< Yeremiya 20 >

1 Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
Et Phassur, le prêtre, fils d’Emmer, qui avait été établi prince dans la maison du Seigneur, entendit Jérémie prophétisant ces choses.
2 Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
Et Phassur frappa Jérémie, le prophète, et le jeta dans la prison qui était à la porte haute de Benjamin, dans la maison du Seigneur.
3 Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
Et lorsque le jour eut paru le lendemain, Phassur fit sortir Jérémie de prison, et Jérémie lui dit: Le Seigneur n’appelle plus ton nom, Phassur, mais l’épouvante de toutes parts.
4 Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
Parce que voici ce que dit le Seigneur: Voilà que moi, je te livrerai à l’épouvante, toi et tous tes amis; et ils tomberont sous le glaive de leurs ennemis, et tes yeux le verront; et tout Juda, je le livrerai à la main du roi de Babylone; et il les transportera à Babylone, et il les frappera par le glaive.
5 Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
Et je livrerai toutes les richesses de cette cité; et tout son travail, et tout ce qu’elle a de précieux, et tous les trésors des rois de Juda, je les livrerai à la main de leurs ennemis; et ceux-ci les arracheront, les enlèveront, et les conduiront à Babylone.
6 Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
Mais toi, Phassur, et tous les habitants de ta maison, vous irez en captivité; et tu viendras à Babylone, et là tu mourras, et là tu seras enseveli, toi et tous tes amis à qui tu as prophétisé le mensonge.
7 Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
Vous m’avez séduit. Seigneur, et j’ai été séduit; vous avez été plus fort, et vous avez prévalu; je suis devenu un objet de dérision durant tout le jour; et tous me raillent.
8 Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
Parce que déjà depuis longtemps je parle, criant contre l’iniquité, et annonçant à grand bruit une désolation, et la parole du Seigneur est devenue pour moi un sujet d’opprobre et de dérision durant tout le jour.
9 Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
Et j’ai dit: Je ne ferai pas mention de lui, et je ne parlerai plus en son nom; et alors il s’est allumé dans mon cœur comme un feu ardent, et renfermé dans mes os; et j’ai défailli, ne pouvant le soutenir.
10 Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
Car j’ai entendu les outrages d’un grand nombre et la terreur tout autour de moi. Poursuivez-le, et nous le poursuivrons; j’ai entendu aussi de tous les hommes qui vivaient en paix avec moi, et qui se tenaient à mes côtés: Si en quelque manière il était trompé, et que nous prévalions contre lui, et que nous tirions vengeance de lui.
11 Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
Mais le Seigneur est avec moi comme un guerrier vaillant; c’est pour cela que ceux qui me persécutent tomberont et seront sans force; ils seront confondus grandement, parce qu’ils n’ont pas compris un opprobre éternel qui ne s’effacera jamais.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
Et vous. Seigneur des armées, vous qui éprouvez le juste, et qui voyez les reins et les cœurs; que je voie, je vous prie, la vengeance que vous tirerez d’eux, car à vous j’ai révélé ma cause.
13 Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
Chantez le Seigneur, louez le Seigneur, parce qu’il a délivré l’âme d’un pauvre de la main des méchants.
14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
Maudit le jour auquel je suis né! que le jour auquel m’a enfanté ma mère ne soit pas béni!
15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
Maudit l’homme qui Va annoncé à mon père, disant: Un enfant mâle t’est né, et qui l’a comme rempli de joie!
16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
Que cet homme soit comme sont les cités qu’a détruites le Seigneur, sans qu’il s’en soit repenti; qu’il entende des clameurs le matin, et des hurlements à l’heure de midi;
17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
Lui qui ne m’a pas tué avant ma naissance; en sorte que ma mère devînt mon sépulcre, et que sa grossesse fût éternelle,
18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?
Pourquoi suis-je sorti du sein de ma mère pour voir le travail et la douleur, et pour que mes jours fussent consumés dans la confusion?

< Yeremiya 20 >