< Yeremiya 20 >

1 Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
Men då Pashur, Immers son, Prestens, den för en öfversta i Herrans hus satt var, hörde Jeremia prophetera dessa orden,
2 Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
Slog han Propheten Jeremia, och kastade honom i fängelse, i den öfra portenom BenJamins, hvilken på Herrans huse är.
3 Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
Och då morgonen kom, tog Pashur Jeremia åter utu fängelset. Då sade Jeremia till honom: Herren kallar dig icke Pashur, utan Magor allt omkring.
4 Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
Ty så säger Herren: Si, jag skall gifva dig, samt med alla dina vänner, uti en fruktan, och de skola falla genom dina fiendars svärd; det skall du se med din ögon; och jag skall öfvergifva hela Juda uti Konungens hand af Babel; han skall föra dem bort till Babel, och dräpa dem med svärd.
5 Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
Och jag skall gifva allt godset i denna staden, samt med allt hans arbete och alla klenodier, alla Juda Konungars håfvor, uti deras fiendars hand, så att de skola dem skinna, borttaga och till Babel föra.
6 Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
Och du, Pashur, skall med allt ditt husfolk gå fången, och till Babel komma; der skall du dö, och begrafven varda, samt med alla dina vänner, hvilkom du lögn predikar.
7 Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
Herre, du hafver dragit mig, och jag hafver mig draga låtit; du hafver varit mig för stark, och hafver vunnit; men jag är deröfver kommen till spott dagliga, och hvar man gör gäck af mig.
8 Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
Ty sedan jag talat, ropat och predikat hafver om den plågan och förderfvet, är mig Herrans ord vordet till hån och spott dagliga.
9 Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
Då föll mig i sinnet: Jag vill intet mer tänka uppå honom, och intet mer predika i hans Namn; men i mino hjerta och minom benom vardt lika som en brinnande eld insluten, så att jag icke förmådde det lida, och var hardt när förgången.
10 Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
Ty jag hörer, huru månge banna mig, och jag måste allestäds vara rädder. Anklager, vi vilje anklaga honom, säga alle mine vänner och stallbröder; om vi kunne blifva honom öfvermägtige, och komma åt honom, och hämnas öfver honom.
11 Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
Men Herren är med mig, såsom en stark hjelte; derföre skola mine förföljare falla, och icke vinna, utan skola på stor skam komma, derföre att de så dårliga handla; evig skall den skammen vara, och skall icke förgäten varda.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
Och nu, Herre Zebaoth, du som pröfvar de rättfärdiga, och ser njurar och hjerta, låt mig se dina hämnd öfver dem; ty jag hafver befallt dig min sak.
13 Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
Sjunger Herranom, lofver Herran, som hjelper dens fattigas lif utu de ondas händer.
14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
Förbannad vare den dag, der jag uti född var; den dagen vare osignad, på hvilkom min moder mig födt hafver.
15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
Förbannad vare den som minom fader god tidende bar, och sade: Du hafver fått en ungan son, på det han skulle glädja honom.
16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
Den mannen vare såsom de städer som Herren omvände, och honom det intet ångrade; han höre ett skriande om morgonen, och om middagen ett jämrande.
17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
Att du dock icke hafver dräpit mig i moderlifvena; att min moder måtte varit min graf, och hennes lif måtte evinnerliga hafvandes varit!
18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?
Hvi är jag dock utu moderlifvena framkommen, att jag sådana jämmer och hjertans sorg se måste, och slita mina dagar med skam?

< Yeremiya 20 >