker: Nu väl, jag vill bygga mig ett stort hus, och ett vidt palats; och låter hugga sig fenster deruppå, och panelar det med cedreträ, och målar det rödt.
15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Menar du, att du vill vara Konung, efter du prålar med cedreträ? Hafver din fader ock icke ätit och druckit, och blef ändock likväl vid rätt och rättfärdighet; och honom gick väl?
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
Han halp dem elända och fattiga till rätt, och det gick honom väl af. Är icke detta rättsliga känna mig? säger Herren.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
Men din ögon och ditt hjerta stå intet alltså, utan på din girighet, på att utgjuta oskyldigt blod, till att göra öfvervåld och orätt.
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
Derföre säger Herren om Jojakim, Josia son, Juda Konung: Man skall intet begråta honom ( sägandes ): Ack broder, ack syster! Man skall intet begråta honom ( sägandes ): Ack herre, ack ädling!
19 Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
Han skall likasom en åsne begrafven varda, försläpad och utkastad i porten i Jerusalem.
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
Ja, gack ock nu upp på Libanon, och ropa, och låt dig höra i Basan, och ropa af Abarim; ty alle dine älskare äro ömkelige.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
Jag hafver tillförene sagt dig det, då det ännu väl stod med dig; men du sade: Jag vill intet hörat. Alltså hafver du gjort alla dina lifsdagar, att du intet hafver hört mina röst.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
Vädret drifver alla dina herdar, och dine älskare fara bort fångne; der måste du till spott och skam varda, för alla dina ondskos skull.
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
Du som nu i Libanon bor, och hafver din näste i cedreträ, huru skönliga skall du se ut, när dig värk och sveda uppåkommer, såsom ene i barnsnöd?
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
Så sant som jag lefver, säger Herren: Om Chonia, Jojakims son, Juda Konung, vore en signetsring på mine högra hand, så skulle jag ändå rifva dig deraf;
25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
Och gifva dig dem i händer, som efter ditt lif stå, och för hvilkom du dig fruktar, nämliga uti NebucadNezars händer, Konungens i Babel, och de Chaldeers;
26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
Och skall drifva dig, och dina moder, som dig födt hafver, uti ett annat land, der edart fädernesland icke är, och der skolen I dö.
27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
Och uti det land, der de af hjertat gerna igen voro, skola de icke igenkomma.
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
Hvilken en elände, föraktad och fördrifven man är dock Chonia! Ett vanvördt och uselt fat! Ack! huru är han dock, samt med sine säd, fördrifven, och uti ett obekant land kastad!
29 Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
O land, land, land, hör Herrans ord.
30 Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”
Detta säger Herren: Skrifver denna mannen upp för en förderfvad; för en man dem i sina lifsdagar intet lyckas skall; ty han skall icke hafva den lyckona, att någor af hans säd skall sitta på Davids stol, och länger öfver Juda råda.