< Yeremiya 21 >

1 Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya.
Ilizwi elafika kuJeremiya livela eNkosini lapho inkosi uZedekhiya ethuma kuye uPashuri indodana kaMalikiya, loZefaniya indodana kaMahaseya, umpristi, isithi:
2 Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.”
Ake usibuzele eNkosini, ngoba uNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni ulwa emelene lathi; mhlawumbe iNkosi ingasenzela njengokwezimangaliso zayo zonke, ukuze enyuke asuke kithi.
3 Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti,
UJeremiya wasesithi kubo: Lizakutsho njalo kuZedekhiya:
4 ‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu.
Itsho njalo iNkosi uNkulunkulu kaIsrayeli: Khangelani, ngizaphendulela emuva izikhali zempi ezisezandleni zenu, elilwa ngazo lenkosi yeBhabhiloni lamaKhaladiya, abalivimbezeleyo ngaphandle komduli, ngibaqoqe ngaphakathi kwalumuzi.
5 Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali.
Njalo mina ngizakulwa lani ngesandla eseluliweyo, langengalo elamandla, langentukuthelo, langokufutheka, langolaka olukhulu.
6 Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa.
Njalo ngizatshaya abakhileyo balumuzi, umuntu kanye lesifuyo; bazakufa ngomatshayabhuqe wesifo omkhulu.
7 Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’
Kuthi emva kwalokhu, itsho iNkosi, uZedekhiya inkosi yakoJuda, lenceku zakhe, labantu, labaseleyo phakathi kwalumuzi kumatshayabhuqe wesifo, enkembeni, lendlaleni, ngizabanikela esandleni sikaNebhukadirezari inkosi yeBhabhiloni, lesandleni sezitha zabo, lesandleni salabo abadinga impilo yabo. Njalo uzabatshaya ngobukhali benkemba; kayikubayekela, kayikuhawukela, kayikuba lomusa.
8 “Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa.
Njalo kulababantu uzakuthi: Itsho njalo INkosi: Khangelani, ngibeka phambi kwenu indlela yokuphila lendlela yokufa.
9 Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka.
Osala kulumuzi uzakufa ngenkemba langendlala langomatshayabhuqe wesifo; kodwa ophumayo, awele kumaKhaladiya alivimbezelayo, uzaphila, lempilo yakhe izakuba yimpango kuye.
10 Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto.
Ngoba ngimisile ubuso bami bumelene lalumuzi ngokubi, hatshi ngokuhle, itsho iNkosi; uzanikelwa esandleni senkosi yeBhabhiloni, iwutshise ngomlilo.
11 “Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova;
Lamayelana lendlu yenkosi yakoJuda, zwanini ilizwi leNkosi:
12 inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti, “‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse; pulumutsani mʼdzanja la wozunza aliyense amene walandidwa katundu wake, kuopa kuti ukali wanga ungabuke ndi kuyaka ngati moto wosazimitsika chifukwa cha zoyipa zimene mwachita.
Wena ndlu kaDavida, itsho njalo INkosi: Yehlulelani isahlulelo ekuseni, lophule ophangiweyo esandleni somcindezeli, hlezi ulaka lwami luphume njengomlilo, lutshise, ukuthi kungabi khona ocitshayo, ngenxa yobubi bezenzo zenu.
13 Ndidzalimbana nanu, inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa, inu okhala ngati thanthwe lapachidikha, akutero Yehova. Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe? Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’
Khangela, ngimelene lawe, wena mhlali wesigodi, dwala legceke, itsho iNkosi; lina elithi: Ngubani ozakwehla amelane lathi? Kumbe ngubani ozangena endaweni zethu zokuhlala?
14 Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu, akutero Yehova. Ndidzatentha nkhalango zanu; moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’”
Kodwa ngizalijezisa njengokwesithelo sezenzo zenu, itsho iNkosi, ngiphembe umlilo ehlathini lakho, ozaqeda konke inhlangothi zonke zakho.

< Yeremiya 21 >