< Yeremiya 21 >
1 Mfumu Zedekiya inatuma Pasuri mwana wa Malikiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa Yeremiya.
The word which came unto Jeremiah from the Lord, when king Zedekiah sent unto him Pashchur the son of Malkiyah, and Zephanyah the son of Ma'asseyah the priest, saying,
2 Iwo amati akanene kwa Yeremiya mawu akuti, “Tinenere kwa Yehova chifukwa Nebukadinezara mfumu ya Babuloni akutithira nkhondo. Mwina mwake Yehova nʼkutichitira zodabwitsa kuti Nebukadinezarayo achoke kwathu kuno.”
Inquire, I pray thee, in our behalf of the Lord; for Nebuchadrezzar the king of Babylon maketh war against us; peradventure the Lord will deal with us according to all his wondrous deeds, so that he may withdraw from us.
3 Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti,
Then said Jeremiah unto them, Thus shall ye say to Zedekiah:
4 ‘Yehova, Mulungu wa Israeli akuti ndikulandeni zida zimene zili mʼmanja mwanu zimene mukugwiritsa ntchito polimbana ndi mfumu ya ku Babuloni ndi ankhondo ake amene akuzingani kunja kwa lingali. Ndipo ndidzasonkhanitsa zidazo mʼkati mwa mzindawu.
Thus hath said the Lord the God of Israel, Behold, I will turn back the weapons of war that are in your hands, wherewith ye fight against the king of Babylon, and against the Chaldeans, who besiege you without the walls, and I will assemble them into the midst of this city.
5 Ineyo mwini wakene ndi mkono wotambasula ndi dzanja lamphamvu, ndidzachita nanu nkhondo ndili wokwiya, wokalipa ndi waukali.
And I myself will fight against you with an outstretched hand and with a strong arm, and in anger, and in fury, and in great wrath.
6 Ndidzakantha amene amakhala mu mzinda muno, anthu pamodzi ndi zirombo, ndipo zidzafa ndi mliri woopsa.
And I will smite the inhabitants of this city, both man and beast: of a great pestilence shall they die.
7 Pambuyo pake, ndidzapereka Zedekiya mfumu ya ku Yuda, nduna zake pamodzi ndi anthu a mu mzinda muno amene adzapulumuke pa nthawi ya mliri, lupanga ndi njala kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni ndi kwa adani awo amene ankafuna kuwapha. Iye adzawapha ndi lupanga. Sadzawachitira chifundo kapena kuwamvera chisoni kapenanso kuwakomera mtima.’
And afterward, saith the Lord, will I give up Zedekiah the king of Judah, and his servants, and the people, and those that are left in this city from the pestilence, from the sword, and from the famine, into the hand of Nebuchadrezzar the king of Babylon, and into the hand of their enemies, and into the hand of those that seek their life: and he shall smite them with the edge of the sword; he will not spare them, nor have pity, nor have mercy.
8 “Yehova anati ndiwawuzenso anthu amenewa kuti asankhe pakati pa moyo ndi imfa.
And unto this people shalt thou say, Thus hath said the Lord, Behold, I set before you the way of life, and the way of death.
9 Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzaphedwa ndi lupanga, njala kapena mliri. Koma aliyense amene apite kukadzipereka kwa Ababuloni amene akuzinganiwa adzakhala ndi moyo, adzapulumuka.
He that remaineth in this city shall die by the sword, or by the famine, or by the pestilence; but he that goeth out, and runneth away to the Chaldeans that besiege you, shall remain alive, and his life shall be unto him as a booty.
10 Ine ndatsimikiza kuchitira mzinda uno choyipa osati chabwino, akutero Yehova. Udzaperekedwa mʼdzanja la mfumu ya ku Babuloni, ndipo iyeyo adzawutentha ndi moto.
For I have set my face against this city for evil, and not for good, saith the Lord: into the hand of the king of Babylon shall it be given up, and he will burn it with fire.
11 “Komanso, uwuze banja laufumu la Yuda kuti, ‘Imva mawu a Yehova;
And to the house of the king of Judah [say], Hear ye the word of the Lord:
12 inu a mʼbanja la Davide, Yehova akuti, “‘Weruzani mwachilungamo mmawa uliwonse; pulumutsani mʼdzanja la wozunza aliyense amene walandidwa katundu wake, kuopa kuti ukali wanga ungabuke ndi kuyaka ngati moto wosazimitsika chifukwa cha zoyipa zimene mwachita.
O house of David, thus hath said the Lord, Exercise justice on [every] morning, and deliver him that is robbed out of the hand of the oppressor; lest my fury go forth like fire, and burn so that none can quench it, because of the evil of your doings.
13 Ndidzalimbana nanu, inu amene mukukhala pamwamba pa chigwa, inu okhala ngati thanthwe lapachidikha, akutero Yehova. Inu amene mumanena kuti, ‘Ndani amene angabwere kudzalimbana nafe? Ndani amene angathe kulowa mʼmalinga mwathu?’
Behold, I am against thee, O inhabitress of the valley, [about] the rock of the plain, saith the Lord; who say, Who shall descend down against us? or who shall enter into our habitations?
14 Ndidzakulangani molingana ndi ntchito zanu, akutero Yehova. Ndidzatentha nkhalango zanu; moto udzapsereza zonse zimene zakuzungulirani.’”
But I will inflict punishment on you according to the fruit of your doings, saith the Lord: and I will kindle a fire in its forest, and it shall devour all its environs.