< Yeremiya 22 >

1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
Itsho njalo iNkosi: Yehlela endlini yenkosi yakoJuda, ukhulume khona lelilizwi,
2 ‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
uthi: Zwana ilizwi leNkosi, wena nkosi yakoJuda, ohlezi esihlalweni sobukhosi sikaDavida, wena, lezinceku zakho, labantu bakho abangena ngalamasango.
3 Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
Itsho njalo iNkosi: Yenzani isahlulelo lokulunga, lophule ophangiweyo esandleni somcindezeli; lingacindezeli, lingenzi udlakela kowezizwe, izintandane, lomfelokazi, njalo lingachithi igazi elingelacala kulindawo.
4 Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
Ngoba uba lisenza linto isibili, khona kuzangena ngamasango alindlu amakhosi ahlalela uDavida esihlalweni sakhe sobukhosi, egade izinqola lamabhiza, yona lenceku zayo labantu bayo.
5 Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
Kodwa uba lingawalaleli lamazwi, ngiyafunga ngami, kutsho iNkosi, ukuthi lindlu izakuba lunxiwa.
6 Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
Ngoba itsho njalo iNkosi mayelana lendlu yenkosi yakoJuda: UyiGileyadi kimi, inhloko yeLebhanoni; isibili ngizakwenza inkangala, imizi engahlalwayo.
7 Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
Ngizakulungisela abachithi, ngulowo elezikhali zakhe; njalo bazagamula ikhethelo lemisedari yakho, bayiphosele emlilweni.
8 “Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
Lezizwe ezinengi zizadlula kulumuzi, zithi, ngulowo kumakhelwane wakhe: INkosi yenzeleni kanje kulumuzi omkhulu?
9 Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
Khona bazakuthi: Ngenxa yokuthi basidelile isivumelwano seNkosi uNkulunkulu wabo, bakhonza abanye onkulunkulu, babasebenzela.
10 Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
Lingamkhaleli ofileyo, lingamlileli; khalelani kakhulu ohambileyo, ngoba kasayikubuya kumbe abone ilizwe lokuzalwa kwakhe.
11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
Ngoba itsho njalo iNkosi mayelana loShaluma indodana kaJosiya, inkosi yakoJuda, owabusa esikhundleni sikaJosiya uyise, owaphuma kulindawo: Kasayikubuya lapha;
12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
kodwa uzafela endaweni abamthumbele kuyo, kasayikulibona lelilizwe.
13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
Maye kowakha indlu yakhe ngokungalungi, lamakamelo akhe aphezulu ngokungaqondanga, osebenzisa umakhelwane wakhe ngeze, angamniki umvuzo wakhe;
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
othi: Ngizazakhela indlu enkulu lamakamelo aphezulu abanzi; azisikele amawindi, yembeswe ngemisedari, iconjwe ngokubomvu.
15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Uzabusa yini, ngoba utshisekela ulaka ugqoke imisedari? Uyihlo kadlanga yini wanatha, wenza isahlulelo lokulunga, kwasekusiba kuhle kuye?
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
Wehlulela udaba lomyanga loswelayo; khona kwaba kuhle. Lokhu kakusikungazi yini? itsho iNkosi.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
Kodwa amehlo akho lenhliziyo yakho kakukho kokunye ngaphandle kwemhawini wakho, lekuchitheni igazi elingelacala, lencindezelweni, lekwenzeni udlakela.
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
Ngakho itsho njalo iNkosi mayelana loJehoyakhimi indodana kaJosiya, inkosi yakoJuda: Kabayikumkhalela besithi: Hawu mfowethu! kumbe: Hawu dadewethu! Kabayikumkhalela besithi: Hawu nkosi! loba: Hawu, bukhosi bakhe!
19 Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
Uzangcwatshwa ngokungcwatshwa kukababhemi, ehudulwa alahlwe ngaphandle kwamasango eJerusalema.
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
Yenyukela eLebhanoni, umemeze, uphakamise ilizwi lakho eBashani, umemeze useAbarimi, ngoba zonke izithandwa zakho zibhujisiwe.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
Ngakhuluma lawe ekonwabeni kwakho, kodwa wathi: Kangiyikulalela. Lokhu bekuyindlela yakho kusukela ebutsheni bakho, ukuthi ungalilaleli ilizwi lami.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
Umoya uzakudla bonke abelusi bakho, lezithandwa zakho zizakuya ekuthunjweni; isibili khona uzakuba lenhloni, uyangeke, ngenxa yobubi bakho bonke.
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
Wena ohlala eLebhanoni, owakhe isidleke phakathi kwemisedari, uzahawukelwa kangakanani ekuzeni kwenhlungu kuwe, ubuhlungu obunjengobowesifazana ohelelwayo.
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
Kuphila kwami, itsho iNkosi, loba uKoniya indodana kaJehoyakhimi, inkosi yakoJuda, ebeyindandatho elophawu esandleni sami sokunene, kanti bengizakuhluthula kuso,
25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
ngikunikele esandleni sabadinga impilo yakho, lesandleni salabo owesaba ubuso babo, ngitsho esandleni sikaNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni, lesandleni samaKhaladiya,
26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
ngikuphosele phandle kanye lonyoko owakubelethayo, liye kwelinye ilizwe, elingazalelwanga kulo; njalo lizafela khona.
27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
Kodwa elizweni abaphakamisa umphefumulo wabo ukubuyela kulo, kabayikubuyela kulo.
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
Lumuntu uKoniya uyisithombe esidelelekayo lesiphahlazekileyo yini? Uyisitsha okungelantokozo kuso yini? Baphoselwani phandle, yena lenzalo yakhe, yebo, bephoselwa elizweni abangalaziyo?
29 Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
Lizwe, lizwe, lizwe, zwana ilizwi leNkosi.
30 Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”
Itsho njalo iNkosi: Bhalani lumuntu ukuthi kalabantwana, umuntu ongayikuphumelela ensukwini zakhe; ngoba kakulamuntu enzalweni yakhe ozaphumelela, ohlezi esihlalweni sobukhosi sikaDavida, esabusa koJuda.

< Yeremiya 22 >