< Yeremiya 22 >
1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
Nanku akutshoyo uThixo: “Hamba wehlele endlini yenkosi yakoJuda umemezele khona ilizwi leli uthi,
2 ‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
‘Zwana ilizwi likaThixo, we nkosi yakoJuda, wena ohlala esihlalweni sobukhosi sikaDavida, wena lezikhulu zakho kanye labantu bakho abangena ngamasango la.
3 Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
UThixo uthi: Yenzani okulungileyo lokuqondileyo. Mhlenge esandleni somncindezeli wakhe lowo ophangiweyo. Lingenzi okubi loba udlakela kowezizweni, intandane loba umfelokazi, njalo lingachithi igazi elingelacala kule indawo.
4 Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
Ngoba nxa linanzelela ukulandela imilayo le, amakhosi ahlala esihlalweni sobukhosi sikaDavida azangena ngamasango ale indawo, egade izinqola zempi lamabhiza, elezikhulu zawo kanye labantu bawo.
5 Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
Kodwa nxa imilayo le lingayilaleli, kutsho uThixo, ngifunga ngami ukuthi indawo le izakuba lunxiwa.’”
6 Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
Ngoba mayelana lendawo yenkosi yakoJuda uThixo uthi: “Lanxa unjengeGiliyadi kimi, lanjengengqongo yeLebhanoni, ngeqiniso ngizakwenza ufane lenkangala, lanjengamadolobho angahlali muntu.
7 Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
Ngizakuthumela abachithi, indoda nganye ilezikhali zayo, njalo bazaquma imijabo yenu emihle yemisedari bayiphosele emlilweni.
8 “Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
Abantu abavela ezizweni ezinengi bazadlula kulelidolobho babuzane besithi, ‘Kungani uThixo enze into enje kulelidolobho elikhulu na?’
9 Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
Impendulo izakuthi: ‘Ngoba basidelile isivumelwano sikaThixo uNkulunkulu wabo bakhonza abanye onkulunkulu njalo babasebenzela.’”
10 Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
Lingayikhaleli inkosi efileyo loba lililele ukulilahlekela kwayo; kodwa, khalelani kakhulu othunjiweyo, ngoba kasayikubuya njalo loba abone ilizwe lakibo futhi.
11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
Ngoba mayelana loShalumi indodana kaJosiya, owangena esikhundleni sikayise esiba yinkosi yakoJuda kodwa osesukile kule indawo: UThixo uthi, “Kasoze abuye futhi.
12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
Uzafela kuleyondawo asiwa kuyo ethunjiwe; ilizwe leli kasoze alibone futhi.”
13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
“Maye kuye owakha indlu yakhe yobukhosi ngokungalungi, lezindlu zakhe zangaphezulu ngokungafanelanga, esenza abantu bakibo basebenzele ize, engabaholisi lutho ngokusebenza kwabo.
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
Uthi, ‘Ngizazakhela indlu enkulu yobukhosi elezitezi ezibanzi.’ Ngakho uyenza ibe lamawindi amakhulu, ayinameke ngemisidari, ayicombe ngokubomvu.
15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Ukuba lemisedari eminenginengi kukwenza ube yinkosi na? Uyihlo kazange abe lokudla lokunathwayo na? Wenza okuqondileyo lokulungileyo, ngakho konke kwamlungela.
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
Wavikela amalungelo abayanga labaswelayo, ngakho konke kwamlungela. Lokho akusikho okutsho ukungazi na?” kutsho uThixo.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
“Kodwa amehlo akho lenhliziyo yakho kukhangele inzuzo yenkohliso, lokuchitha igazi elingelacala, ukuncindezela kanye lodlakela.”
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
Ngakho mayelana loJehoyakhimi indodana kaJosiya, inkosi yakoJuda, uThixo uthi: “Kabayikumkhalela besithi: ‘Maye ngomfowethu! Maye ngodadewethu!’ Kabayikumkhalela besithi: ‘Maye ngenkosi yami! Maye ngobuhle bayo obukhulu!’
19 Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
Uzangcwatshwa njengobabhemi, ahudulwe aphoselwe ngaphandle kwamasango aseJerusalema.”
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
“Qansa uye eLebhanoni umemeze, wenze ilizwi lakho lizwakale eBhashani; memeza use-Abharimi, ngoba bonke abamanyane lawe banqotshiwe.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
Ngakuxwayisa uzibona uvikelekile, kodwa wena wathi, ‘Angiyikulalela!’ Le ibe iyindlela yakho kusukela ebutsheni bakho; kawungilalelanga.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
Umoya uzabaxotshela khatshana bonke abelusi bakho, labamanyene lawe bazathunjwa. Lapho-ke uzayangeka ube lenhloni ngenxa yobubi bakho bonke.
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
Lina abahlala ‘eLebhanoni,’ eligcineke kuhle ezindlini zemisedari, lizabubula kakhulu lapho inhlungu zilehlela, ubuhlungu obunjengowesifazane ehelelwa!”
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
UThixo uthi, “Ngeqiniso njengoba ngikhona, lanxa ngabe wena, Jehoyakhini ndodana kaJehoyakhimi inkosi yakoJuda, wawuyindandatho ebukekayo esandleni sami sokunene, ngangizakukhupha.
25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
Ngizakunikela kulabo abafuna ukukubulala, labo obesabayo, uNebhukhadineza inkosi yaseBhabhiloni lakumaKhaladiya.
26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
Wena kanye lonyoko owakuzalayo ngizaliphosela kwelinye ilizwe, lapho elingazalelwanga khona, lapho elizafela khona lobabili.
27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
Kaliyikuphinda libuye elizweni elifisa ukuza kulo.”
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
Umuntu lo, uJehoyakhini, uyimbiza efileyo, edelelwayo, into engafunwa muntu na? Kungani yena labantwabakhe bezaphoselwa ngaphandle, balahlelwe elizweni abangalaziyo na?
29 Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
Wena lizwe, lizwe, lizwe, zwana ilizwi likaThixo!
30 Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”
UThixo uthi: “Bhalani umuntu lo njengongelabantwana, umuntu ongayikuphumelela empilweni yakhe, ngoba kakho owenzalo yakhe ozaphumelela, kakho ozahlala esihlalweni sobukhosi sikaDavida loba abuse futhi koJuda.”