< Yeremiya 22 >
1 Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
Saa sagde Herren: Gak ned til Judas Konges Hus, og tal der dette Ord,
2 ‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
og sig: Judas Konge, du, som sidder paa Davids Trone, hør Herrens Ord, du og dine Tjenere og dit Folk, som gaa ind ad disse Porte.
3 Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
Saa siger Herren: Øver Ret og Retfærdighed, og redder den, som er bleven til Rov, af Voldsmandens Haand, og forfordeler ej den fremmede, den faderløse og Enken, og gører ikke Uret og udøser ikke uskyldigt Blod paa dette Sted!
4 Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
Thi dersom I rettelig gøre efter dette Ord, da skal der ind ad dette Hus's Porte gaa Konger, som sidde i Davids Sted paa hans Trone, og som fare paa Vogne og paa Heste, han og hans Tjenere og hans Folk.
5 Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
Men dersom I ikke ville høre disse Ord, da har jeg svoret ved mig selv, siger Herren, at dette Hus skal blive til et øde Sted.
6 Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
Thi saa siger Herren om Judas Konges Hus: Du var mig som Gilead, som Libanons Top; men jeg skal sandelig gøre dig til en Ørk, til Stæder, som ikke bebos.
7 Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
Og jeg vil indvie Fordærvere, der skulle komme over dig, hver med sine Vaaben; og de skulle omhugge dine udvalgte Cedre og kaste dem paa Ilden.
8 “Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
Og mange Hedninger skulle gaa forbi denne Stad, og de skulle sige hver til sin Næste: Hvorfor har Herren gjort saaledes ved denne store Stad?
9 Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
Og de skulle sige: Fordi de forlode Herrens, deres Guds, Pagt, og tilbade andre Guder og tjente dem.
10 Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
Græder ikke over den døde, og ynkes ikke over ham; græder bittert over den, som drager bort, thi han skal aldrig komme tilbage og se sit Fædreland.
11 Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
Thi saa har Herren sagt om Sallum, Judas Konge, Josias's Søn, som var Konge i Josias sin Faders Sted, og som drog ud fra dette Sted: Han skal ikke mere komme hid tilbage;
12 Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
men han skal dø paa det Sted, hvorhen de have bortført ham, og han skal ikke mere se dette Land.
13 “Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
Ve den, som bygger sit Hus med Uretfærdighed og sine Sale med Uret, ham, der lader sin Næste tjene for intet, og ikke giver ham hans Arbejdes Løn,
14 Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
ham, der siger: Jeg vil bygge mig et rummeligt Hus og luftige Sale; og som udhugger sig Vinduer og paneler det med Ceder og anstryger det med rødt.
15 “Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
Skulde du være Konge, fordi du brammer med Ceder? har din Fader ikke spist og drukket og øvet Ret og Retfærdighed? da gik det ham vel.
16 Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
Han antog sig den elendiges og den fattiges Sag, da gik det vel til; er dette ikke „at kende mig?‟ siger Herren.
17 “Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
Men dine Øjne og dit Hjerte ere ikke til andet end til din Vinding og til at udøse uskyldigt Blod og til at øve Vold og Undertrykkelse.
18 Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
Derfor, saa siger Herren om Jojakim, Josias's Søn, Kongen i Juda: De skulle ikke sørge over ham, og sige: Ak, min Broder! og ak, Søster! de skulle ikke sørge over ham og sige: Ak, Herre! og ak, hans Herlighed!
19 Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
Han skal begraves som et Asen begraves; man skal slæbe ham bort og kaste ham hen, langt uden for Jerusalems Porte.
20 “Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
Stig op paa Libanon og raab, og opløft din Røst i Basan og raab fra Abarim! thi alle dine Elskere ere knuste.
21 Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
Jeg talte til dig i din Tryghed, men du sagde: Jeg vil ikke høre; dette har været din Vej fra din Ungdom af, at du ikke har villet høre paa min Røst.
22 Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
Alle dine Hyrder skal Vejret fortære, og dine Elskere skulle vandre i Fangenskab; thi da skal du beskæmmes og blive til Skamme for al din Ondskabs Skyld.
23 Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
Du, som bor paa Libanon og bygger Rede i Cedrene, hvor vil du finde Medynk, naar Smerter komme paa dig, Pine som hendes, der føder?
24 “Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
Saa sandt jeg lever, siger Herren, var end Konias, Jojakims, Judas Konges Søn, en Signetring paa min højre Haand, saa vilde jeg dog rive dig bort derfra.
25 Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
Og jeg vil give dig i deres Haand, som tragte efter dit Liv, og i deres Haand, for hvis Ansigt du gruer, og i Nebukadnezar, Kongen af Babels Haand og i Kaldæernes Haand.
26 Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
Og jeg vil kaste dig og din Moder, som dig fødte, ud i et andet Land, hvor I ikke ere fødte, og der skulle I dø.
27 Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
Men til det Land, hvorhen deres Sjæl længes efter at komme tilbage, derhen skulle de ikke komme tilbage.
28 Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
Mon denne Mand, Konias, er et foragtet, sønderslaaet Billede? mon han er et Kar, som ingen har Lyst til? hvorfor ere de bortkastede, han og hans Sæd, ja, henkastede i et Land, som de ikke kende?
29 Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
Land! Land! Land! hør Herrens Ord!
30 Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”
Saa siger Herren: Indtegner denne Mand som barnløs som en Mand, der ikke skal have Lykke i sine Dage; thi ingen af hans Sæd skal have Lykke ved at sidde paa Davids Trone og herske fremdeles i Juda.